Yoswa 11 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yoswa 11:1-23

Kugonjetsedwa kwa Mafumu a Kumpoto

1Yabini, mfumu ya Hazori, inamva zimene zinachitikazi. Tsono inatumiza uthenga kwa Yobabu mfumu ya Madoni, ndiponso kwa mafumu a ku Simironi ndi Akisafu. 2Inatumizanso uthenga kwa mafumu a kumpoto, kumapiri, ndi mʼchigwa cha Yorodani kummwera kwa nyanja ya Kinereti, ndiponso kumadzulo mʼmbali mwa nyanja pafupi ndi Dori. 3Inatumizanso uthenga kwa Akanaani amene ankakhala kummawa ndi kumadzulo kwa Yorodani. Uthenga unapitanso kwa Aamori, Ahiti, Aperezi ndi Ayebusi amene amakhala mʼdziko la ku mapiri ndiponso kwa Ahivi amene ankakhala mʼmunsi mwa phiri la Herimoni ku chigwa cha Mizipa. 4Mafumuwo anabwera pamodzi ndi ankhondo awo onse. Gulu la ankhondo linali lalikulu ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja. Analinso ndi akavalo ndi magaleta ambiri. 5Mafumu onsewa anasonkhana pamodzi ndipo anamanga misasa yawo ku mtsinje wa Meromu, kuti amenyane ndi Israeli.

6Yehova anati kwa Yoswa, “Usawaope chifukwa mawa nthawi ngati yomwe ino ndidzawapereka kuti muwaphe. Akavalo awo muwadule matsinde ndipo magaleta awo muwatenthe ndi moto.”

7Kotero Yoswa pamodzi ndi gulu lonse la nkhondo anafika kwa adani awo aja ku mtsinje wa Meromu modzidzimutsa ndi kuwathira nkhondo. 8Yehova anawapereka mʼmanja mwa Israeli mwakuti anawagonjetseratu ndi kuwapirikitsa njira yonse mpaka ku Sidoni Wamkulu ndi ku Misirefoti Maimu, ndiponso kummawa ku chigwa cha Mizipa. Onse anaphedwa popanda wopulumuka. 9Yoswa anawachita zimene Yehova analamula. Iye anadula matsinde a akavalo awo ndi kutentha magaleta awo.

10Pambuyo pake Yoswa anabwera nalanda mzinda wa Hazori ndi kupha mfumu yake. (Nthawi imeneyo mzinda wa Hazori unali wopambana mizinda ina yonse). 11Anapha aliyense wa mu mzindamo popanda wotsala wamoyo, ndipo mzinda wa Hazori anawutentha ndi moto.

12Yoswa analanda mizinda yonse ndi mafumu ake. Anthu onse anaphedwa ndi lupanga monga momwe analamulira Mose, mtumiki wa Yehova. 13Israeli sanatenthe mizinda yomangidwa pa zitunda, kupatula mzinda wa Hazori, umene Yoswa anawutentha. 14Aisraeli anatenga zinthu zonse za mʼmizindayi pamodzi ndi ziweto kuti zikhale zawo, koma anapha anthu onse ndi lupanga osasiyako ndi mmodzi yemwe wamoyo. 15Monga momwe Yehova analamulira mtumiki wake Mose, nayenso Mose analamulira Yoswa ndipo Yoswa anachita chilichonse chimene Yehova analamulira Mose.

16Kotero Yoswa analanda dziko lonse: dziko la ku mapiri, dera lonse la Negevi, chigawo chonse cha Goseni, ndi chigwa chake chonse, chigwa cha Yorodani, dziko lonse la lamapiri la Israeli pamodzi ndi chigwa chake chomwe. 17Dziko lolandidwalo linayambira ku phiri la Halaki limene linali ku Seiri mpaka ku Baala-Gadi mʼchigwa cha Lebanoni, kumunsi kwa phiri la Herimoni. Yoswa anagwira ndi kupha mafumu a dziko lonselo 18atachita nawo nkhondo kwa nthawi yayitali. 19Palibe ngakhale ndi mfumu imodzi yomwe imene inachita mgwirizano wa mtendere ndi Aisraeli kupatula Ahivi okhala ku Gibiyoni. Koma mizinda ina yonse anachita kuyigonjetsa pa nkhondo. 20Yehova anali atawumitsa mitima yawo kuti alimbane ndi Aisraeli kuti aphedwe popanda kuchitiridwa chifundo. Izi ndi zimene Yehova analamula Mose kuti zichitidwe.

