Yoswa 15 – CCL & CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 15:1-63

Dziko Limene Yuda Analandira

1Chigawo cha dzikolo chimene mabanja a fuko la Yuda analandira chinafika ku malire ndi Edomu mpaka ku chipululu cha Zini kummwera kwenikweni.

2Malire awo a kummwera anayambira kummwera kwenikweni kwa Nyanja ya Mchere, 3kudutsa cha kummwera ku Akirabimu, nʼkupitirira mpaka ku Zini. Kuchokera pamenepo nʼkumapita cha kummwera kwa Kadesi Barinea, kudutsa Hezironi mpaka ku Adari ndi kutembenuka mpaka ku Karika. 4Anapitirira mpaka ku Azimoni motsata mtsinje umene uli malire a Igupto mpaka ku nyanja. Awa ndiwo malire awo a kummwera.

5Malire a kummawa anali Nyanja Yakufa mpaka kumene Yorodani amathira mu Nyanja ya Mchere.

Malire a kumpoto anayambira kumene Yorodani amathirira nyanjayo, 6napitirira mpaka ku Beti-Hogila ndi kupitirira kumpoto mpaka ku Beti-Araba. Anapitirira mpaka anakafika ku Mwala wa Bohani. 7Ndipo malirewo anachokeranso ku chigwa cha Akori mpaka ku Debri, kuchokera ku chigwa cha Akori ndi kutembenukira kumpoto ku Giligala, dera limene linayangʼanana ndi msewu wa Adumimu kummwera kwa chigwa. Anapitirira mpaka ku madzi a ku Eni Semesi ndi kutulukira ku Eni Rogeli. 8Ndipo anapitirira mpaka ku chigwa cha Hinomu mbali ya kummwera kwa mzinda wa Ayebusi (mzinda wa Yerusalemu). Kuchokera kumeneko anakwera mpaka pamwamba pa phiri kumadzulo kwa chigwa cha Hinomu cha kumpoto kwenikweni kwa chigwa cha Refaimu. 9Ndipo anachokeranso pamwamba pa phiri, kukafika mpaka ku akasupe a ku Nepitowa, nadzatulukira ku mizinda ya phiri la Efroni, ndi kutsikira ku Baalahi (ndiye Kiriati Yearimu). 10Kuchokera kumeneko anazungulira cha kumadzulo ku Baalahi mpaka ku phiri la Seiri. Anapitirira cha kumpoto kutsata phiri la Yearimu (lomwe ndi Kesaloni). Anapitirirabe kutsika ku Beti Semesi ndi kuwolokera ku Timna. 11Malirewo anapitirira kumatsitso a mapiri chakumpoto kwa Ekroni, ndi kukhotera ku Sikeroni. Malirewo anadutsa phiri la Baalahi ndi kufika ku Yabineeli. Malirewo anathera ku nyanja.

12Malire a mbali ya kumadzulo anali Nyanja Yayikulu.

Awa ndi malire ozungulira malo amene anapatsidwa kwa mabanja a fuko la Yuda.

13Potsata lamulo la Yehova, Yoswa anapereka kwa Kalebe mwana wa Yefune gawo lina la dziko la Yuda dera la Kiriati Ariba, limene ndi Hebroni. (Ariba anali gogo wa Aanaki). 14Kuchokera ku Hebroni, Kalebe anathamangitsamo mafuko a Aanaki awa: Sesai, Ahimani ndi Talimai, zidzukulu za Aanaki. 15Kuchokera kumeneko, Kalebe anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi). 16Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.” 17Otanieli, mwana wa mʼbale wa Kalebe, Kenazi, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.

18Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani.”

19Iye anayankha kuti “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.

