Yoswa 19 – CCL & KLB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 19:1-51

Dziko la Simeoni

1Maere achiwiri anagwera mabanja a fuko la Simeoni. Dziko lawo linali mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda. 2Dzikolo linaphatikiza zigawo izi:

Beeriseba (ndi Seba), Molada, 3Hazari-Suwali, Bala, Ezemu, 4Elitoladi, Betuli, Horima, 5Zikilagi, Beti-Marikaboti, Hazari-Susa, 6Beti-Lebaoti ndi Saruheni. Yonse pamodzi inali mizinda 13 ndi midzi yawo.

7Panalinso mizinda inayi iyi: Aini, Rimoni, Eteri ndi Asani pamodzi ndi midzi yawo. 8Dzikolo linaphatikizanso midzi yonse yozungulira mizinda imeneyi mpaka ku Baalati-Beeri, ndiye kuti Rama wa kummwera.

Ili ndi dziko limene mabanja a fuko la Simeoni analandira kukhala lawo. 9Cholowa cha fuko la Simeoni chinatengedwa kuchokera ku gawo la Yuda chifukwa fuko la Yuda linali lalikulu kwambiri. Izi zinachititsa fuko la Simeoni kukhala mʼkati mwenimweni mwa dziko la Yuda.

Dziko la Zebuloni

10Maere achitatu anagwera mabanja a fuko la Zebuloni:

Malire a dziko lawo anafika mpaka ku Saridi. 11Malirewo anakwera kupita cha kumadzulo ku Marala nakafika ku Dabeseti ndi ku mtsinje wa kummawa kwa Yokineamu. 12Kuchokera ku mbali ina ya Saridi malire anakhota kupita kummawa ku malire a Kisiloti-Tabori mpaka ku Daberati nakwera mpaka ku Yafiya. 13Kuchokera kumeneko anabzola kulowa cha kummawa mpaka ku Gati-Heferi ndi ku Eti Kazini ndi kumaloza ku Neya njira ya ku Rimoni. 14Mbali ya kumpoto malirewo analoza ku Hanatoni ndipo anakathera ku chigwa cha Ifita Eli. 15Anaphatikizapo Katati, Nahalala, Simironi, Idala ndi Betelehemu. Mizinda yonse inakwana khumi ndi iwiri pamodzi ndi midzi yake.

16Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndi imene mabanja a fuko la Zebuloni analandira.

Dziko la Isakara

17Maere achinayi anagwera mabanja a fuko la Isakara. 18Dziko lawo linaphatikiza zigawo izi:

Yezireeli, Kesuloti, Sunemu, 19Hafaraimu, Sioni, Anaharati, 20Rabiti, Kisoni, Ebezi, 21Remeti, Eni Ganimu, Eni Hada ndi Beti-Pazezi. 22Malirewa anakafikanso ku Tabori, Sahazuma ndi Beti-Semesi ndipo anakathera ku Yorodani. Mizinda yonse inalipo 16 ndi midzi yake.

23Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Isakara.

Dziko la Aseri

24Maere achisanu anagwera mabanja a fuko la Aseri. 25Gawo lawo linaphatikiza

Helikati, Hali, Beteni, Akisafu, 26Alameleki, Amadi ndi Misali. Kumadzulo malire anafika ku Karimeli ndi Sihori Libinati. 27Kenaka anakhotera kummawa kulowera ku Beti-Dagoni nafika ku dziko la Zebuloni ndi ku chigwa cha Ifita Eli, ndipo anapita kumpoto ku Beti-Emeki ndi Neieli. Anapitirirabe kumpoto mpaka kukafika ku Kabuli, 28Ebroni, Rehobu, Hamoni, ndi Kana, mpaka ku Sidoni Wamkulu. 29Kenaka malirewo anakhotera ku Rama ndi kupita ku mzinda wotetezedwa wa ku Turo. Kuchokera pamenepo malirewo anakhota kupita ku Hosa nakatulukira ku Nyanja, mʼchigawo cha Akizibu, 30Uma, Afeki ndi Rehobu. Mizinda yonse inalipo 22 pamodzi ndi midzi yake.

31Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Aseri.

Dziko la Nafutali

32Maere achisanu ndi chimodzi anagwera mabanja a fuko la Nafutali.

