Yoswa 2 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 2:1-24

Rahabe ndi Anthu Ozonda Dziko

1Tsono Yoswa mwana wa Nuni anatuma anthu awiri okazonda dziko mwachinsinsi kuchokera ku Sitimu. Iye anawawuza kuti, “Pitani mukaone dzikolo makamaka mzinda wa Yeriko.” Kotero iwo anapita ndipo anakafika ku nyumba ya mkazi wadama dzina lake Rahabe, ndipo anagona kumeneko.

2Mfumu ya Yeriko inawuzidwa kuti, “Aisraeli ena afika mu mzinda muno usiku uno kudzazonda dziko.” 3Choncho Mfumu ya Yeriko inatumiza uthenga kwa Rahabe kuti, “Atulutse anthu amene abwera ku nyumba kwakowo chifukwa iwo abwera kuti adzazonde dzikoli.”

4Koma pa nthawiyi nʼkuti mkaziyo atatenga amuna awiriwo ndi kuwabisa. Tsono anayankha kuti, “Inde, anthuwo anafikadi ku nyumba kuno. Koma sindinadziwe kumene anachokera. 5Iwo achoka kuno ndi chisisira, chipata cha mzinda chili pafupi kutsekedwa. Ndiye sindidziwa kumene alowera. Koma mukawalondola msanga muwapeza.” 6Koma nʼkuti atawakweza pa denga azondiwo ndi kuwabisa pansi pa mapesi a thonje amene iye anawayika pa dengapo. 7Nthumwi za mfumu zija zitatuluka ndipo chipata chinatsekedwa. Nthumwizo zinapita kukawafunafuna azondi aja mpaka ku dooko la Yorodani.

8Azondiwo asanagone, Rahabe anakwera pa denga 9ndipo anawawuza kuti, “Ine ndikudziwa kuti Yehova wakupatsani dziko lino ndipo tili ndi mantha. Anthu onse a mʼdziko lino ali ndi mantha chifukwa cha inu. 10Ife tinamva mmene Yehova anawumitsira madzi a Nyanja Yofiira inu mukufika pamene munatuluka mʼdziko la Igupto. Tamvanso zimene munachita kwa Sihoni ndi Ogi, mafumu awiri a Aamori amene ali kummawa kwa Yorodani. Inu munawawononga kotheratu. 11Titamva zimenezi, ife tinataya mtima ndipo aliyense wa ife ali ndi mantha chifukwa cha inu. Tikudziwa kuti Yehova Mulungu wanu ndi Mulungu wa kumwamba ndi dziko lapansi. 12Choncho mulumbire pamaso pa Yehova ndi kundipatsa chizindikiro choti mudzachitadi zimene mwalonjeza, kuti monga inu ndakuchitirani chifundo, inunso mudzachitira chifundo a pa banja la abambo anga. 13Inu mulonjeze kuti simudzapha abambo anga ndi amayi anga, abale anga ndi alongo anga ndi mabanja awo omwe.”

14Anthuwo anamuyankha kuti, “Ife ndife okonzeka kufa chifukwa cha inu. Ngati iwe sudzawulula zimene tachitazi, ndiye kuti ife tidzakukomera mtima ndi kusunga pangano lathu ndi iwe, Yehova akadzatipatsa dziko lino.”

15Popeza nyumba ya Rahabe inali pa linga la mzindawo, azondi aja anatulukira pa zenera. Rahabe anawatsitsa pansi ndi chingwe. 16Iye anawawuza kuti, “Pitani ku mapiri kuti okuthamangiraniwo asakupezeni. Mukabisale kumeneko masiku atatu mpaka iwo atabwerera, ndipo kenaka muzikapita kwanu.”

17Anthuwo anati kwa iye, “Lonjezo limene watichititsa ifeli tidzalisungadi 18tikadzalowa mʼdzikoli, iwe udzamangirire kansalu kofiira pa zenera limene unatitulutsira, ndi kusonkhanitsa abambo ako, amayi ako, abale ako ndi banja lako lonse mʼnyumba muno. 19Ngati wina aliyense adzatuluka mʼnyumbamo kuti azikayendayenda mu msewu, magazi ake adzakhala pamutu pake, ife sitidzapalamula kanthu. Koma wina aliyense wokhala mʼnyumba mwakomo akadzaphedwa, mlandu udzakhala wathu. 20Komanso iwe ukangowulula zimene ife tikuchitazi ndiye kuti ife sitidzasunga zimene talonjezazi.”