20Dziko limene mabanja a fuko la Yuda analandira ngati cholowa chawo ndi ili:

21Mizinda yakummwera kwenikweni kwa fuko la Yuda yoyandikana ndi malire a Edomu anali:

Kabizeeli, Ederi, Yaguri 22Kina, Dimona, Adada 23Kedesi, Hazori, Itinani 24Zifi, Telemu, Bealoti, 25Hazori-Hadata, Keriyoti Hezironi (ndiye kuti Hazori) 26Amamu, Sema, Molada 27Hazari-Gada, Hesimoni, Beti-Peleti 28Hazari-Suwali, Beeriseba, Biziotiya, 29Baalahi, Iyimu, Ezemu 30Elitoladi, Kesili, Horima 31Zikilagi, Madimena, Sanisana, 32Lebaoti, Silihimu, Aini ndi Rimoni. Mizinda yonse inalipo 29 pamodzi ndi midzi yake yozungulira.

33Mizinda ya ku chigwa cha kumadzulo ndi iyi:

Esitaoli, Zora, Asina 34Zanowa, Eni-Ganimu, Tapuwa, Enamu, 35Yarimuti, Adulamu, Soko, Azeka, 36Saaraimu, Aditaimu, ndi Gederi (kapena Gederotaimu). Mizinda yonse inalipo 14 pamodzi ndi midzi yake yozungulira.

37Mizinda ina inali iyi: Zenani, Hadasa, Migidali-Gadi, 38Dileani, Mizipa, Yokiteeli, 39Lakisi, Bozikati, Egiloni, 40Kaboni, Lahimasi, Kitilisi, 41Gederoti, Beti-Dagoni, Naama ndi Makeda. Mizinda yonse pamodzi inalipo 16 pamodzi ndi midzi yake yozungulira.

42Mizinda ina inali iyi: Libina, Eteri, Asani, 43Ifita, Asina, Nezibu, 44Keila, Akizibu ndi Maresa, mizinda isanu ndi inayi pamodzi ndi midzi yake.

45Panalinso Ekroni pamodzi ndi midzi yake; 46komanso yonse imene inali mʼmbali mwa Asidodi ndi midzi yake kuyambira ku Ekroni mpaka ku Nyanja Yayikulu. 47Panalinso mizinda ya Asidodi ndi Gaza pamodzi ndi midzi yawo. Malire ake anafika ku mtsinje wa Igupto mpaka ku Nyanja Yayikulu.

48Mizinda ya kumapiri inali:

Samiri, Yatiri, Soko, 49Dana, Kiriati-Sana, (ndiye kuti Debri) 50Anabu, Esitemo, Animu, 51Goseni, Holoni ndi Gilo. Mizinda yonse pamodzi inali khumi ndi umodzi pamodzi ndi midzi yake.

52Analandiranso mizinda iyi: Arabu, Duma, Esani, 53Yanumu, Beti-Tapuwa, Afeki 54Humita, Kiriati-Ariba (ndiye kuti Hebroni) ndi Ziori, mizinda isanu ndi inayi pamodzi ndi midzi yake.

55Panalinso Maoni, Karimeli, Zifi, Yuta 56Yezireeli, Yokideamu, Zanowa, 57Kaini, Gibeya ndi Timna, mizinda khumi ndi midzi yake.

58Mizinda ina inali: Halihuli, Beti Zuri, Gedori, 59Maarati, Beti-Anoti ndi Elitekoni, mizinda isanu ndi umodzi pamodzi ndi midzi yake

60Panalinso Kiriati Baala (ndiye kuti Kiriati Yearimu) ndi Raba; mizinda iwiri pamodzi ndi midzi yake.

61Mizinda ya ku chipululu inali iyi:

Beti-Araba, Midini, Sekaka, 62Nibisani, Mzinda wa Mchere ndi Eni Gedi, mizinda isanu ndi umodzi pamodzi ndi midzi yake.

63Koma Yuda sanathe kuthamangitsa Ayebusi amene amakhala ku Yerusalemu, ndipo mpaka lero Ayebusi akukhala komweko pamodzi ndi Ayudawo.

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 15:1-63

Dziko Limene Yuda Analandira

1Chigawo cha dzikolo chimene mabanja a fuko la Yuda analandira chinafika ku malire ndi Edomu mpaka ku chipululu cha Zini kummwera kwenikweni.

