Yoswa 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 4:1-24

1Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa, 2“Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse. 3Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’ ”

4Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse, 5ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli, 6kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’ 7Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’ ”

8Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko. 9Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.

10Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira. 11Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova. 12Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira. 13Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.

14Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.

15Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, 16“Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”

17Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.

18Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.

19Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko. 20Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija. 21Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’ 22Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’ 23Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma. 24Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約書亞記 4:1-24

堆石為證

1民眾都過河之後,耶和華對約書亞說: 2「你去從民眾中選出十二個人,每支派選一人, 3吩咐他們從約旦河床祭司站立的地方取十二塊石頭,放在你們今天晚上住宿的地方。」 4約書亞便召來他從以色列人中選的十二個人,對他們說: 5「你們到約旦河床你們的上帝耶和華的約櫃前面,每人扛一塊石頭回來,每個支派一塊,一共十二塊。 6這些石頭要在你們中間作記號。以後,倘若你們的子孫問你們,『這些石頭是什麼意思?』 7你們就告訴他們,『約旦河水在耶和華的約櫃前曾經被截斷,當約櫃過河的時候,河水被截斷了。這些石頭要在以色列人當中作為永久的紀念。』」

8以色列人就照約書亞的吩咐,也就是照耶和華對約書亞的吩咐,按以色列人支派的數目,從約旦河中取了十二塊石頭,搬來放在住宿的地方。 9約書亞又在約旦河床抬約櫃的祭司站立的地方立了十二塊石頭。石頭至今還在那裡。 10抬約櫃的祭司站在約旦河中間,一直站到耶和華吩咐約書亞交待民眾做的每一件事都完成了,正如摩西約書亞的吩咐。民眾迅速過了河。 11所有人都過河以後,祭司才抬著耶和華的約櫃在民眾注視之下過了河。 12呂便支派、迦得支派和瑪拿西半個支派的人照摩西從前的囑咐,帶著兵器走在以色列人的前面。 13大約有四萬全副武裝的以色列人在耶和華面前過了河,前往耶利哥平原,準備作戰。 14那一天,耶和華使約書亞以色列眾人面前受尊重,他像摩西一樣終生受民眾敬畏。

15耶和華對約書亞說: 16「你去吩咐抬約櫃的祭司從約旦河裡上來。」 17約書亞便吩咐他們上來。 18抬耶和華約櫃的祭司從河床上來,腳剛一踏上岸,約旦河的水立刻恢復了原狀,像以往一樣漲過兩岸。

19那天是一月十日。以色列人從約旦河上來之後,就在耶利哥東邊的吉甲紮營。 20約書亞把從約旦河取來的十二塊石頭立在吉甲21並對以色列人說:「以後,你們的子孫問你們這堆石頭是什麼意思, 22你們就告訴他們,『這是代表以色列人曾在乾地上走過約旦河。』 23因為你們的上帝耶和華為了讓你們過河而使約旦河成為乾地,就像祂從前為了讓我們過紅海而使海成為乾地一樣。 24這是要讓天下萬民都知道耶和華有無比的能力,要讓你們永遠敬畏你們的上帝耶和華。」