21Rahabe anayankha kuti, “Zikhale monga mwaneneramo.” Kenaka iye anawatulutsa ndipo iwowo anapita. Pambuyo pake Rahabe anamangirira kansalu kofiira pa zenera paja.

22Azondi aja anachoka napita ku mapiri ndipo anakhalako masiku atatu. Apa nʼkuti otumidwa ndi mfumu aja atawafunafuna ponseponse nʼkubwerera osawapeza. 23Pambuyo pake azondi awiri aja anayamba ulendo wobwerera kwawo. Anatsika ku mapiri kuja, nawoloka mtsinje mpaka anakafika kwa Yoswa mwana wa Nuni. Ndipo anamuwuza zonse zimene zinawachitikira. 24Iwo anati kwa Yoswa, “Ndithu, Yehova wapereka dziko lonse mʼmanja mwathu. Anthu onse kumeneko akuchita nafe mantha.”

Thai New Contemporary Bible

โยชูวา 2:1-24

นางราหับกับสายสืบ

1แล้วโยชูวาบุตรนูนส่งสายสืบสองคนไปจากชิทธีมอย่างลับๆ และสั่งว่า “จงไปสืบดูสภาพดินแดนนั้น โดยเฉพาะที่เมืองเยรีโค” คนทั้งสองเข้าไปถึงบ้านของหญิงโสเภณี2:1 หรืออาจจะเป็นเจ้าของที่พักแรมก็ได้ชื่อราหับและพักอยู่ที่นั่น

2มีคนไปบอกกษัตริย์เยรีโคว่า “ดูเถิด! มีชาวอิสราเอลบางคนเข้ามาเมื่อคืนเพื่อมาสืบดูดินแดนนี้” 3ดังนั้นกษัตริย์เยรีโคจึงส่งคนมาสั่งนางราหับว่า “จงนำตัวคนที่มาพักในบ้านของเจ้าออกมา เพราะพวกเขาเป็นสายสืบมาสืบดูทั่วทั้งดินแดนของเรา”

4แต่นางได้ซ่อนตัวคนทั้งสองไว้แล้ว นางจึงเรียนว่า “พวกเขามาที่นี่ แต่ดิฉันไม่ทราบว่าเขามาจากไหน 5เขาออกจากเมืองไปตอนพลบค่ำ ใกล้เวลาปิดประตูเมือง ดิฉันไม่ทราบว่าเขาไปทางไหน ถ้าพวกท่านรีบตามไปอาจจะทัน” 6(ที่จริงนางพาคนทั้งสองขึ้นไปบนดาดฟ้า และให้ซ่อนตัวอยู่ใต้กองเส้นป่านที่ผึ่งอยู่) 7คนที่กษัตริย์ใช้มาจึงไล่ตามสายสืบไปตามถนนที่ทอดไปยังท่าข้ามแม่น้ำจอร์แดน และทันทีที่ผู้ติดตามออกไป เขาก็ปิดประตูเมือง

