Yuda 1 – CCL & PCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yuda 1:1-25

1Ndine Yuda, mtumiki wa Yesu Khristu, komanso mʼbale wake wa Yakobo.

Kwa inu amene Mulungu Atate anakuyitanani, amene amakukondani ndikukusungani mwa Yesu Khristu.

2Chifundo, mtendere ndi chikondi zikhale nanu mochuluka.

Tchimo ndi Kuwonongeka kwa Osapembedza

3Okondedwa, ngakhale ndinkafunitsitsa kukulemberani za chipulumutso cha tonsefe, ndakakamizidwa kuti ndikulembereni ndi kukupemphani kolimba kuti mumenye ndithu nkhondo yotchinjiriza chikhulupiriro chimene Mulungu anachipereka kamodzi kokha kwa anthu onse oyera mtima. 4Pakuti anthu ena amene za chilango chawo zinalembedwa kale, alowa mobisika pakati panu. Amenewa ndi anthu osapembedza Mulungu, amene amapotoza chisomo cha Mulungu wathu kuchisandutsa ufulu ochitira zonyansa ndiponso amakana Yesu Khristu amene Iye ndiye Mbuye ndi Mfumu yathu.

5Ngakhale munazidziwa kale zonsezi, ndafuna kuti ndikukumbutseni kuti Ambuye anapulumutsa anthu ake ndi kuwatulutsa mʼdziko la Igupto, koma pambuyo pake anawononga amene sanakhulupirire. 6Ndipo mukumbukire angelo amene sanakhutire ndi maudindo awo, koma anasiya malo awo. Angelo amenewa Mulungu anawamanga ndi maunyolo osatha, ndipo akuwasunga mʼmalo a mdima mpaka tsiku lalikulu lachiweruzo. 7Musayiwale mizinda ya Sodomu ndi Gomora ija, ndi mizinda yoyandikana nayo. Anthu mʼmenemo anadziperekanso kuchita zadama ndi kuchita zonyansa zachilendo. Mizinda imeneyi yakhala ngati chitsanzo cha amene adzalangidwa ndi moto wosatha.

8Nʼchimodzimodzinso zimene akuchita anthu amenewa potsata maloto awo, amadetsa matupi awo, amakana ulamuliro wa Mulungu ndiponso amachitira chipongwe angelo akumwamba. 9Koma ngakhale mkulu wa angelo Mikayeli, pamene ankalimbana ndi Mdierekezi za mtembo wa Mose, sanamunene kuti wachipongwe, koma anati, “Ambuye akudzudzule iwe!” 10Koma anthu awa amachita chipongwe zinthu zimene sakuzidziwa. Ndipo zinthu zimene amazidziwa ndi nzeru zachibadwa, monga za nyama, ndizo zimene zimawawononga.

11Tsoka kwa iwo chifukwa anatsatira njira ya Kaini. Iwo athamangira phindu, nʼchifukwa chake anagwa mʼtchimo la Baalamu. Iwo anawonongedwa chifukwa chowukira monga anachitira Kora.

12Anthu amenewa ndiwo amayipitsa maphwando anu achikondi. Amadya nanu mopanda manyazi ndipo ali ngati abusa amene amangodzidyetsa okha. Anthuwa ali ngati mitambo yowuluzika ndi mphepo, yopanda mvula. Ali ngati mitengo ya nthawi ya masika, yopanda zipatso, yozuka mizu, mitengo yoferatu. 13Iwowa ali ngati mafunde awukali apanyanja, amene amatulutsa thovu la zonyansa zawo. Amenewa ali ngati nyenyezi zosochera, ndipo Mulungu akuwasungira mdima wandiweyani mpaka muyaya.

14Enoki, wachisanu ndi chiwiri kuyambira pa Adamu, ananeneratu za anthu amenewa kuti, “Onani, Ambuye akubwera ndi oyera ake osawerengeka 15kuti adzaweruze aliyense, ndi kudzagamula kuti onse osapembedza ndi olakwa, chifukwa cha ntchito zawo zosalungama zimene anachita mʼmoyo wawo osaopa Mulungu. Adzawatsutsa chifukwa cha mawu onse achipongwe amene osapembedzawa ananyoza nawo Ambuye.” 16Anthu amenewa amangʼungʼudza ndi kudandaula. Amatsatira zilakolako zawo zoyipa. Amayankhula zodzitamandira ndipo amanamiza ena pofuna kupeza phindu.

