Yoweli 3 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 3:1-21

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

1“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,

nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,

2ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse

ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.

Kumeneko ndidzawaweruza

chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,

pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu

ndikugawa dziko langa.

3Anagawana anthu anga pochita maere

ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;

anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo

kuti iwo amwe.

4“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. 5Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. 6Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

7“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. 8Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

9Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:

Konzekerani nkhondo!

Dzutsani ankhondo amphamvu!

Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.

10Sulani makasu anu kuti akhale malupanga

ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.

Munthu wofowoka anene kuti,

“Ndine wamphamvu!”

11Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,

ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12“Mitundu ya anthu idzuke;

ipite ku Chigwa cha Yehosafati,

pakuti kumeneko Ine ndidzakhala

ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.

13Tengani chikwakwa chodulira tirigu,

pakuti mbewu zakhwima.

Bwerani dzapondeni mphesa,

pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza

ndipo mitsuko ikusefukira;

kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,

mʼchigwa cha chiweruzo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira

mʼchigwa cha chiweruzo.

15Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,

ndipo nyenyezi sizidzawalanso.

16Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni

ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;

dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.

Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,

linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,

ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.

Yerusalemu adzakhala wopatulika;

alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,

ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;

mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.

Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova

ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.

19Koma Igupto adzasanduka bwinja,

Edomu adzasanduka chipululu,

chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda

mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.

20Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya

ndi Yerusalemu ku mibadomibado.

21Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke

ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

约珥书 3:1-21

上帝要审判万国

1“到那日,在我复兴犹大耶路撒冷的时候, 2我要聚集万国,带他们下到约沙法3:2 约沙法”意思是“耶和华审判”。谷,在那里审判他们,因为他们把我的子民,就是我的产业以色列,分散到各国,并瓜分我的土地。 3他们抽签分了我的子民,将男童换妓女,卖女童买酒喝。

4泰尔西顿非利士境内所有的人啊,你们为什么这样对我?你们要报复我吗?如果你们是报复我,我必速速使你们遭报应。 5你们夺去我的金银,抢走我的珍宝,拿去放在你们的庙中, 6并把犹大耶路撒冷的居民卖给希腊人,使他们远离家乡。 7然而,他们被卖到哪里,我要从哪里把他们带回来,并要使你们得到报应, 8我要把你们的儿女卖给犹大人,犹大人必把他们卖给远方的示巴人。这是耶和华说的。”

9你们去向万国宣告:

“要召集勇士,征调军队,

前去打仗!

10要将犁头打成刀剑,

把镰刀铸成矛头,

软弱的人也要做勇士!

11四围的列国啊,

你们快快聚集到那里吧!”

耶和华啊,

求你差遣大能的勇士降临。

12“万国都要起来,

上到约沙法谷受审判,

因为我要坐在那里审判他们。

13开镰吧,因为庄稼熟了;

踩踏吧,因为榨酒池的葡萄满了。

他们恶贯满盈,如酒池满溢。”

14千千万万的人聚集在审判谷,

因为耶和华的日子要临到那里。

15日月昏暗,

星辰无光。

16耶和华从锡安发出怒吼,

耶路撒冷发出雷声,

天地为之震动。

但耶和华却是祂子民的避难所,

以色列人的堡垒。

17“这样,你们就知道我是你们的上帝耶和华,

我住在锡安——我的圣山上。

耶路撒冷必成为圣地,

外族人必不再侵犯它。

18“到那日,群山要滴下甜酒,

丘陵要流出乳汁。

犹大的溪涧碧水常流,

必有清泉从耶和华的殿中流出,

浇灌什亭谷。

19埃及必一片荒凉,

以东必成为不毛之地,

因为他们曾残暴地对待犹大人,

犹大滥杀无辜。

20犹大必人口兴盛,

耶路撒冷必存到万代。

21我必追讨3:21 追讨”希伯来文是“洗净”。尚未追讨的血债,

因为耶和华住在锡安。”