33Malire awo anayambira ku Helefu mpaka ku mtengo wa thundu wa ku Zaananimu, ndipo anapitirira nʼkukafika ku Adami Nekebu, Yabineeli mpaka ku Lakumi ndi kukathera ku Yorodani. 34Tsono malirewo anakhotera kumadzulo kupita ku Azinoti-Tabori. Kuchoka kumeneko anapita ku Hukoki, modutsa Zebuloni cha kummwera, Aseri cha kumadzulo ndi mtsinje wa Yorodani cha kummawa. 35Mizinda yotetezedwa inali Zidimi, Zeri, Hamati, Rakati, Kinereti, 36Adama, Rama, Hazori, 37Kedesi, Ederi, Eni Hazori, 38Yironi, Migidali Eli, Horemu, Beti-Anati ndi Beti-Semesi. Yonse pamodzi inalipo mizinda 19 ndi midzi yake.

39Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yawo ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Nafutali.

Dziko la Dani

40Maere achisanu ndi chiwiri anagwera mabanja a fuko la Dani. 41Gawo lawo linaphatikiza mizinda iyi:

Zora, Esitaoli, Iri Semesi, 42Saalabini, Ayaloni, Itira, 43Eloni, Timna, Ekroni, 44Eliteke, Gibetoni, Baalati, 45Yehudi, Beni Beraki, Gati-Rimoni, 46Me-Yarikoni ndi Rakoni, pamodzi ndi dera loyangʼanana ndi Yopa.

47Anthu a fuko la Dani atalandidwa dziko lawo, anapita kukathira nkhondo Lesemu. Iwo anapha anthu ake onse, nawulandiratu mzindawo, kuwusandutsa wawo ndi kumakhalamo. Tsono anatcha mzindawo dzina loti Dani popeza ndilo linali dzina la kholo lawo.

48Mizinda yonseyi pamodzi ndi midzi yake ndiyo inali cholowa cha mabanja a fuko la Dani.

Dziko la Yoswa

49Atatha kugawana zigawo zosiyanasiyana za dzikolo, Aisraeli anamupatsa Yoswa mwana wa Nuni chigawo chake. 50Potsata zimene Yehova anawalamula, anamupatsa mzinda wa Timnati-Sera umene anawupempha. Mzindawu unali mʼdziko lamapiri la Efereimu. Iye anawumanga mzindawu ndi kukhazikikako.

51Wansembe Eliezara, Yoswa ndi atsogoleri a mabanja onse a Israeli anagawa dziko lija zigawozigawo pogwiritsa ntchito maere pamaso pa Yehova. Izi zinachitika ku Silo pa khomo la tenti ya msonkhano. Choncho anamaliza kugawa dzikolo.

Korean Living Bible

여호수아 19:1-51

시므온 지파

1두 번째로 시므온 지파를 위해 제비를 뽑았다. 그들은 유다 지파의 땅 중에서 분배받았는데

2그들이 얻은 성은 다음과 같다: 브엘세바 곧 세바, 몰라다,

3하살 – 수알, 발라, 에셈,

4엘돌랏, 브둘, 호르마,

5시글락, 벧 – 말가봇, 하살 – 수사,

6벧 – 르바옷, 사루헨 – 이상 13개의 성과 그 주변 부락들;

7아인, 림몬, 에델, 아산 – 이상 4개의 성과 그 주변 부락들;

8그리고 남쪽으로 라마 곧 바알랏 – 브엘까지 이 성들을 두르고 있는 모든 부락들이었다. 이상은 시므온 지파가 집안별로 분배받은 땅이며

9시므온 지파가 그들의 땅을 유다 지파의 땅 가운데서 분배받은 것은 유다 지파가 분배받은 땅 몫이 그들에게는 너무 컸기 때문이었다.

스불론 지파

10세 번째로 스불론 지파를 위해 제비를 뽑았다. 그들이 분배받은 땅의 경계는 사릿까지 미치고

11거기서 서쪽으로 돌아 마랄라에 이르러 답베셋을 지나 욕느암 동쪽 시내에 미친다.

12그리고 사릿의 다른 방면에서 그 경계선은 동쪽으로 나아가 기슬롯 – 다볼의 경계에 이르고 계속 다브랏으로 가서 야비아로 올라가고

13거기서 가드 – 헤벨과 엣 – 가신 동쪽을 지나 림몬으로 가는 도중에 네아 방면에서 구부러졌다.

14그리고 그 경계선은 한나돈 북쪽을 지나 입다 – 엘 골짜기에서 끝났다.

15스불론 지파가 차지한 성은 갓닷, 나할랄, 시므론, 이달라, 베들레헴을 포함한 12개의 성과 그 주변 부락들이었다.

