Yoswa 3 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 3:1-17

Aisraeli Awoloka Yorodani

1Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo. 2Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse, 3kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira. 4Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”

5Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”

6Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.

7Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose. 8Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’ ”

9Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu. 10Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi. 11Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu. 12Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli. 13Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”

14Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo. 15Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo, 16madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko. 17Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.

Священное Писание

Иешуа 3:1-17

Переправа через Иордан

1Рано утром Иешуа и все исраильтяне вышли из Шиттима и пришли к Иордану, где разбили лагерь перед тем, как переправиться через реку. 2Через три дня начальники прошли по лагерю, 3приказывая народу:

– Когда вы увидите священнослужителей-левитов, которые будут нести сундук соглашения3:3 Сундук соглашения – см. пояснительный словарь, а также Исх. 25:10-22. с Вечным, вашим Богом, то снимайтесь со своих мест и идите за ним, 4чтобы вам знать, каким путём идти, потому что вы не ходили этим путём прежде. Но пусть между вами и сундуком будет расстояние около километра3:4 Букв.: «две тысячи локтей».. Не приближайтесь к нему.

5Иешуа сказал народу:

– Освятитесь, потому что завтра Вечный совершит среди вас чудеса.

6Иешуа сказал священнослужителям:

– Возьмите сундук соглашения и идите перед народом.

Они взяли его и пошли перед народом.

7Вечный сказал Иешуа:

– Сегодня Я начну возвышать тебя в глазах всего Исраила, чтобы народ знал, что Я буду с тобой, как прежде был с Мусой. 8Вели священнослужителям, которые несут сундук соглашения: «Когда вы дойдёте до Иордана, войдите в реку и остановитесь».

9Иешуа сказал исраильтянам:

– Подойдите и выслушайте слова Вечного, вашего Бога. 10Вот как вы узнаете, что живой Бог среди вас и что Он непременно прогонит перед вами хананеев, хеттов, хивеев, перизеев, гиргашеев, аморреев и иевусеев. 11Смотрите, сундук соглашения с Владыкой всей земли войдёт в Иордан впереди вас. 12Итак, выберите из родов Исраила двенадцать человек, по одному из каждого рода. 13И как только стопы священнослужителей, несущих сундук Вечного, Владыки всей земли, коснутся Иордана, его воды иссякнут, а воды, текущие сверху, встанут стеной.

14Когда народ свернул лагерь, чтобы переправиться через Иордан, священнослужители пошли перед народом, неся сундук соглашения. 15(А Иордан выступает из берегов во всё время жатвы.) Но как только те, кто нёс сундук, подошли к Иордану и их ноги коснулись края воды, 16вода, текущая сверху, остановилась. Она встала стеной очень далеко, у города Адама, что рядом с Цартаном, а вода, текущая вниз, в Мёртвое море3:16 Букв.: «в море Аравы, Солёное море»., полностью иссякла. 17И народ переправился напротив Иерихона. Священнослужители, которые несли сундук соглашения с Вечным, стояли на сухой земле посреди Иордана, пока весь народ Исраила, идущий мимо них, не переправился посуху.