Yoweli 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 1:1-20

1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

2Inu akuluakulu, imvani izi;

mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.

Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,

kapena mʼnthawi ya makolo anu?

3Muwafotokozere ana anu,

ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,

ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.

4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya

dzombe lowuluka ladya;

chimene dzombe lowuluka lasiya

dzombe lalingʼono ladya;

chimene dzombe lalingʼono lasiya

chilimamine wadya.

5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!

Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;

lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,

pakuti wachotsedwa pakamwa panu.

6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,

wamphamvu ndi wosawerengeka;

uli ndi mano a mkango,

zibwano za mkango waukazi.

7Wawononga mphesa zanga

ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.

Wakungunula makungwa ake

ndi kuwataya,

kusiya nthambi zake zili mbee.

8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,

chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.

9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.

Ansembe akulira,

amene amatumikira pamaso pa Yehova.

10Minda yaguga,

nthaka yauma;

tirigu wawonongeka,

vinyo watsopano watha,

mitengo ya mafuta yauma.

11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,

lirani mofuwula inu alimi a mphesa;

imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,

pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.

12Mpesa wauma

ndipo mtengo wamkuyu wafota;

makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,

mitengo yonse ya mʼmunda yauma.

Ndithudi chimwemwe cha anthu

chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;

lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.

Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,

inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;

pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.

14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,

itanani msonkhano wopatulika.

Sonkhanitsani akuluakulu

ndi anthu onse okhala mʼdziko

ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu

ndipo alirire Yehova.

15Kalanga ine tsikulo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa

ife tikuona?

Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu

simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?

17Mbewu zikunyala

poti pansi ndi powuma.

Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;

nkhokwe zapasuka

popeza tirigu wauma.

18Taonani mmene zikulirira ziweto;

ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku

chifukwa zilibe msipu;

ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19Kwa Inu Yehova ndilirira,

pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,

malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.

20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;

timitsinje tonse taphwa

ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

New Russian Translation

Иоиль 1:1-20

1Слово Господне, которое было к Иоилю, сыну Петуила:

Нашествие саранчи

2Слушайте, старцы,

внимайте, все жители этой страны!

Случалось ли что-либо, подобное этому, в ваши дни

или в дни ваших отцов?

3Расскажите об этом вашим детям,

они же пусть перескажут это своим,

а их дети пусть передадут следующему поколению.

4То, что осталось от подбирающей саранчи,

ела грызущая саранча,

то, что осталось от грызущей саранчи,

ела поедающая саранча,

а то, что осталось от поедающей саранчи,

доела пожирающая саранча1:4 В этом стихе на языке оригинала для обозначения саранчи использованы четыре слова. Эти слова могут быть либо просто синонимами, либо терминами, которые отражают четыре стадии развития саранчи. То же в ст. 2:25..

5Пробудитесь, пьяницы, и плачьте,

причитайте, пьющие вино,

оплакивайте молодое вино,

потому что оно отнято от уст ваших!

6На мою землю вступил народ,

сильный и бесчисленный.

Его зубы – зубы льва,

а клыки – как у львицы.

7Он разорил мою виноградную лозу,

обломал мой инжир.

Обнажил, ободрав его кору, и бросил;

белыми стали его ветви.

8Плачьте, как девушка, что облачилась в рубище

и оплакивает своего возлюбленного.

9Прекратились хлебные приношения

и возлияния в доме Господнем.

Скорбят священники, служители Господа.

10Опустошено поле

и плачет земля;

уничтожено зерно,

засох молодой виноград

и увяла олива.

11Сокрушайтесь, земледельцы,

о пшенице и ячмене,

потому что погиб урожай на полях.

Рыдайте, виноградари,

12потому что засохла виноградная лоза

и завял инжир;

гранат, пальма и яблоня –

все деревья на поле засохли;

потому и прекратилось веселье

у сынов человеческих.

13Облекитесь в рубище, священники, и плачьте,

рыдайте, служащие перед жертвенником.

Придите, служители моего Бога,

и проведите ночь в рубищах,

потому что хлебные приношения и возлияния

прекратились в доме вашего Бога.

14Объявите священный пост,

созовите собрание,

пригласите старцев

и всех жителей страны

в дом Господа, вашего Бога,

и взывайте к Господу.

День Господень

15О, этот день!

Близок день Господень,

придет он подобно разрушению от Всемогущего.

16Не на наших ли глазах отнимается пища,

а радость и веселье уходят из дома нашего Бога?

17Истлели зерна под глыбами земли,

разрушены кладовые,

опустели амбары,

потому что нет больше зерна.

18О, как стонет скот!

Уныло бродят стада,

потому что нет для них пищи;

даже отары овец несут наказание.

19Я взываю к Тебе, Господи,

потому что огонь спалил степные пастбища

и пламя пожрало все деревья в поле.

20Даже дикие животные взывают к Тебе,

потому что высохли источники воды

и огонь спалил степные пастбища.