21Pa nthawi imeneyi Yoswa anapita kukawononga Aanaki okhala mʼdziko lija la ku mapiri ku Hebroni, Debri, Anabu komanso madera onse a ku mapiri a Yuda ndi Israeli. Yoswa anawawononga onse pamodzi ndi mizinda yawo. 22Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatsalako mʼdziko lonse la Israeli; komabe ku Gaza, ku Gati ndi Asidodi kokha ndi kumene anatsalako pangʼono. 23Choncho Yoswa anagonjetsa dziko lonse monga momwe Yehova analamulira Mose. Tsono Yoswa analipereka kwa Aisraeli kuti likhale lawo, fuko lililonse gawo lake.

Anthu onse anapumula, osamenyanso nkhondo.

Священное Писание

Иешуа 11:1-23

Победа над северными царями

1Когда Иавин, царь Хацора, услышал о захвате южных городов, он послал сообщить об этом Иоваву, царю Мадона, царям Шимрона и Ахшафа, 2и царям, которые жили в северных нагорьях, в Иорданской долине к югу от Генисаретского озера11:2 Букв.: «от Киннерета»., в западных предгорьях и на возвышенностях Дора11:2 Или: «в Нафот-Доре». на западе; 3хананеям на востоке и на западе, аморреям, хеттам, перизеям и иевусеям в нагорьях, и хивеям под Хермоном в области Мицпы. 4Они выступили со всеми своими воинами и большим количеством коней и колесниц – огромным войском, многочисленным, как песок на морском берегу. 5Все эти цари объединили свои силы и, придя, расположились станом у реки Мером, чтобы воевать с Исраилом.

6Вечный сказал Иешуа:

– Не бойся их, потому что завтра к этому времени они все будут мертвы. Перережь жилы их коням и сожги их колесницы.

7Иешуа и всё его войско внезапно вышли на них возле реки Мером и напали, 8а Вечный отдал их в руки Исраила. Исраильтяне разбили их и гнались за ними до великого Сидона и Мисрефот-Маима и до долины Мицпа на востоке, пока никого из них не осталось в живых. 9Иешуа поступил с ними так, как сказал ему Вечный – он перерезал жилы их коням и сжёг их колесницы.

10Затем Иешуа повернул назад, взял Хацор и предал его царя мечу. (Хацор был главным из всех этих царств.) 11Всех, кто был в нём, они предали мечу, уничтожив их полностью – никого не оставили в живых; а сам город Иешуа сжёг.

12Он взял все эти царские города и их царей и предал их мечу. Он полностью уничтожил их, как велел Муса, раб Вечного. 13Впрочем, Исраил не сжёг ни один из городов, построенных на возвышенностях, кроме Хацора, который сжёг Иешуа. 14Исраильтяне забирали себе из этих городов всю добычу и скот, а всех жителей предавали мечу, пока не истребили их полностью, никого не оставив в живых. 15Как повелел Вечный Своему рабу Мусе, так Муса повелел Иешуа, а Иешуа исполнил это – он не оставил неисполненным ничего из того, что Вечный повелел Мусе.

16Иешуа захватил всю эту землю: нагорья, весь Негев, всю область Гошен, западные предгорья, Иорданскую долину и горы Исраила с их предгорьями, 17от горы Халак, которая высится к Сеиру, до самого Баал-Гада в Ливанской долине, под горой Хермон. Он захватил всех их царей и, сразив их, предал смерти. 18Долгое время Иешуа воевал с этими царями. 19Кроме хивеев, что в Гаваоне, ни один город не заключил мира с исраильтянами, все их они взяли войной. 20Ведь Сам Вечный ожесточил их сердца, чтобы они воевали с Исраилом, и чтобы не было им пощады, и они были полностью уничтожены, как Вечный повелел Мусе.

21В то время Иешуа пошёл и искоренил анакитов (народ гигантов) в нагорьях: в Хевроне, Девире и Анаве, во всех нагорьях Иуды и во всех нагорьях Исраила. Иешуа полностью уничтожил их и их города. 22На земле Исраила не осталось анакитов, они уцелели лишь в Газе, Гате и Ашдоде. 23Так Иешуа захватил всю ту землю, как говорил Мусе Вечный, и отдал её в наследие исраильтянам по их родовым разделениям. И земля успокоилась от войны.