Yona 2 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 2:1-10

Pemphero la Yona

1Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake. 2Iye anati:

“Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova,

ndipo Iye anandiyankha.

Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo,

ndipo Inu munamva kulira kwanga.

3Munandiponya mʼnyanja yozama,

mʼkati mwenimweni mwa nyanja,

ndipo madzi oyenda anandizungulira;

mafunde anu onse ndi mkokomo wake

zinandimiza.

4Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa

pamaso panu;

komabe ndidzayangʼananso

ku Nyumba yanu yopatulika.’

5Madzi wondimiza anandichititsa mantha,

nyanja yozama inandizungulira;

udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.

6Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri;

mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha.

Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo,

Inu Yehova Mulungu wanga.

7“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine,

ine ndinakumbukira Inu Yehova,

ndipo pemphero langa linafika kwa inu,

ku Nyumba yanu yopatulika.

8“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe

amataya chisomo chawo.

9Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe

ndikuyimba nyimbo yamayamiko.

Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.

Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”

10Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Юнус 2:1-11

Молитва Юнуса

1А Вечный сделал так, что Юнуса проглотила огромная рыба, и Юнус пробыл в желудке рыбы три дня и три ночи. 2Находясь в желудке рыбы, Юнус помолился Вечному, своему Богу.

3Он сказал:

– В беде я к Вечному воззвал,

и Он ответил мне.

Из глубин мира мёртвых я закричал,

и Ты услышал мой крик.

4Ты в пучину меня вверг,

в самое сердце морей,

и потоки окружили меня.

Все Твои волны, все Твои валы

надо мной прошли.

5Я сказал: «Изгнан я от глаз Твоих;

однако я вновь увижу святой храм Твой».

6Воды надо мной сомкнулись,

бездна меня обступила,

и водоросли голову оплели.

7На дно, к основаниям гор я нисшёл,

засовы земли закрылись за мной навек,

но Ты, Вечный, Бог мой,

извлёк меня из могилы живым!

8Когда жизнь угасала во мне,

я вспомнил Вечного,

и дошла молитва моя к Тебе,

в святой храм Твой.

9Те, кто ничтожных идолов чтит,

лишились милости, что могли получить.

10А я с хвалебными песнями

буду жертвы Тебе приносить.

Что обещал, исполню.

Спасение – от Вечного!

11Тогда Вечный повелел огромной рыбе, и она изрыгнула Юнуса на сушу.