Yohane 9 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 9:1-41

Yesu Achiritsa Munthu Wosaona Chibadwire

1Iye akuyendabe, anaona munthu wosaona chibadwire. 2Ophunzira ake anamufunsa Iye kuti, “Rabi anachimwa ndani, munthuyu kapena makolo ake, kuti iye abadwe wosaona?”

3Yesu anayankha kuti, “Sikuti iyeyu anachimwa kapena makolo ake, koma izi zinachitika kuti Mulungu aonetse ntchito zake mwa iyeyu. 4Ife tiyenera kugwira ntchito za Iye amene anandituma kukanali masana. Usiku ukubwera, pamene wina aliyense sadzagwira ntchito. 5Pamene Ine ndili mʼdziko lapansi, Ine ndine kuwunika kwa dziko lapansi.”

6Atanena izi, Iye anathira malovu pansi ndi kukanda dothi, napaka matopewo mʼmaso a munthuyo. 7Yesu anamuwuza iye kuti, “Pita kasambe mʼdziwe la Siloamu” (mawu awa akutanthauza Wotumidwa). Choncho munthuyo anapita ndi kukasamba ndipo anabwerako akupenya.

8Anzake ndi iwo amene anamuona iye poyamba akupempha anafunsa kuti, “Kodi uyu si munthu amene amapemphapempha uja?” 9Ena ananena kuti anali yemweyo.

Ena anati, “Ayi, sakuoneka ngati yemweyo.”

Koma iye mwini ananenetsa kuti, “Munthuyo ndine.”

10Iwo anafunsitsa kuti, “Kodi nanga maso ako anatsekuka bwanji?”

11Iye anayankha kuti, “Munthu wina wotchedwa Yesu anakanda dothi ndi kupaka mʼmaso anga. Iye anandiwuza kuti ndipite ku Siloamu ndi kukasamba. Choncho ndinapita kukasamba, ndipo ndikuona.”

12Iwo anamufunsa iye kuti, “Ali kuti munthu ameneyu?”

Iye anati, “Ine sindikudziwa.”

Afarisi Afufuza za Kuchiritsidwa Kwake

13Iwo anabwera naye munthu amene poyamba anali wosaona kwa Afarisi. 14Tsono linali la Sabata tsiku limene Yesu anakanda dothi ndi kutsekula maso a munthuyu. 15Choncho Afarisi anamufunsanso iye momwe analandirira kuona kwake. Munthuyo anayankha kuti, “Iye anapaka matope mʼmaso anga, ndipo ine ndinakasamba, ndipo ndikuona.”

16Ena a Afarisi anati, “Munthu uyu siwochokera kwa Mulungu, pakuti sasunga Sabata.”

Koma enanso anafunsa kuti, “Kodi munthu wochimwa angachite bwanji zizindikiro zodabwitsa ngati izi?” Choncho iwo anagawanika.

17Pomaliza iwo anatembenukiranso kwa munthu amene anali wosaona uja nati, “Kodi iwe unena chiyani za Iye poti ndi maso ako amene watsekula?”

Munthuyo anayankha kuti, “Iye ndi mneneri.”

18Ayuda sanakhulupirirebe kuti iye anali wosaona ndi kuti anayamba kuona kufikira atayitana makolo ake. 19Iwo anafunsa kuti, “Kodi uyu ndi mwana wanu? Kodi iyeyu ndi amene mukunena kuti anabadwa wosaona? Nanga zikutheka bwanji kuti akuona?”

20Makolo anayankha kuti, “Ife tikudziwa kuti ndi mwana wathu, ndipo tikudziwa kuti anabadwa wosaona. 21Koma sitidziwa zimene zachitika kuti tsopano azipenya. Amenenso wamupenyetsa sitikumudziwa. Mufunseni ndi wamkulu; iye adziyankhira yekha.” 22Makolo ake ananena izi chifukwa amaopa Ayuda, popeza Ayuda anatsimikiza kale kuti aliyense amene adzamuvomereza Yesu kuti anali Khristu adzatulutsidwa mʼsunagoge. 23Ichi ndi chifukwa chake makolo ake anati, “Mufunseni iye ndi wamkulu.”

24Iwo anamuyitanitsa kachiwiri munthu amene anali wosaonayo. Iwo anati, “Lemekeza Mulungu. Ife tikudziwa kuti munthu uyu ndi wochimwa.”

25Iye anayankha kuti, “Zakuti Iye ndi wochimwa kapena ayi, ine sindikudziwa. Ine ndikudziwa chinthu chimodzi. Ndinali wosaona koma tsopano ndikuona!”

26Kenaka anamufunsa kuti, “Kodi Iye anachita chiyani kwa iwe? Iye anatsekula motani maso ako?”

27Iye anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kale ndipo inu simunamvetsetse. Chifukwa chiyani mukufuna mumvenso? Mukufuna kuti inu mukhale ophunzira akenso?”

28Pamenepo anamunyoza ndipo anati, “Iwe ndiye ophunzira wa munthuyu! Ife ndife ophunzira a Mose! 29Ife tikudziwa kuti Mulungu anayankhula kwa Mose, koma za munthu uyu, ife sitikudziwa ngakhale kumene akuchokera.”

30Munthuyo anayankha kuti, “Tsopano izi ndi zodabwitsa! Inu simukudziwa kumene akuchokera, komabe iye watsekula maso anga. 31Ife tikudziwa kuti Mulungu samvera wochimwa. Iye amamvera munthu woopa Mulungu amene amachita chifuniro chake. 32Palibe amene anamvapo za kutsekula maso a munthu wobadwa wosaona. 33Ngati munthu uyu akanakhala wosachokera kwa Mulungu, palibe chimene Iye akanachita.”

