Yoswa 23 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 23:1-16

Kutsanzika kwa Yoswa

1Panapita nthawi yayitali kuchokera pamene Yehova anakhazikitsa mtendere pakati pa Aisraeli ndi adani awo owazungulira. Nthawi imeneyi nʼkuti Yoswa atakalamba, ali ndi zaka zambiri. 2Yoswayo anayitanitsa Aisraeli onse pamodzi ndi akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi oyangʼanira anthu antchito ndipo anawawuza kuti, “Ine ndakalamba ndipo ndili ndi zaka zambiri. 3Inu mwaona zonse zimene Yehova Mulungu wanu wachita kwa mitundu yonseyi chifukwa cha inu. Ndi Yehova Mulungu wanu amene anakumenyerani nkhondo. 4Tsono onani! Mitundu ya anthu otsalawa ndayipereka kwa mafuko anu pamodzi ndi mitundu ya anthu ya pakati pa Yorodani ndi Nyanja Yayikulu ya kumadzulo imene ndinayigonjetsa. 5Yehova Mulungu wanu ndiye adzawathamangitsa pamaso panu. Mudzatenga dziko lawo monga Yehova anakulonjezerani.

6“Choncho khalani amphamvu, ndipo samalani kuti mumvere zonse zimene zalembedwa mʼbuku la malamulo a Mose. Musapatuke pa malamulo onse amene alembedwamo. 7Musagwirizane ndi mitundu ya anthu imene yatsala pakati panu. Musatchule mayina a milungu yawo kapena kuyitchula polumbira. Musayitumikire kapena kuyigwadira. 8Koma mukuyenera kugwiritsa Yehova Mulungu wanu, monga mwachitira mpaka lero lino.

9“Yehova wapirikitsa patsogolo panu mitundu ya anthu ikuluikulu ndi yolimba. Mpaka lero palibe amene watha kulimbana nanu. 10Aliyense wa inu atha kuthamangitsa anthu 1,000 chifukwa Yehova Mulungu wanu ndiye amakumenyerani nkhondo, monga momwe analonjezera. 11Choncho samalitsani kuti mukonde Yehova Mulungu wanu.

12“Koma ngati mubwerera mʼmbuyo ndi kuphatikizana ndi mitundu yotsalayi imene ili pakati panu ndi kumakwatirana nayo, 13pamenepo mudziwe kuti Yehova, Mulungu wanu, sadzapirikitsa mitundu imeneyi pamaso panu, koma idzakhala ngati msampha kwa inu kapenanso khwekhwe lokukolani. Idzakhala ngati zikwapu pa msana panu kapenanso ngati minga mʼmaso mwanu mpaka mutatha psiti mʼdziko labwinoli limene Yehova Mulungu wanu wakupatsani.

14“Aliyense wa inu akudziwa mu mtima mwake komanso mʼmoyo mwake kuti zabwino zonse zimene Yehova Mulungu wanu anakulonjezani zachitika. Palibe lonjezo ndi limodzi lomwe limene silinakwaniritsidwe. 15Monga momwe Yehova Mulungu wanu wakuchitirani zabwino zonse zimene ananena kuti adzachita, Yehovayo angathenso kukuchitirani zoyipa zonse zimene waopseza, mpaka kukuchotsani mʼdziko lokoma limene anakupatsani. 16Ngati muphwanya pangano la Yehova Mulungu wanu, limene anakulamulirani nʼkumapita kukatumikira milungu ina ndi kuyigwadira, Yehova adzakukwiyirani, ndiye mudzachotsedwa mʼdziko labwinoli limene Yehova wakupatsani.”

Korean Living Bible

여호수아 23:1-16

여호수아의 고별사

1여호와께서 이스라엘 백성에게 그 주변 일대의 모든 적들을 물리치게 하시고 평안을 주신 지도 오랜 세월이 지났으며 이제 여호수아도 많이 늙었다.

2그래서 그는 장로들과 지도자들과 재판관들과 사무원들을 포함한 모든 이스라엘 백성을 불러 놓고 이렇게 말하였다. “이제 나는 많이 늙었습니다.

3여러분은 여호와 하나님이 이 모든 나라에 행하신 일을 보아 알겠지만 여러분의 하나님 여호와께서는 여러분을 위해 싸우신 분이십니다.

4보십시오. 내가 동쪽으로 요단강에서부터 서쪽으로 지중해에 이르기까지 이미 정복한 땅은 물론, 아직 정복하지 않은 땅까지 다 여러분에게 제비 뽑아 나누어 주었습니다.

5그리고 여러분의 하나님 여호와께서는 약속하신 대로 남아 있는 자들을 모조리 쫓아내고 대신 여러분이 그 땅에 살 수 있도록 하실 것입니다.

6그러므로 여러분은 모세의 율법책에 기록된 모든 것을 힘써 지키고 조금도 거기서 이탈하지 마십시오.

7그리고 여러분은 아직 남아 있는 이방 민족들과 사귀지 말고 그 신들의 이름을 부르거나 그 이름으로 맹세하지 마십시오. 여러분이 그들의 신을 섬기거나 절해서는 안 됩니다.

8지금까지 해 온 대로 여러분은 여러분의 하나님 여호와만 따르고 섬겨야 합니다.

9여호와께서 크고 강한 나라들을 여러분 앞에서 쫓아내셨으므로 지금까지 여러분을 당해 낼 자가 하나도 없었습니다.

10여러분의 하나님 여호와께서 약속하신 대로 여러분을 위해 싸우시기 때문에 앞으로도 여러분은 한 사람이 적군 천 명을 당해 낼 수 있을 것입니다.

11그러므로 조심하여 여러분의 하나님 여호와를 사랑하십시오.

12만일 여러분이 그렇게 하지 않고 남아 있는 이방 민족들과 하나가 되어 혼인을 맺고 그들과 교제하면

13여러분의 하나님 여호와께서 이 이방 민족들을 여러분 앞에서 더 이상 쫓아내지 않으실 것입니다. 그래서 그들이 여러분에게 덫이나 함정과 같은 위험스러운 존재가 되고 또 옆구리의 채찍이나 눈의 가시와 같은 고통스러운 존재가 될 것입니다. 이렇게 되면 결국 여러분은 여러분의 하나님 여호와께서 주신 이 좋은 땅에서 한 사람도 살아 남지 못하고 완전히 멸망하게 될 것입니다.

14“이제 나는 온 세상 사람이 가는 길로 떠날 때가 되었습니다. 여러분은 여호와 하나님이 약속하신 모든 선한 일이 다 이루어진 것을 잘 알고 있습니다.

15그러나 여호와께서는 약속하신 모든 선한 일을 다 이루신 것과 마찬가지로 자기가 말씀하신 23:15 또는 ‘불길한 일’재앙도 여러분에게 내리실 것입니다.

16만일 여러분이 여호와께서 지키라고 명령하신 계약을 어겨 다른 신들을 섬기고 절하면 그가 노하셔서 여러분을 벌하실 것입니다. 그렇게 되면 여러분은 여호와께서 주신 이 좋은 땅에서 순식간에 망하고 말 것입니다.”