8ราหับขึ้นไปพบคนทั้งสองก่อนที่พวกเขาจะเข้านอน 9นางกล่าวกับเขาว่า “ดิฉันทราบดีว่าองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงยกดินแดนนี้ให้ท่าน และเราทุกคนกลัวท่านมาก ดังนั้นทุกคนที่อาศัยอยู่ในประเทศนี้จึงตกอยู่ในความกลัวเพราะท่าน 10เราได้ยินเรื่องที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงให้ทะเลแดงแห้งเป็นทางผ่านแก่พวกท่าน ตอนที่ท่านออกมาจากอียิปต์ และเราได้ยินถึงสิ่งที่ท่านทำกับสิโหนและโอก กษัตริย์ทั้งสองของชาวอาโมไรต์ทางฟากตะวันออกของแม่น้ำจอร์แดนซึ่งท่านทำลายล้างหมดสิ้น2:10 คำนี้ในภาษาฮีบรูหมายถึงสิ่งของหรือบุคคลที่ถวายแด่องค์พระผู้เป็นเจ้าแล้วไม่อาจเรียกคืนได้ มักจะต้องทำลายให้หมดสิ้นไป 11เมื่อได้ฟังแล้วเราทุกคนก็หวาดกลัวขวัญกระเจิง เพราะพระยาห์เวห์พระเจ้าของท่านเป็นพระเจ้าแห่งฟ้าสวรรค์เบื้องบนและแผ่นดินโลกเบื้องล่าง 12บัดนี้ขอท่านโปรดสาบานในพระนามพระยาห์เวห์ว่า ท่านจะแสดงความเมตตาต่อครอบครัวของดิฉันเพราะดิฉันได้เมตตาต่อท่าน โปรดให้เครื่องหมายที่ชัดเจนอย่างหนึ่งไว้ 13ว่าท่านจะไว้ชีวิตบิดามารดา พี่น้องชายหญิงของดิฉันกับคนทั้งหมดของพวกเขา และว่าท่านจะช่วยพวกเราให้รอดพ้นจากความตาย”

14คนทั้งสองให้ความมั่นใจแก่นางว่า “ชีวิตแลกด้วยชีวิต หากเจ้าไม่แพร่งพรายสิ่งที่เราทำอยู่ เราจะซื่อสัตย์และกรุณาเจ้าเมื่อองค์พระผู้เป็นเจ้าประทานดินแดนนี้แก่เรา”

15นางจึงเอาเชือกหย่อนลงทางหน้าต่าง ให้พวกเขาไต่ลงไป เนื่องจากบ้านของนางเป็นส่วนหนึ่งของกำแพงเมือง 16นางบอกพวกเขาว่า “หนีไปซ่อนที่เนินเขาเถิด รออยู่สักสามวันจนกว่าคนที่เที่ยวตามหาท่านกลับเข้ามา แล้วจึงค่อยไป”

17ชายทั้งสองบอกนางว่า “เราจะพ้นจากข้อผูกมัดที่เจ้าให้เราสาบาน 18เมื่อเราบุกเข้ามาในดินแดน ถ้าเจ้าไม่ได้ผูกเชือกสีแดงไว้ที่หน้าต่างซึ่งเจ้าหย่อนเราลงมา และถ้าเจ้าไม่ได้ให้พ่อแม่พี่น้องกับทุกคนในครอบครัวอยู่ในบ้านของเจ้า 19ถ้ามีใครออกไปนอกบ้าน เขาต้องรับผิดชอบชีวิตตัวเอง เราจะไม่รับผิดชอบ ส่วนคนที่อยู่ในบ้านกับเจ้า หากมีใครมาแตะต้อง เราจะรับผิดชอบด้วยชีวิตของเราเอง 20แต่หากเจ้าแพร่งพรายสิ่งที่เราทำอยู่ เราก็จะพ้นจากข้อผูกมัดที่เจ้าให้เราสาบานไว้”

21นางตอบว่า “ตกลงตามที่ท่านว่า” แล้วนางก็ส่งคนทั้งสองไป และผูกเชือกแดงไว้ที่หน้าต่างบานนั้น

22สายสืบทั้งสองขึ้นไปบนเนินเขา ค้างอยู่ที่นั่นสามวัน จนกลุ่มคนที่ตามหาตัวเขากลับมาในเมืองนั้น หลังจากเที่ยวตามหาตลอดทางแล้วไม่พบ 23จากนั้นคนทั้งสองก็ลงจากเนินเขา ลุยข้ามแม่น้ำไปรายงานให้โยชูวาบุตรนูนทราบทุกเหตุการณ์ที่เกิดขึ้นโดยตลอด 24พวกเขากล่าวแก่โยชูวาว่า “องค์พระผู้เป็นเจ้าประทานดินแดนทั้งหมดนั้นแก่เราอย่างแน่นอน ทุกคนที่นั่นหวาดหวั่นขวัญผวาเพราะพวกเรา”