Awalimbikitsa kuti Apirire

17Koma okondedwa, kumbukirani zimene atumwi a Ambuye athu Yesu Khristu ananeneratu. 18Iwo anakuwuzani kuti, “Mʼmasiku otsiriza kudzafika anthu onyoza, otsatira zofuna zawo zoyipa.” 19Anthu amenewa ndi amene akubweretsa mipatuko pakati panu, amatsatira nzeru zachibadwa ndipo alibe Mzimu Woyera.

20Koma inu okondedwa, muthandizane kuti mukule pa chikhulupiriro chanu choyera, ndipo muzipemphera ndi mphamvu ya Mzimu Woyera. 21Khalani mʼchikondi cha Mulungu pamene mukudikira chifundo cha Ambuye athu Yesu Khristu kuti akubweretsereni moyo wosatha.

22Muwachitire chifundo amene akukayika. 23Ena muwapulumutse powalanditsa ku moto. Enanso muwachitire chifundo, koma mwa mantha, ndipo muzidana ngakhale ndi mwinjiro yomwe yayipitsidwa ndi machimo.

Mawu Olemekeza Mulungu

24Kwa Iye amene angathe kukusungani kuti mungagwe mʼmachimo, ndiponso amene angathenso kukufikitsani pamaso pake pa ulemerero wopanda cholakwa muli okondwa, 25kwa Mulungu yekhayo, Mpulumutsi wathu, kwa Iye kukhale ulemerero, ukulu, mphamvu ndi ulamuliro, mwa Yesu Khristu Ambuye athu, kuyambira isanayambe nthawi, tsopano mpaka muyaya. Ameni.

Persian Contemporary Bible

يهودا 1:1-25

سلام و درود از يهودا

1از طرف «يهودا»، خدمتگزار عيسی مسيح و برادر يعقوب،

به مسيحيانی كه محبوب و برگزيدهٔ خدای پدر هستند و در عيسی مسيح محفوظ می‌باشند.

2از درگاه خدا، برای شما طالب رحمت و آرامش و محبت روزافزون می‌باشم.

گناه و هلاكت بی‌دينان

3ای عزيزان، در نظر داشتم دربارهٔ نجاتی كه خداوند به ما عطا فرموده، مطالبی برايتان بنويسم. اما اكنون لازم می‌بينم، مطلب ديگری به جای آن بنويسم تا شما را ترغيب نمايم از آن حقيقتی كه خدا يكبار برای هميشه به مقدسين خود عطا كرد، با جديت تمام دفاع كنيد. 4زيرا عده‌ای خدانشناس با نيرنگ وارد كليسا شده‌اند و تعليم می‌دهند كه ما پس از مسيحی شدن، می‌توانيم هر چه دلمان می‌خواهد انجام دهيم بدون آنكه از مجازات الهی بترسيم. عاقبت هولناک اين معلمين دروغين و گمراه از مدتها پيش تعيين شده است، زيرا با سرور و خداوند يگانهٔ ما عيسی مسيح، سر به مخالفت برداشته‌اند.

5گرچه اين حقايق را به خوبی می‌دانيد، اما می‌خواهم برخی نكات را بار ديگر يادآوری نمايم. همانگونه كه می‌دانيد، خداوند پس از آنكه قوم اسرائيل را از سرزمين مصر رهايی بخشيد، تمام كسانی را كه بی‌ايمان شده بودند و از خدا سرپيچی می‌كردند، هلاک ساخت. 6همچنين يادآوری می‌كنم كه خدا فرشتگانی را كه زمانی پاک و مقدس بودند، ولی خود را به گناه آلوده ساختند، در تاريكی مطلق محبوس فرموده تا روز داوری فرا برسد. 7در ضمن، شهرهای «سدوم» و «عموره» را نيز به ياد داشته باشيد. اهالی آنجا و شهرهای مجاور، به انواع شهوات و انحرافات جنسی آلوده بودند. بنابراين، همهٔ آنها نابود شدند تا برای ما درس عبرتی باشند و بدانيم كه آتش ابدی وجود دارد كه در آنجا گناهكاران مجازات می‌شوند.

8با وجود همهٔ اينها، اين معلمين گمراه به زندگی فاسد و بی‌بند و بار خود ادامه می‌دهند، و بدن خود را آلوده می‌سازند؛ در ضمن مطيع هيچ مرجع قدرتی نيز نيستند و موجودات آسمانی را به باد مسخره می‌گيرند. 9در حالی که «ميكائيل»، رئيس فرشتگان، وقتی با شيطان بر سر جسد موسی بحث می‌كرد، به خود اجازه نداد به او تهمت بزند و اهانت كند؛ بلكه فقط گفت: «خداوند تو را توبيخ فرمايد!» 10اما اين اشخاص هر چه را كه نمی‌فهمند مسخره می‌كنند و ناسزا می‌گويند؛ ايشان همچون حيوانات بی‌فهم، دست به هر كاری كه دلشان می‌خواهد می‌زنند، و به اين ترتيب، به سوی نابودی و هلاكت می‌شتابند.

