Yoweli 1 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoweli 1:1-20

1Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

2Inu akuluakulu, imvani izi;

mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.

Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,

kapena mʼnthawi ya makolo anu?

3Muwafotokozere ana anu,

ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,

ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.

4Chimene dzombe losamera mapiko lasiya

dzombe lowuluka ladya;

chimene dzombe lowuluka lasiya

dzombe lalingʼono ladya;

chimene dzombe lalingʼono lasiya

chilimamine wadya.

5Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!

Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;

lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,

pakuti wachotsedwa pakamwa panu.

6Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,

wamphamvu ndi wosawerengeka;

uli ndi mano a mkango,

zibwano za mkango waukazi.

7Wawononga mphesa zanga

ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.

Wakungunula makungwa ake

ndi kuwataya,

kusiya nthambi zake zili mbee.

8Lirani ngati namwali wovala chiguduli,

chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.

9Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.

Ansembe akulira,

amene amatumikira pamaso pa Yehova.

10Minda yaguga,

nthaka yauma;

tirigu wawonongeka,

vinyo watsopano watha,

mitengo ya mafuta yauma.

11Khalani ndi nkhawa, inu alimi,

lirani mofuwula inu alimi a mphesa;

imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,

pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.

12Mpesa wauma

ndipo mtengo wamkuyu wafota;

makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,

mitengo yonse ya mʼmunda yauma.

Ndithudi chimwemwe cha anthu

chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;

lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.

Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,

inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;

pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa

sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.

14Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,

itanani msonkhano wopatulika.

Sonkhanitsani akuluakulu

ndi anthu onse okhala mʼdziko

ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu

ndipo alirire Yehova.

15Kalanga ine tsikulo!

Pakuti tsiku la Yehova layandikira;

lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16Kodi chakudya chathu sichachotsedwa

ife tikuona?

Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu

simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?

17Mbewu zikunyala

poti pansi ndi powuma.

Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;

nkhokwe zapasuka

popeza tirigu wauma.

18Taonani mmene zikulirira ziweto;

ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku

chifukwa zilibe msipu;

ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19Kwa Inu Yehova ndilirira,

pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,

malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.

20Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;

timitsinje tonse taphwa

ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

Священное Писание

Иоиль 1:1-20

1Слово Вечного1:1 Вечный – на языке оригинала: «Яхве». Под этим именем Всевышний открылся Мусе и народу Исраила (см. Исх. 3:13-15). См. пояснительный словарь., которое было к Иоилю, сыну Петуила.

Нашествие саранчи

2Слушайте, старцы,

внимайте, все жители этой страны!

Случалось ли что-либо подобное в ваши дни

или в дни ваших отцов?

3Расскажите об этом вашим детям,

они же пусть перескажут это своим,

а те пусть передадут следующему поколению.

4Стая за стаей налетела саранча,

пожрала всё на своём пути.

Что оставалось после одной стаи,

уничтожала следующая1:4 В этом стихе на языке оригинала для обозначения саранчи использованы четыре слова. Эти слова могут быть либо просто синонимами, либо терминами, которые отражают четыре стадии развития саранчи. То же в 2:25..

5Пробудитесь, пьяницы, и плачьте,

причитайте, пьющие вино,

оплакивайте молодое вино,

потому что оно отнято от уст ваших!

6На мою землю вступил народ,

сильный и бесчисленный.

Его зубы – зубы льва,

а клыки – как у львицы.

7Он разорил мою виноградную лозу,

обломал мой инжир.

Обнажил, ободрав его кору, и бросил;

белыми стали его ветви.

8Плачьте, как девушка, что облачилась в рубище

и оплакивает своего возлюбленного.

9Хлебные приношения и жертвенные возлияния

прекратились в доме Вечного;

скорбят священнослужители Вечного.

10Опустошено поле,

и высохла земля;

уничтожено зерно,

засох молодой виноград,

и увяла маслина.

11Сокрушайтесь, земледельцы,

о пшенице и ячмене,

потому что погиб урожай на полях.

Рыдайте, виноградари,

12потому что засохла виноградная лоза

и завял инжир;

гранат, пальма и яблоня –

все деревья на поле засохли;

потому и прекратилось веселье

у всего народа.

13Облекитесь в рубище, священнослужители, и плачьте,

рыдайте, служащие перед жертвенником.

Придите, служители моего Бога,

и проведите ночь в рубищах,

потому что хлебные приношения и жертвенные возлияния

прекратились в доме вашего Бога.

14Объявите священный пост,

созовите собрание,

пригласите старцев

и всех жителей страны

в дом Вечного, вашего Бога,

и взывайте к Нему.

День Вечного

15О, этот день!

Близок день Вечного,

несёт он разрушение от Всемогущего.

16Не на наших ли глазах

отнимается пища,

а радость и веселье уходят

из дома нашего Бога?

17Истлели зёрна под глыбами земли,

разрушены кладовые,

опустели амбары,

потому что нет больше зерна.

18О, как стонет скот!

Уныло бродят стада,

потому что нет для них пищи;

даже отары овец несут наказание.

19Я взываю к Тебе, о Вечный,

потому что огонь спалил степные пастбища

и пламя пожрало все деревья в поле.

20Даже дикие животные взывают к Тебе,

потому что высохли источники воды

и огонь спалил степные пастбища.