Yoswa 13 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 13:1-33

Mayiko Otsala Oyenera Kulandidwa

1Yoswa atakalamba Yehova anamuwuza kuti, Iwe tsopano wakalamba kwambiri, koma dziko losalandidwa lilipobe lalikulu.

2“Madera amene atsala ndi awa: chigawo chonse cha Afilisti ndi Agesuri 3kuchokera ku mtsinje wa Sihori kummawa kwa Igupto mpaka kumpoto kwa dziko la Ekroni. Madera onse amawerengedwa kuti ndi a Akanaani ngakhale amalamulidwa ndi mafumu asanu a Afilisti a ku Gaza, Asidodi, Asikeloni, Gati, Ekroni ndi Agiti, komanso ku Avimu ku chigawo cha kumpoto. 4Dziko lina la Akanaani ndi Ameara limene lili mʼmanja mwa Asidoni mpaka ku Afeki, dziko limene linachitana malire ndi dziko la Aamori. 5Palinso dziko lonse la Gebala ndi Lebanoni cha kummawa kuyambira ku Baala-Gadi pa tsinde pa phiri la Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.

6“Palinso anthu okhala mʼchigawo cha ku mapiri kuchokera ku Lebanoni mpaka ku Misirefoti-Maimu, Ine ndidzawapirikitsa pamene Aisraeli azidzalowa. Tsono uwagawire Aisraeli dziko limeneli kuti likhale cholowa chawo monga momwe ndakulamulira. 7Tsopano ugawire dziko limeneli mafuko asanu ndi anayi ndiponso theka la fuko la Manase, kuti likhale cholowa chawo.”

Kugawidwa kwa Dziko la Kummawa kwa Yorodani

8Anthu a fuko la Rubeni ndi fuko la Gadi pamodzi ndi theka lina la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo chimene Mose mtumiki wa Yehova anawapatsa. Cholowa chawocho chinali kummawa kwa mtsinje wa Yorodani.

9Dziko lawolo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, ndiponso mzinda umene uli pakati pa chigwacho. Dzikolo linkaphatikizanso dera lonse lokwera kuyambira ku Medeba mpaka ku Diboni. 10Linkaphatikizanso mizinda yonse ya mfumu Sihoni ya Aamori, imene inkalamulira mu Hesiboni, mpaka ku malire a Aamoni. 11Dzikoli linaphatikizanso Giliyadi, dziko la anthu a ku Gesuri ndi Maaka, phiri lonse la Herimoni ndi dziko lonse la Basani mpaka ku Saleka. 12Linaphatikizanso dziko la mfumu Ogi ya ku Basani imene imalamulira kuchokera ku Asiteroti ndi Ederi. Iye yekha ndiye anali mfumu ya Arefaimu amene anapulumuka. Mose anali atawagonjetsa anthu amenewa ndi kuwathamangitsira kutali. 13Koma Aisraeli sanathamangitse anthu a ku Gesuri ndi Maaka, kotero iwowa amakhalabe pakati pawo mpaka lero.

14Koma Mose sanapereke dziko kwa fuko la Alevi popeza zopereka zopatulika zimene anthu ankapereka kwa Yehova, Mulungu wa Israeli, ndizo zinali cholowa chawo monga Yehova anawalonjezera.

15Mose anapereka gawo lina la dziko kwa mabanja a fuko la Rubeni.

16Dziko lawo linayambira ku Aroeri mzinda umene uli pafupi ndi chigwa cha Arinoni, mʼmudzi wa pakati pa chigwa, ndiponso dera lonse lokwera mpaka ku Medeba. 17Dzikolo linaphatikizanso Hesiboni ndi mizinda yake yonse, komanso mizinda monga Diboni, Bamoti Baala, Beti-Baala-Meoni, 18Yahaza, Kedemoti, Mefaati. 19Kiriataimu, Sibima, Zereti-Sahari, pa phiri limene lili mʼchigwa, 20Beti-Peori, ku matsitso a Pisiga, ndiponso Beti-Yesimoti. 21Dzikolo linaphatikizanso mizinda yonse ya ku madera okwera ndiponso dziko lonse la mfumu Sihoni ya Aamori amene ankalamulira kuchokera ku Hesiboni. Mose anamugonjetsa iye pamodzi ndi mafumu a Amidiyani awa: Evi, Rekemu, Zuri, Huri ndi Reba, mafumu amene anagwirizana ndi Sihoni. Onsewa analamulira dzikolo ngati nduna za Sihoni. 22Kuwonjezera pa amene anaphedwa ndi nkhondo, Aisraeli anapha ndi lupanga Balaamu mwana wa Beori, amene amachita za matsenga. 23Malire a fuko la Rubeni anali mtsinje wa Yorodani. Mizinda imeneyi pamodzi ndi midzi yake zinapatsidwa kwa mabanja a fuko la Rubeni kuti akhale cholowa chawo.

