Yoweli 3 – CCL & OL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

O Livro

Joel 3:1-21

As nações serão julgadas

1Nesse tempo, restaurarei a prosperidade de Judá e de Jerusalém. 2Reunirei os exércitos do mundo no vale onde o Senhor julga, o vale de Jeosafá, e ali os castigarei por terem ferido o meu povo, por terem feito com que a minha possessão se tivesse espalhado entre as nações e por terem dividido entre si a minha terra. 3Dispuseram do meu povo como escravos; deram um rapaz em troca duma meretriz e uma rapariga em troca de vinho bastante para se embriagarem.

4Atenção, Tiro e Sídon, não tentem interferir! Estão a tentar vingar-se de mim, cidades da Filisteia? Cuidado! Em breve farei cair sobre as vossas cabeças a recompensa que merecem. 5Vocês levaram a minha prata e o meu ouro, assim como todos os tesouros preciosos que me pertenciam; levaram tudo para os vossos templos pagãos. 6Venderam o povo de Judá e Jerusalém aos gregos, que os levaram para longe, para as suas terras. 7Mas vou trazê-los de novo desses sítios para onde os venderam e dar-vos-ei a paga de tudo o que fizeram. 8Venderei os vossos filhos e filhas ao povo de Judá, que por sua vez os venderão aos sabeus, nação remota.” Trata-se duma promessa que o Senhor dá.

Bênçãos para o povo do Senhor

9Anuncia longe e perto: Aprontem-se para a guerra! Alistem os vossos melhores guerreiros! Façam a listagem de todas as armas que possuem! 10Forjem espadas das vossas enxadas e lanças das foices. Diga o fraco: “Sou forte!” 11Juntem-se e venham, povos de toda a parte!

E agora, Senhor, faz descer ali os teus valentes.

12“Convoca as nações e trá-las ao vale de Jeosafá, porque será ali que pronunciarei a sentença sobre todos eles. 13Que a foice seja lançada! A seara está madura. Pisem nos lagares, pois estão repletos da maldade destes homens.”

14Multidões e multidões esperam neste vale, o vale da Decisão! Porque o dia do Senhor está perto! Será no vale da Decisão! 15O Sol e a Lua escurecerão e as estrelas apagarão a sua luz. 16O Senhor clama desde Sião e levantará a sua voz em Jerusalém; a Terra e os céus começam a tremer. Contudo, para este povo de Israel o Senhor será bom. Ele é o seu refúgio e a sua força.

17Então saberão, enfim, que eu sou o Senhor, vosso Deus, em Sião, no meu santo monte. Jerusalém será de novo santa. Virá o tempo em que nenhum exército estrangeiro a atravessará.

18Escorrerá mosto das montanhas e leite das colinas. Os rios já secos de Judá encher-se-ão de água e jorrará água do templo do Senhor que regará o vale de Sitim. 19O Egito será destruído e Edom também, por causa da sua violência contra os judeus, pois mataram gente inocente na sua própria terra.

20Contudo, Israel prosperará para sempre e Jerusalém permanecerá de geração em geração. 21Porque purificarei a sua culpa dos crimes que eu ainda não tinha perdoado. E o Senhor habitará em Sião!