Yoswa 21 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 21:1-45

Mizinda ya Alevi

1Tsono atsogoleri a mabanja a fuko la Levi anabwera kwa wansembe Eliezara, Yoswa mwana wa Nuni, ndi kwa atsogoleri a mabanja a mafuko onse a Aisraeli, 2ku Silo mʼdziko la Kanaani ndipo anati, “Yehova analamula kudzera mwa Mose kuti atipatse mizinda kuti tikhalemo, pamodzi ndi malo odyetseramo ziweto zathu.” 3Choncho, Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizinda iyi pamodzi ndi malo owetera ziweto zawo kuchokera ku madera awo, monga Yehova analamulira:

4Maere oyamba anagwera mabanja a Kohati, Alevi amene anali zidzukulu za wansembe Aaroni anapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mafuko a Yuda, Simeoni ndi Benjamini. 5Ndipo mabanja otsala a Kohati anapatsidwa mizinda khumi kuchokera ku mafuko a Efereimu, Dani ndi theka la fuko la Manase.

6Zidzukulu za Geresoni zinapatsidwa mizinda 13 kuchokera ku mabanja a mafuko a Isakara, Aseri, Nafutali ndi theka la fuko la Manase ku Basani.

7Mabanja a Merari anapatsidwa mizinda khumi ndi iwiri kuchokera ku mafuko a Rubeni, Gadi ndi Zebuloni.

8Choncho Aisraeli anapereka kwa fuko la Levi mizindayi pamodzi ndi malo odyetserako ziweto pogwiritsa ntchito maere, monga Yehova analamula kudzera mwa Mose.

9Awa ndi mayina a mizinda ya mafuko a Yuda ndi Simeoni imene inaperekedwa kwa zidzukulu za Aaroni, 10ku banja la Kohati amene anali Alevi. Paja maere oyamba anagwera mabanja a Kohati kuti alandira mizinda.

11Anapatsidwa mzinda wa Kiriati Ariba. (Paja Ariba ndiye kholo la Anaaki). Dzina lina la mzindawu ndi Hebroni, ndipo unali mʼdziko la mapiri la Yuda. Pamodzi ndi mzindawu anapatsidwanso mabusa ake onse ozungulira. 12Komabe minda ndi midzi yozungulira mizindayi inali itaperekedwa kale kwa Kalebe, mwana wa Yefune kuti ikhale cholowa chake.

13Choncho zidzukulu za Aaroni wansembe, zinapatsidwa Hebroni (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu), Libina, 14Yatiri, Esitemowa, 15Holoni, Debri, 16Aini, Yuta, ndi Beti-Semesi pamodzi ndi mabusa odyetseramo ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda isanu ndi inayi yochokera ku mafuko awiriwa.

17Fuko la Benjamini linapereka Gibiyoni, Geba, 18Anatoti ndi Alimoni, pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

19Choncho mizinda 13 pamodzi ndi malo odyetsera ziweto anapatsidwa kwa ansembe, zidzukulu za Aaroni.

20Mabanja ena otsalira a Kohati a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iyi kuchokera ku fuko la Efereimu:

21Mizinda ya Sekemu ndi Gezeri ndiye inali mizinda wopulumukirako munthu aliyense wopha mnzake mwangozi. Mizindayi inali ku mapiri a Efereimu. 22Analandiranso mizinda ya Gezeri, Kibuzaimu, Beti-Horoni pamodzi ndi malo odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

23Fuko la Dani linapereka mizinda ya Eliteke, Gibetoni, 24Ayaloni, Gati-Rimoni pamodzi ndi mabusa odyetsera ziweto ozungulira mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

25Kuchokera ku theka la fuko la Manase analandira Taanaki ndi Gati-Rimoni pamodzi ndi malo awo owetera ziweto, mizinda iwiri.

26Mizinda khumi yonseyi pamodzi ndi malo odyetsera ziweto, zinapatsidwa ku mabanja ena onse a Akohati.

27Mabanja a Ageresoni a fuko la Levi anapatsidwa mizinda iwiri

kuchokera ku theka la Manase wa kummawa,

Golani ku Basani (mzinda wopulumukirako amene wapha munthu mwangozi) ndi Beesitera, pamodzi ndi malo awo odyetserako ziweto.

28Fuko la Isakara linapereka mizinda ya

Kisoni, Daberati, 29Yarimuti ndi Eni Ganimu, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

30Fuko la Aseri linapereka mizinda ya

Misali, Abidoni, 31Helikati ndi Rehobu pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

32Fuko la Nafutali linapereka mizinda ya

Kedesi wa ku Galileya, mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. Analandiranso mizinda ya Hamoti-Dori ndi Karitani. Kuphatikizira apa, analandira malo odyetsera ziweto a mizindayi. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

33Mabanja onse a Ageresoni analandira mizinda 13 pamodzi ndi malo awo odyetsera a ziweto.

34Mabanja a Merari amene anali otsala a fuko la Levi, anapatsidwa

mizinda iyi kuchokera ku fuko la Zebuloni:

Yokineamu, Karita, 35Dimuna ndi Nahalali, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

36Kuchokera ku fuko la Rubeni analandira

Bezeri, Yahaza, 37Kedemoti ndi Mefaati, pamodzi ndi malo awo odyetsera ziweto. Yonse pamodzi inali mizinda inayi.

38Kuchokera ku fuko la Gadi

analandira mzinda wa Ramoti ku Giliyadi. Mzinda umene unali wopulumukiramo munthu wopha mnzake mwangozi. 39Analandiranso mizinda ya Mahanaimu, Hesiboni, Yazeri pamodzi ndi malo odyetserako ziweto ozungulira mizinda yonseyi. Yonse pamodzi inali mizindayi anayi.