24Dera limene Mose anapereka kwa mabanja a fuko la Gadi ndi ili:

25Dziko la Yazeri, mizinda yonse ya mu Giliyadi ndiponso theka la dziko la Amori kukalekezera ku Aroeri, kufupi ndi Raba; 26ndiponso kuyambira ku Hesiboni mpaka ku Ramati-Mizipa, ndi Betonimu; ndiponso kuyambira ku Mahanaimu mpaka ku dziko la Debri. 27Mu chigwa cha Yorodani analandiramo Beti-Haramu, Beti-Nimira, Sukoti ndi Zafoni pamodzi ndi dziko lonse la mfumu Sihoni ya ku Hesiboni. Malire ake a ku madzulo anali mtsinje wa Yorodani kufikira ku Nyanja ya Kinereti, kumpoto. 28Mizinda ndi midzi imeneyi inali cholowa cha mabanja a fuko la Gadi.

29Mose anali atapereka kale gawo lina la dziko limeneli kwa theka la mabanja a fuko la Manase kuti likhale cholowa chawo.

30Derali linayambira ku Mahanaimu kuphatikizapo dziko lonse la mfumu Ogi, Mfumu ya ku Basani, pamodzi ndi mizinda 60 ya ku Yairi, ku Basaniko. 31Derali linaphatikizanso theka la Giliyadi pamodzi ndi Asiteroti ndi Ederi, mizinda yayikulu ya mfumu Ogi wa Basani. Mizinda imeneyi inapatsidwa kwa mabanja a Makiri, mwana wa Manase kuti ikhale cholowa cha theka la ana a Makiri, malinga ndi mabanja awo.

32Umu ndi mmene Mose anagawira malo a mʼchigwa cha Yorodani, kummawa kwa Yeriko, ku tsidya kwa Yorodani. 33Komatu Mose sanapereke malo kwa fuko la Levi. Mose anawawuza kuti zopereka zimene anthu ankapereka kwa Yehova ndizo cholowa chawo.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約書亞記 13:1-33

尚未攻取之地

1約書亞年事已高,耶和華對他說:「你年紀大了,但還有許多地方有待征服, 2就是非利士人和基述人的全境, 3即從埃及東面的西曷河直到北面以革倫的邊境,這一帶都算是迦南,是統治迦薩人、亞實突人、亞實基倫人、迦特人、以革倫人的五個非利士王的地方;南方亞衛人的地方; 4整個迦南人的地方,從西頓人的米亞拉直到亞摩利人邊境的亞弗5迦巴勒人的地方;以及東從黑門山山麓的巴力·迦得直到哈馬口的整個黎巴嫩6我必為以色列人趕走從黎巴嫩米斯利弗·瑪音一帶山區的西頓人。你只管照我的吩咐,把這些土地分給以色列人作產業, 7分給其他九個支派和瑪拿西半個支派作產業。」

約旦河東土地的分配

8瑪拿西半個支派和呂便迦得兩支派已經得到耶和華的僕人摩西約旦河東分給他們的產業: 9亞嫩谷旁的亞羅珥起,包括谷中的城,直到底本的整個米底巴平原, 10以及希實本亞摩利西宏統治的各城,直到亞捫的邊境。 11此外,還包括基列基述人和瑪迦人的疆域、整個黑門山和直到撒迦的整個巴珊地, 12以及巴珊的國土。曾經在亞斯她錄以得來做王,是僅存的利乏音人。摩西打敗了這些人,趕走了他們。 13以色列人卻沒有趕走基述人和瑪迦人,他們到今天還住在以色列人當中。

14摩西並沒有把土地分給利未支派作產業,因為獻給以色列的上帝耶和華的火祭就是他們的產業,正如耶和華對他們的應許。

15以下是摩西按宗族分給呂便支派的產業: 16亞嫩谷的城、谷旁的亞羅珥米底巴附近的整個平原, 17希實本城和希實本平原的所有城邑,即底本巴末·巴力伯·巴力·勉18雅雜基底莫米法押19基列亭西比瑪、谷中山丘上的細列哈·沙轄20伯毗珥毗斯迦山坡和伯·耶西末21平原的各城邑和亞摩利西宏的國土。西宏曾在希實本做王,摩西打敗了他和他的米甸首領以未利金蘇珥戶珥利巴22以色列人所殺的人中有比珥的兒子術士巴蘭23呂便支派的土地以約旦河為界。以上是呂便支派按宗族分到的城邑和村莊。

24以下是摩西按宗族分給迦得支派的土地: 25雅謝基列境內所有的城邑;亞捫人的一半領土,直到拉巴附近的亞羅珥26希實本直到拉抹·米斯巴比多寧,從瑪哈念底璧的邊境; 27還有谷中的伯亞蘭伯·寧拉疏割撒分,就是希實本西宏國中其餘的土地,以約旦河為界,沿東岸直到加利利海的頂端。 28以上這些城邑、村莊便是迦得支派按宗族所分到的產業。

29以下是摩西按宗族分給瑪拿西半個支派的土地: 30瑪哈念開始,包括整個巴珊,就是巴珊的國土及其境內雅珥的六十座城邑, 31還有基列的一半和巴珊的兩座城——亞斯她錄以得來瑪拿西的兒子瑪吉的一半子孫按宗族分到這些土地。

32以上是摩西耶利哥對面約旦河東的摩押平原分給以色列人的產業。 33摩西並沒有分給利未支派任何產業,因為以色列的上帝耶和華就是他們的產業,正如耶和華對他們的應許。