2Malire awo a kummwera anayambira kummwera kwenikweni kwa Nyanja ya Mchere, 3kudutsa cha kummwera ku Akirabimu, nʼkupitirira mpaka ku Zini. Kuchokera pamenepo nʼkumapita cha kummwera kwa Kadesi Barinea, kudutsa Hezironi mpaka ku Adari ndi kutembenuka mpaka ku Karika. 4Anapitirira mpaka ku Azimoni motsata mtsinje umene uli malire a Igupto mpaka ku nyanja. Awa ndiwo malire awo a kummwera.

5Malire a kummawa anali Nyanja Yakufa mpaka kumene Yorodani amathira mu Nyanja ya Mchere.

Malire a kumpoto anayambira kumene Yorodani amathirira nyanjayo, 6napitirira mpaka ku Beti-Hogila ndi kupitirira kumpoto mpaka ku Beti-Araba. Anapitirira mpaka anakafika ku Mwala wa Bohani. 7Ndipo malirewo anachokeranso ku chigwa cha Akori mpaka ku Debri, kuchokera ku chigwa cha Akori ndi kutembenukira kumpoto ku Giligala, dera limene linayangʼanana ndi msewu wa Adumimu kummwera kwa chigwa. Anapitirira mpaka ku madzi a ku Eni Semesi ndi kutulukira ku Eni Rogeli. 8Ndipo anapitirira mpaka ku chigwa cha Hinomu mbali ya kummwera kwa mzinda wa Ayebusi (mzinda wa Yerusalemu). Kuchokera kumeneko anakwera mpaka pamwamba pa phiri kumadzulo kwa chigwa cha Hinomu cha kumpoto kwenikweni kwa chigwa cha Refaimu. 9Ndipo anachokeranso pamwamba pa phiri, kukafika mpaka ku akasupe a ku Nepitowa, nadzatulukira ku mizinda ya phiri la Efroni, ndi kutsikira ku Baalahi (ndiye Kiriati Yearimu). 10Kuchokera kumeneko anazungulira cha kumadzulo ku Baalahi mpaka ku phiri la Seiri. Anapitirira cha kumpoto kutsata phiri la Yearimu (lomwe ndi Kesaloni). Anapitirirabe kutsika ku Beti Semesi ndi kuwolokera ku Timna. 11Malirewo anapitirira kumatsitso a mapiri chakumpoto kwa Ekroni, ndi kukhotera ku Sikeroni. Malirewo anadutsa phiri la Baalahi ndi kufika ku Yabineeli. Malirewo anathera ku nyanja.

12Malire a mbali ya kumadzulo anali Nyanja Yayikulu.

Awa ndi malire ozungulira malo amene anapatsidwa kwa mabanja a fuko la Yuda.

13Potsata lamulo la Yehova, Yoswa anapereka kwa Kalebe mwana wa Yefune gawo lina la dziko la Yuda dera la Kiriati Ariba, limene ndi Hebroni. (Ariba anali gogo wa Aanaki). 14Kuchokera ku Hebroni, Kalebe anathamangitsamo mafuko a Aanaki awa: Sesai, Ahimani ndi Talimai, zidzukulu za Aanaki. 15Kuchokera kumeneko, Kalebe anakathira nkhondo anthu amene ankakhala ku Debri (mzindawu poyamba unkatchedwa Kiriati Seferi). 16Tsono Kalebe anati, “Munthu amene angathire nkhondo mzinda wa Kiriati Seferi ndi kuwulanda, ndidzamupatsa mwana wanga Akisa kuti akhale mkazi wake.” 17Otanieli, mwana wa mʼbale wa Kalebe, Kenazi, ndiye anawulanda. Choncho Kalebe anamupatsa mwana wake Akisa kuti akhale mkazi wake.

18Tsiku lina atafika Akisayo, Otanieli anamuwumiriza mkazi wakeyo kuti apemphe munda kwa Kalebe abambo ake. Pamene Akisa anatsika pa bulu wake, Kalebe anamufunsa kuti, “Kodi ukufuna ndikuchitire chiyani.”

19Iye anayankha kuti “Mundikomere mtima. Popeza mwandipatsa ku Negevi, kumalo kumene kulibe madzi, mundipatsenso akasupe amadzi.” Choncho Kalebe anamupatsa akasupe a kumtunda ndi a kumunsi.