34Pamenepo anayankha kuti, “Iwe unabadwa mu uchimo kotheratu; bwanji ukuyesa kutiphunzitsa ife!” Ndipo anamutulutsa kunja.

Kusaona kwa Uzimu

35Yesu anamva kuti anamutulutsa kunja ndipo pamene anamupeza anati, “Kodi ukukhulupirira Mwana wa Munthu?”

36Munthuyo anafunsa kuti, “Kodi, Ambuye, ameneyo ndi ndani? Ndiwuzeni kuti ndimukhulupirire Iye?”

37Yesu anati, “Iwe wamuona tsopano. Zoonadi ndiye amene akuyankhula nawe.”

38Pamenepo munthuyo anati, “Ambuye, ndikukhulupirira,” ndipo anamulambira Iye.

39Yesu anati, “Ndinabwera pansi pano kudzaweruza kuti osaona aone ndi openya asaone.”

40Afarisi ena amene anali pafupi naye anamva akunena izi ndipo anafunsa kuti, “Chiyani? Kodi ndife osaonanso?”

41Yesu anati, “Mukanakhala osaona, simukanachimwa; koma tsopano popeza mukuti mumaona, ndinu ochimwabe.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約翰福音 9:1-41

醫治盲人

1耶穌在路上看見一個生來失明的人。 2門徒問耶穌:「老師,這個人生下來便雙目失明,是因為他犯了罪呢,還是他父母犯了罪呢?」

3耶穌說:「不是他犯了罪,也不是他父母犯了罪,而是要在他身上彰顯上帝的作為。 4趁著白天,我們必須做差我來者的工作,黑夜一到,就沒有人能工作了。 5我在世上的時候,是世界的光。」

6耶穌講完後,便吐唾沫在地上,用唾沫和泥抹在那盲人的眼睛上, 7對他說:「到西羅亞池去洗洗!」西羅亞是「奉差遣」的意思。那盲人照著去做,回來的時候已經能看見了。

8他的鄰居和從前見他討飯的人說:「他不是那個常在這裡討飯的人嗎?」

9有人說:「是他。」有人說:「不是他,只是長得像他。」

他自己說:「我就是那個人。」

10他們問:「你的眼睛是怎麼好的?」

11他回答說:「有一位叫耶穌的人和泥抹我的眼睛,叫我到西羅亞池子去洗。我照著去做,眼睛就能看見了。」

12他們問:「那個人現在在哪裡?」他說:「我不知道。」

盤問復明的盲人

13他們就把這個從前失明的人帶到法利賽人那裡。 14耶穌和泥開他眼睛的那天是安息日。 15法利賽人也查問他的眼睛是怎麼復明的。盲人便對他們說:「祂把泥抹在我的眼睛上,我去一洗,眼睛就看見了。」

16有些法利賽人說:「那個人不是從上帝那裡來的,因為祂不守安息日。」有些人卻說:「如果祂是個罪人,又怎能行這樣的神蹟呢?」他們就爭論起來。

17於是,他們又問那個盲人:「既然祂開了你的眼睛,你認為祂是什麼人?」

他說:「祂是先知。」

18猶太人不相信他以前是瞎眼的,現在能看見了,便叫來他的父母, 19問他們:「這是你們的兒子嗎?你們不是說他生來就瞎眼嗎?怎麼現在能看見了?」

20他父母回答說:「我們知道他是我們的兒子,生來雙目失明。 21至於他現在怎麼能看見了,我們就不知道了。是誰醫好了他,我們也不知道。他現在已經長大成人,你們可以去問他,他自己可以回答。」

22他父母因為害怕那些猶太人,所以才這樣說,因為那些猶太人早就商量好了,誰承認耶穌是基督,就把他趕出會堂。 23因此他父母才說他已經長大成人,叫他們去問他。

24法利賽人又把那個從前失明的人叫來,對他說:「你應該把榮耀歸給上帝9·24 這是古時叫人在上帝面前起誓說實話的慣用語,參見約書亞記7·19!我們知道那個人是罪人。」

25他說:「祂是不是罪人,我不知道;我只知道從前我是瞎眼的,現在能看見了。」

26他們就問他:「祂向你做了些什麼?祂是怎樣醫好你眼睛的?」

27他回答說:「我已經告訴過你們了,你們不聽,現在又問,難道你們也想作祂的門徒嗎?」

28他們就罵他:「你才是祂的門徒!我們是摩西的門徒。 29我們知道上帝曾對摩西講話,至於這個人,我們不知道祂是從哪裡來的。」

30那人說:「祂開了我的眼睛,你們竟不知道祂從哪裡來,真是奇怪。 31我們知道上帝不聽罪人的禱告,只聽那些敬拜祂、遵行祂旨意者的禱告。 32從創世以來,從未聽過有人能把天生失明的人醫好。 33如果這個人不是從上帝那裡來的,就什麼也不能做。」

34法利賽人斥責他:「你這生來就深陷罪中的傢伙,居然敢教導我們!」於是把他趕了出去。

35耶穌聽說了這事,後來祂找到這個人,對他說:「你信上帝的兒子嗎?」

36他說:「先生,誰是上帝的兒子?我要信祂。」

37耶穌說:「你已經看見祂了,現在跟你說話的就是祂。」

38他說:「主啊!我信!」他就敬拜耶穌。

39耶穌說:「我為了審判來到這世界,使瞎眼的可以看見,使看得見的反成了瞎眼的。」

40有些跟祂在一起的法利賽人聽了這句話,就問:「難道我們也瞎了眼嗎?」

41耶穌說:「如果你們是瞎眼的,就沒有罪了。但現在你們自稱看得見,所以你們的罪還在。」