Yona 3 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 3:1-10

Yona Apita ku Ninive

1Ndipo Yehova anayankhula ndi Yona kachiwiri kuti, 2“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire uthenga umene ndikupatsa.”

3Yona anamvera mawu a Yehova ndipo anapita ku Ninive. Tsono Ninive unali mzinda waukulu kwambiri; wofunika masiku atatu kuwudutsa. 4Yona analowa mu mzindawo, nayenda ulendo wa tsiku limodzi. Iye ankalalikira kuti, “Atsala masiku makumi anayi kuti Ninive awonongedwe.” 5Anthu a ku Ninive anakhulupirira Mulungu. Analengeza kuti aliyense, wamkulu ndi wamngʼono yemwe asale zakudya ndipo avale chiguduli.

6Mfumu ya ku Ninive itamva nkhaniyi, inatsika pa mpando wake waufumu, nivula mkanjo wake waufumu ndipo inavala chiguduli ndi kukhala pansi pa fumbi. 7Tsono mfumuyo inalengeza mu Ninive kuti,

“Mwa lamulo lochokera kwa mfumu ndi akalonga ake:

“Munthu aliyense kapenanso nyama, ngʼombe kapena nkhosa, zisadye kanthu kalikonse; musazilole kuti zidye kapena kumwa. 8Koma anthu avale ziguduli, ndipo nyamanso aziveke ziguduli. Munthu aliyense azifuwula kwa Mulungu ndi mphamvu zake zonse. Anthuwo asiye makhalidwe awo oyipa ndi machitidwe achiwawa. 9Angadziwe ndani? Mwina Mulungu nʼkutikhululukira ndipo mwa chifundo chake nʼkuleka kutikwiyira, ifeyo osawonongedwa.”

10Mulungu ataona zimene anthuwo anachita, ndi mmene anasiyira makhalidwe awo oyipa, anawachitira chifundo ndipo sanabweretse chiwonongeko chimene anawaopseza nacho.

New International Reader’s Version

Jonah 3:1-10

Jonah Goes to Nineveh

1A message from the Lord came to Jonah a second time. The Lord said, 2“Go to the great city of Nineveh. Announce to its people the message I give you.”

3Jonah obeyed the Lord. He went to Nineveh. It was a very large city. In fact, it took about three days to go through it. 4Jonah began by going one whole day into the city. As he went, he announced, “In 40 days Nineveh will be destroyed.” 5The people of Nineveh believed God’s warning. So they decided not to eat any food for a while. And all of them put on the rough clothing people wear when they’re sad. That’s what everyone did, from the least important of them to the most important.

6Jonah’s warning reached the king of Nineveh. He got up from his throne. He took off his royal robes. He also dressed himself in the clothing of sadness. And then he sat down in the dust. 7Here is the message he sent out to the people of Nineveh.

“I and my nobles give this order.

Don’t let people or animals taste anything. That includes your herds and flocks. People and animals must not eat or drink anything. 8Let people and animals alike be covered with the clothing of sadness. All of you must call out to God with all your hearts. Stop doing what is evil. Don’t harm others. 9Who knows? God might take pity on us. He might not be angry with us anymore. Then we won’t die.”

10God saw what they did. He saw that they stopped doing what was evil. So he took pity on them. He didn’t destroy them as he had said he would.