40Choncho mabanja onse a Merari, amene anali otsala a fuko la Levi analandira mizinda khumi ndi iwiri pogwiritsa ntchito maere.

41Motero mizinda 48 ya mʼdziko limene Aisraeli analanda inapatsidwa kwa Alevi, kuphatikizapo malo ake odyetsera ziweto. 42Iliyonse mwa mizindayi inali ndi malo owetera ziweto oyizungulira.

43Motero Yehova anapereka kwa Israeli dziko limene analumbira kulipereka kwa makolo awo. Atalilandira anadzakhalamo. 44Yehova anawapatsa mtendere mʼdziko lonse monga momwe analonjezera makolo awo. Palibe ndi mmodzi yemwe mwa adani awo amene anatha kuwagonjetsa chifukwa Yehova anapereka adani awo onse mʼmanja mwawo. 45Yehova anakwaniritsa zonse zimene analonjeza kwa Aisraeli.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иешуа 21:1-45

Города для левитов

(1 Лет. 6:54-80)

1Главы левитских семейств пришли к священнослужителю Элеазару, к Иешуа, сыну Нуна, и к главам остальных семейств в родах Исроила 2в Шило в Ханоне и сказали им:

– Вечный повелел через Мусо, чтобы нам дали города для жительства с пастбищами для нашего скота.

3И по повелению Вечного исроильтяне дали левитам следующие города и пастбища из своих наделов:

4Первый жребий выпал каафитам, по их кланам. Левитам, которые были потомками священнослужителя Хоруна, досталось тринадцать городов от родов Иуды, Шимона и Вениамина. 5Остальные потомки Каафы получили по жребию десять городов от кланов, принадлежащих родам Ефраима, Дона и половине рода Манассы.

6Потомкам Гершона досталось тринадцать городов от кланов, принадлежащих родам Иссокора, Ошера и Неффалима и половине рода Манассы в Бошоне.

7Потомки Мерари, по их кланам, получили двенадцать городов от родов Рувима, Гада и Завулона.

8Так исроильтяне выделили левитам эти города и пастбища, как повелел через Мусо Вечный.

9От родов Иуды и Шимона дали следующие города, упоминаемые по названию 10(эти города были предназначены потомкам священнослужителя Хоруна из каафитских кланов левитов, потому что им выпал первый жребий):

11Они дали им город Кириат-Арбу (то есть Хеврон) с его окрестными пастбищами в нагорьях Иуды. (Арба был отцом Анака.) 12Но поля и поселения вокруг города были отданы во владение Халеву, сыну Иефоннии.

13Итак, потомкам священнослужителя Хоруна они дали Хеврон (город-убежище для обвиняемого в убийстве), Ливну, 14Иаттир, Эштемоа, 15Холон, Девир, 16Аин, Ютту и Бет-Шемеш с их пастбищами – девять городов от двух этих родов.

17А от рода Вениамина дали им Гаваон, Геву, 18Анатот и Алмон с их пастбищами – четыре города.

19Всего для священнослужителей, потомков Хоруна, было отдано тринадцать городов с их пастбищами.

20Остальным каафитским кланам левитов достались следующие города от рода Ефраима:

21Им дали Шахем (город-убежище для обвиняемого в убийстве) в нагорьях Ефраима, Гезер, 22Кивцаим и Бет-Хорон с их пастбищами – четыре города.

23А от рода Дона они получили Элтеке, Гиббетон, 24Аялон и Гат-Риммон с их пастбищами – четыре города.

25От половины рода Манассы они получили Таанах и Гат-Риммон с их пастбищами – два города.

26Все эти города с их пастбищами были даны остальным каафитским кланам.

27Гершонитским кланам левитов дали

от половины рода Манассы: Голан, что в Бошоне (город-убежище для обвиняемого в убийстве), и Беэштера с их пастбищами – два города;

28от рода Иссокора: Кишион, Даверат, 29Иармут и Ен-Ганним с их пастбищами – четыре города;

30от рода Ошера: Мишал, Авдон, 31Хелкат и Рехов с их пастбищами – четыре города;

32от рода Неффалима: Кедеш, что в Галилее (город-убежище для обвиняемого в убийстве), Хаммот-Дор и Картан с их пастбищами – три города.

33Всего у гершонитских кланов было тринадцать городов с пастбищами.

34Мераритским кланам (остальным левитам) дали

от рода Завулона: Иокнеам, Карту, 35Димну и Нахалал с их пастбищами – четыре города;

36от рода Рувима: Бецер, Иахац, 37Кедемот и Мефаат с их пастбищами – четыре города;

38от рода Гада: Рамот, что в Галааде (город-убежище для обвиняемого в убийстве), Маханаим, 39Хешбон и Иазер с их пастбищами – всего четыре города.

40Всего городов, доставшихся мераритским кланам, остальным левитам, было двенадцать.

41Всего в земельных владениях исроильтян было сорок восемь левитских городов с их пастбищами. 42Вокруг каждого из этих городов были пастбища. Так было вокруг всех этих городов.

43Так Вечный отдал исроильтянам всю землю, которую Он клялся дать их предкам, и они завладели ею и поселились там. 44Вечный дал им покой со всех сторон, как Он и клялся их предкам. Никто из их врагов не устоял перед ними, Вечный отдал их врагов им в руки. 45Ни одно из тех добрых обещаний, которые Вечный дал народу Исроила, не осталось неисполненным, исполнилось каждое.