Yona 4 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 4:1-11

Mkwiyo wa Yona ndi Chifundo cha Yehova

1Koma Yona anakhumudwa kwambiri ndipo anakwiya. 2Iye anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, kodi izi si zimene ndinanena ndikanali kwathu? Nʼchifukwa chaketu ine ndinafulumira kuthawa kupita ku Tarisisi. Ine ndinadziwa kuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wa chikondi chopanda malire, Mulungu amene mumaleka kubweretsa tsoka. 3Ndipo tsopano, Inu Yehova, ingondiphani basi, pakuti ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”

4Koma Yehova anayankha kuti, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye?”

5Yona anatuluka mu mzindamo nakakhala pansi cha kummawa kwa mzindawo. Kumeneko anadzimangira chithando nakhala mʼmenemo mu mthunzi, kudikira kuti aone zimene zichitikire mzindawo. 6Tsono Yehova Mulungu anameretsa msatsi ndi kuyikulitsa kuti ipereke mthunzi kwa Yona kuchotsa mavuto ake; ndipo Yona anasangalala kwambiri chifukwa cha msatsiyo. 7Koma tsiku linalo mmawa, Mulungu anabweretsa mbozi imene inadya msatsiyo ndipo inafota. 8Dzuwa litatuluka, Yehova anabweretsa mphepo yotentha yochokera kummawa, ndipo dzuwa linatentha pamutu pa Yona kotero analenguka nalo. Iye anangofuna atafa, ndipo anati, “Ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”

9Koma Mulungu anati kwa Yona, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye chifukwa cha msatsi?”

Iye anayankha kuti, “Inde nʼkoyenera. Kukwiya kwanga nʼkofuna kufa nako.”

10Koma Yehova anati, “Iwe ukumvera chisoni msatsiwo, ngakhale kuti sunawugwirire ntchito kapena kuwukulitsa. Inamera pa usiku umodzi ndipo inafanso pa usiku umodzi. 11Koma mu Ninive muli anthu opitirira 120,000 amene sadziwa kusiyanitsa kuti chabwino nʼchiti ndipo choyipa nʼchiti, mulinso ziweto zochuluka. Kodi sindiyenera kumvera chisoni mzinda waukulu ngati uwu?”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約拿書 4:1-11

1這事令約拿十分不悅,非常惱怒。 2他向耶和華禱告說:「耶和華啊,我在家鄉的時候豈不早就說過你會這樣做嗎?我知道你是一位有恩典、有憐憫的上帝,不輕易發怒,充滿慈愛,不忍心降災,所以我才急速逃往他施3耶和華啊,求你收回我的性命吧,我死了比活著還好!」 4耶和華對他說:「你這樣大發脾氣合理嗎?」

5於是,約拿跑到城外,在城東為自己搭了一個棚,坐在棚下蔭涼處,要看看尼尼微城究竟會怎樣。 6後來,耶和華上帝安排了一棵蓖麻迅速地長起來,為約拿遮蔭,使他的頭免受日曬。約拿因有這棵蓖麻而非常歡喜。 7第二天黎明的時候,上帝卻安排了一條蟲來咬這棵蓖麻,蓖麻就枯萎了。 8太陽出來的時候,上帝颳起燥熱的東風,烈日把約拿曬得發昏,他就再次求死說:「我死了比活著還好!」

9上帝對約拿說:「你為這棵蓖麻大發脾氣合理嗎?」約拿回答說:「我就是氣死了也合理。」 10耶和華說:「這棵蓖麻不是你種的,也不是你栽培的,它在一夜之間長成,又在一夜之間死去,你尚且如此愛惜, 11我怎能不愛惜這尼尼微大城呢?城中單是連左右手都分不清的人就有十二萬多,還有許多的牲畜。」