11وای به حال آنان، زيرا از «قائن» سرمشق می‌گيرند كه برادرش را كشت؛ مانند «بلعام» رفتار می‌كنند كه به خاطر پول، دست به هر كاری می‌زد؛ مانند «قورح» عمل می‌كنند كه از دستور خدا سرپيچی كرد. به همين دليل، دچار لعنت الهی شده، هلاک خواهند شد.

12اين اشخاص كه در ضيافتهای كليسايی، به جمع شما می‌پيوندند، لكه‌های ناپاكی هستند كه شما را آلوده می‌كنند. با بی‌شرمی می‌خندند و شكم خود را سير می‌كنند، بدون آنكه رعايت حال ديگران را بنمايند. همچون ابرهايی هستند كه از زمينهای خشک عبور می‌كنند، بدون آنكه قطره‌ای باران ببارانند. قولهای آنان اعتباری ندارد. درختانی هستند كه در موسم ميوه، ثمر نمی‌دهند. اينان دو بار طعم مرگ را چشيده‌اند؛ يک بار زمانی كه در گناه بودند، و بار ديگر وقتی از مسيح روگردان شدند. از این رو، بايد منتظر داوری خدا باشند. 13تنها چيزی كه از خود برجای می‌گذارند، ننگ و رسوايی است، درست مانند كف ناپاک دريا كه از موجهای خروشان بر ساحل باقی می‌ماند. درخشان همچون ستارگان، اما سرگردان هستند و به سوی ظلمت و تاريكی ابدی می‌شتابند.

14«خنوخ» كه هفت نسل بعد از حضرت آدم زندگی می‌كرد، از وضع اين افراد آگاه بود و فرمود: «بنگريد، خداوند با هزاران هزار از مقدسين خود می‌آيد، 15و مردم دنيا را داوری می‌فرمايد، تا مشخص شود چه اعمال وحشتناكی برخلاف خواست خدا انجام داده‌اند و چه سخنان زشتی عليه او گفته‌اند؛ آنگاه ايشان را به سزای اعمالشان خواهد رساند.» 16ايشان دائماً گله و شكايت می‌كنند و هرگز به چيزی قانع نيستند. هر كار زشتی كه به فكرشان خطور كند، انجام می‌دهند؛ جسور و خودنما هستند و فقط به كسی احترام می‌گذارند كه بدانند سودی از او عايدشان می‌شود.

دعوت به پايداری

17ای عزيزان، سخنان رسولان خداوند ما عيسی مسيح را به ياد آوريد. 18ايشان می‌گفتند كه در زمانهای آخر اشخاصی پيدا خواهند شد كه مطابق اميال ناپاک خود رفتار خواهند كرد و حقيقت را مسخره خواهند نمود. 19همين اشخاصند كه بين شما تفرقه و جدايی ايجاد می‌كنند. آنان فقط به دنبال هوسهای خود هستند و روح خدا در وجود ايشان ساكن نيست.

20اما شما ای عزيزان، زندگی خود را بر پايهٔ ايمان بنا نماييد، و به ياری روح‌القدس عبادت كنيد. 21به محبتی كه خدا در حق شما كرده، وفادار بمانيد و با صبر منتظر آن زندگی جاودان باشيد كه خداوند ما عيسی مسيح، از روی رحمت خود به شما عنايت خواهد فرمود. 22به كمک كسانی بشتابيد كه در ترديد به سر می‌برند، تا بر شک خود غلبه كنند. 23گمراهان را از آتش مجازات رهايی دهيد، اما مراقب باشيد كه خودتان نيز به سوی گناه كشيده نشويد. در همان حال كه دلتان بر اين گناهكاران می‌سوزد، از اعمال گناه‌آلود ايشان متنفر باشيد.

دعای تجليل

24‏-25تمام جلال و عزت، برازندهٔ خدای يگانه‌ای است كه بوسيلهٔ خداوند ما عيسی مسيح ما را نجات می‌دهد. بلی، شكوه و عظمت و تمام قدرت و اقتدار از ازل تا به ابد از آن خداوند باد كه قادر است شما را از لغزش و سقوط محفوظ دارد و بی‌عيب و بی‌گناه، با شادی عظيم در پيشگاه باشكوه خود حاضر سازد. آمين.