Yoswa 3 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 3:1-17

Aisraeli Awoloka Yorodani

1Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo. 2Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse, 3kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira. 4Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”

5Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”

6Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.

7Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose. 8Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’ ”

9Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu. 10Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi. 11Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu. 12Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli. 13Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”

14Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo. 15Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo, 16madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko. 17Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.

New Serbian Translation

Књига Исуса Навина 3:1-17

Прелазак преко Јордана

1Исус порани и са свим Израиљцима крене из Ситима. Дођу до Јордана, па тамо, код прелаза, преноће. 2Након три дана, војни заповедници прођу табором 3и заповеде народу: „Чим видите да свештеници Левити носе Ковчег савеза Господа, Бога вашега, ви крените са вашег места и идите за њима. 4Међутим, нека растојање између вас и Ковчега буде око две хиљаде лаката3,4 Око 1 km.. Не прилазите му ближе, да бисте знали којим путем да идете, јер тим путем нисте путовали раније.“

5Затим Исус рече народу: „Посветите се, јер ће Господ сутра учинити чудеса међу вама.“

6А свештеницима рече: „Понесите Ковчег савеза и крените испред народа.“ Они понесу Ковчег савеза и крену испред народа.

7Господ рече Исусу: „Овог истог дана ћу почети да те узвисујем у очима целог Израиља, да знају да ћу бити са тобом као што сам био са Мојсијем. 8Ти заповеди свештеницима који носе Ковчег савеза: ’Када стигнете до руба вода јорданских, станите у Јордан.’“

9Онда Исус рече Израиљцима: „Приђите овде и чујте речи Господа Бога вашега.“ 10Исус рече: „По овоме ћете знати да је живи Бог међу вама: он ће терати испред вас Хананце, Хетите, Евејце, Фережане, Гергешане, Аморејце и Јевусејце. 11Ево, Ковчег савеза Господа целе земље ићи ће пред вама у Јордан. 12А сада одаберите међу собом дванаест људи из племена Израиљевих, од сваког племена по једног. 13Чим стопала свештеника који носе Ковчег Господа, Владара целе земље, ступе у воде Јордана, разделиће се воде Јордана што теку од горе и остати да стоје као брана.“

14Кад је народ кренуо из својих шатора да пређе преко Јордана, свештеници који носе Ковчег савеза су били испред народа. 15Тек што су носачи Ковчега дошли до Јордана и ноге свештеника који носе Ковчег дотакле руб воде (а током свег времена жетве Јордан плави своје обале), 16воде које теку од горе су стале и усправиле се као брана веома далеко одатле, код Адама, града који се налази покрај Сартана, док је вода која се спушта до мора Араве – Мртвог мора, потпуно отекла. Народ је, пак, прелазио према Јерихону. 17Свештеници који носе Ковчег савеза Господњег су непомично стајали на сувом усред Јордана, док сав Израиљ није прешао преко Јордана.