16이상의 성과 부락은 스불론 지파가 집안별로 분배받은 땅이다.

잇사갈 지파

17네 번째로 잇사갈 지파를 위해 제비를 뽑았다.

18그들이 분배받은 땅은 이스르엘, 그술롯, 수넴,

19하바라임, 시온, 아나하랏,

20랍빗, 기시온, 에베스,

21레멧, 엔 – 간님, 엔 – 핫다, 벧 – 바세스를 포함하며

22그 경계는 다볼, 사하수마, 벧 – 세메스에 미치고 요단강에서 끝났다.

23이상의 16개 성과 그 주변 부락은 잇사갈 지파가 집안별로 분배받은 땅이다.

아셀 지파

24다섯 번째로 아셀 지파를 위해 제비를 뽑았다.

25그들이 분배받은 땅은 헬갓, 할리, 베덴, 악삽,

26알람멜렉, 아맛, 미살을 포함하며 그들의 경계선은 서쪽 갈멜에서부터 시홀 – 림낫에 미치고

27거기서 동쪽으로 돌아 벧 – 다곤으로 가서 스불론과 입다 – 엘 골짜기에 미치고 벧 – 에멕과 느이엘에 이른 다음 북쪽으로 올라가서 가불을 지나

28에브론, 르홉, 함몬, 가나를 지나 큰 시돈까지 이르고

29다시 라마쪽으로 돌아 요새화된 두로에 미치고 호사로 내려가 지중해에서 끝났다. 또 그들의 영토는 마할랍, 악십,

30움마, 아벡, 르홉을 포함하여 모두 22개의 성과 그 주변 부락들이었다.

31이상은 아셀 지파가 집안별로 분배받은 땅이다.

납달리 지파

32여섯 번째로 납달리 지파를 위해 제비를 뽑았다.

33그들의 경계선은 헬렙에서 시작하여 사아난님 상수리나무에 이르러 아다미 – 네겝, 얍느엘, 락굼을 지나 요단강에서 끝났다.

34그리고 다른 방면에서 그 경계선은 헬렙 부근에서 시작하여 아스놋 – 다볼을 지나 훅곡에 이르렀다. 그래서 납달리 지파의 땅은 남쪽으로 스불론 땅과 접하고 서쪽으로 아셀 땅과 접하며 동쪽으로는 요단강과 접하였다.

35그리고 납달리 지파의 요새화된 성들은 싯딤, 세르, 함맛, 락갓, 긴네렛,

36아다마, 라마, 하솔,

37게데스, 에드레이, 엔 – 하솔,

38이론, 믹달 – 엘, 호렘, 벧 – 아낫, 벧 – 세메스이며 그들의 땅은 모두 19개 성과 그 주변 부락들이었다.

39이상은 납달리 지파가 집안별로 분배받은 땅이다.

단 지파

40마지막으로 단 지파를 위해 제비를 뽑았다.

41그들이 분배받은 땅은 소라, 에스다올, 이르 – 세메스,

42사알랍빈, 아얄론, 이들라,

43엘론, 딤나, 에그론,

44엘드게, 깁브돈, 바알랏,

45여훗, 브네 – 브락, 가드 – 림몬,

46메 – 얄곤, 락곤, 그리고 욥바 일대의 지역이었다.

47-48이상은 단 지파가 집안별로 분배받은 땅이다. 그러나 단 지파는 자기들이 분배받은 땅을 잃어버렸다. 그래서 그들은 19:47-48 히 ‘레셈’라이스로 올라가서 그 곳 주민들을 쳐죽이고 그 땅을 점령하여 거기서 정착하였다. 그리고 그들은 자기들 조상의 이름을 따서 그 곳을 단이라고 불렀다.

여호수아가 얻은 땅

49이스라엘 백성은 땅의 분배 작업이 끝났을 때 자기들 땅 중에서 한 곳을 눈의 아들 여호수아에게 주었다.

50그들은 여호와의 명령대로 여호수아가 요구한 성 곧 에브라임 산간 지대에 있는 딤낫 – 세라를 주었는데 그는 그 성을 재건하고 그 곳에서 살았다.

51이상은 제사장 엘르아살과 눈의 아들 여호수아와 이스라엘 지파의 지도자들이 실로의 성막 입구에 모여 여호와 앞에서 제비 뽑아 나누어 준 땅이다. 이렇게 하여 땅 분배 작업은 완전히 끝났다.