20Dziko limene mabanja a fuko la Yuda analandira ngati cholowa chawo ndi ili:

21Mizinda yakummwera kwenikweni kwa fuko la Yuda yoyandikana ndi malire a Edomu anali:

Kabizeeli, Ederi, Yaguri 22Kina, Dimona, Adada 23Kedesi, Hazori, Itinani 24Zifi, Telemu, Bealoti, 25Hazori-Hadata, Keriyoti Hezironi (ndiye kuti Hazori) 26Amamu, Sema, Molada 27Hazari-Gada, Hesimoni, Beti-Peleti 28Hazari-Suwali, Beeriseba, Biziotiya, 29Baalahi, Iyimu, Ezemu 30Elitoladi, Kesili, Horima 31Zikilagi, Madimena, Sanisana, 32Lebaoti, Silihimu, Aini ndi Rimoni. Mizinda yonse inalipo 29 pamodzi ndi midzi yake yozungulira.

33Mizinda ya ku chigwa cha kumadzulo ndi iyi:

Esitaoli, Zora, Asina 34Zanowa, Eni-Ganimu, Tapuwa, Enamu, 35Yarimuti, Adulamu, Soko, Azeka, 36Saaraimu, Aditaimu, ndi Gederi (kapena Gederotaimu). Mizinda yonse inalipo 14 pamodzi ndi midzi yake yozungulira.

37Mizinda ina inali iyi: Zenani, Hadasa, Migidali-Gadi, 38Dileani, Mizipa, Yokiteeli, 39Lakisi, Bozikati, Egiloni, 40Kaboni, Lahimasi, Kitilisi, 41Gederoti, Beti-Dagoni, Naama ndi Makeda. Mizinda yonse pamodzi inalipo 16 pamodzi ndi midzi yake yozungulira.

42Mizinda ina inali iyi: Libina, Eteri, Asani, 43Ifita, Asina, Nezibu, 44Keila, Akizibu ndi Maresa, mizinda isanu ndi inayi pamodzi ndi midzi yake.

45Panalinso Ekroni pamodzi ndi midzi yake; 46komanso yonse imene inali mʼmbali mwa Asidodi ndi midzi yake kuyambira ku Ekroni mpaka ku Nyanja Yayikulu. 47Panalinso mizinda ya Asidodi ndi Gaza pamodzi ndi midzi yawo. Malire ake anafika ku mtsinje wa Igupto mpaka ku Nyanja Yayikulu.

48Mizinda ya kumapiri inali:

Samiri, Yatiri, Soko, 49Dana, Kiriati-Sana, (ndiye kuti Debri) 50Anabu, Esitemo, Animu, 51Goseni, Holoni ndi Gilo. Mizinda yonse pamodzi inali khumi ndi umodzi pamodzi ndi midzi yake.

52Analandiranso mizinda iyi: Arabu, Duma, Esani, 53Yanumu, Beti-Tapuwa, Afeki 54Humita, Kiriati-Ariba (ndiye kuti Hebroni) ndi Ziori, mizinda isanu ndi inayi pamodzi ndi midzi yake.

55Panalinso Maoni, Karimeli, Zifi, Yuta 56Yezireeli, Yokideamu, Zanowa, 57Kaini, Gibeya ndi Timna, mizinda khumi ndi midzi yake.

58Mizinda ina inali: Halihuli, Beti Zuri, Gedori, 59Maarati, Beti-Anoti ndi Elitekoni, mizinda isanu ndi umodzi pamodzi ndi midzi yake

60Panalinso Kiriati Baala (ndiye kuti Kiriati Yearimu) ndi Raba; mizinda iwiri pamodzi ndi midzi yake.

61Mizinda ya ku chipululu inali iyi:

Beti-Araba, Midini, Sekaka, 62Nibisani, Mzinda wa Mchere ndi Eni Gedi, mizinda isanu ndi umodzi pamodzi ndi midzi yake.

63Koma Yuda sanathe kuthamangitsa Ayebusi amene amakhala ku Yerusalemu, ndipo mpaka lero Ayebusi akukhala komweko pamodzi ndi Ayudawo.