Yoswa 20 – CCL & CARST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 20:1-9

Mizinda Yopulumukiramo

1Pambuyo pake Yehova anati kwa Yoswa: 2“Uza Aisraeli kuti apatule mizinda yopulumukiramo, monga ine ndinakulangizira kudzera mwa Mose, 3kuti aliyense amene wapha munthu mosazindikira osati mwadala azithawirako. Motero adzatetezedwa kwa wolipsira. 4Ngati munthu wathawira ku umodzi mwa mizinda imeneyi, akafike pa malo oweruzira milandu amene ali pa chipata cha mzindawo ndipo akafotokoze mlandu wake pamaso pa akuluakulu a mzindawo. Kenaka iwo adzamulola kulowa mu mzinda wawo ndi kumupatsa malo woti akhale nawo. 5Ngati munthu wolipsirayo amutsatira komweko atsogoleriwo asapereke munthu wakuphayo chifukwa anapha Mwisraeli mnzakeyo mosazindikira, osati mwachiwembu. 6Munthu wakuphayo adzakhalabe mu mzindawo mpaka atayimbidwa mlandu pamaso pa gulu lonse, ndiponso mpaka atamwalira mkulu wa ansembe amene akutumikira pa nthawiyo. Pamenepo munthuyo atha kubwereranso ku mudzi kwawo kumene anachoka mothawa kuja.”

7Choncho iwo anapatula Kedesi mʼdera la Galileya ku mapiri a Nafutali, Sekemu ku mapiri a Efereimu, ndi Kiriati Ariba (ndiye Hebroni) ku mapiri a Yuda. 8Kummawa kwa Yorodani, mʼmapiri a chipululu a kummawa kwa Yeriko, anapatula Bezeri pakati pa dera la fuko la Rubeni. Anapatulanso Ramoti ku Giliyadi mʼdera la fuko la Gadi, ndiponso Golani ku Basani mʼdera la fuko la Manase. 9Imeneyi ndiyo inali mizinda yopulumukiramo ya Aisraeli onse ngakhalenso mlendo wokhala pakati pawo. Munthu aliyense wopha mnzake mwangozi ankathawira ku mizinda imeneyi. Munthu wolipsira sankaloledwa kuti aphe munthu wothawayo ngati mlandu wake sunazengedwe pamaso pa gulu lonse.

Священное Писание (Восточный перевод), версия для Таджикистана

Иешуа 20:1-9

Города-убежища

(Чис. 35:6-34; Втор. 4:41-43; 19:1-14)

1Вечный сказал Иешуа:

2– Повели исроильтянам выбрать города-убежища, как Я говорил вам через Мусо, 3чтобы всякий, кто убьёт другого человека случайно и неумышленно, мог убежать туда и найти защиту от мстителя за кровь. 4Когда он убежит в один из этих городов, то пусть встанет у городских ворот20:4 Ворота города были центром всей общественной жизни, около них проходили и судебные разбирательства. и изложит своё дело перед старейшинами того города. После этого пусть они примут его в свой город и дадут ему место, чтобы он мог жить там. 5Если мститель за кровь станет преследовать его, они не должны выдавать обвиняемого, потому что он убил неумышленно и не питал к убитому ненависти. 6Пусть он остаётся в том городе, пока не предстанет перед обществом на суд или пока не умрёт главный священнослужитель, который будет в то время. Потом он может вернуться в свой дом, в город, из которого убежал.

7И они отделили Кедеш в Галилее в нагорьях Неффалима, Шахем в нагорьях Ефраима и город Кириат-Арбу (то есть Хеврон) в нагорьях Иуды. 8На восточной стороне Иордана, что близ Иерихона, они выбрали Бецер в пустыне на плоскогорье в роду Рувима, Рамот в Галааде в роду Гада и Голан в Бошоне в роду Манассы. 9Всякий исроильтянин или живущий среди них чужеземец, который убивал кого-либо неумышленно, мог убежать в эти выбранные города и не погибнуть от руки мстителя за кровь, пока не предстанет перед обществом на суд.