Yohane 7 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 7:1-53

Yesu Apita Kuphwando Lamisasa

1Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe. 2Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira, 3abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita. 4Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.” 5Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.

6Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera. 7Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa. 8Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.” 9Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.

10Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri. 11Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”

12Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.”

Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.” 13Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.

Yesu Aphunzitsa pa Phwando

14Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa. 15Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”

16Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma. 17Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha. 18Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse. 19Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”

20Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”

21Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa. 22Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata. 23Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata? 24Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”

Kodi Yesu ndi Khristu?

25Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu? 26Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu? 27Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”

28Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa, 29koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”

30Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike. 31Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”

32Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.

33Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine. 34Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”

35Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki? 36Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’ ”

Mitsinje ya Madzi Opatsa Moyo

37Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe. 38Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’ ” 39Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.

40Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”

41Ena anati, “Iye ndiye Khristu.”

Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya? 42Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?” 43Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu. 44Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.

Kusakhulupirira kwa Atsogoleri a Ayuda

45Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”

46Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”

47Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?” 48“Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye? 49Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”

50Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti, 51“Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”

52Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”

[Mipukutu yoyambirira ndi maumboni akale mulibe 7:53 mpaka 8:11]

Za Mkazi Wachigololo

53Kenaka onse anachoka, napita kwawo.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

הבשורה על-פי יוחנן 7:1-53

1לאחר מכן חזר ישוע לגליל ועבר מכפר לכפר. הוא לא רצה לשוב ליהודה, כי מנהיגי היהודים שם רצו להרגו. 2בהתקרב חג הסוכות 3האיצו בו אחיו לעלות לירושלים לרגל החג. ”לך ליהודה, כדי שגם תלמידיך יראו את הנסים שאתה מחולל“, לעגו לו.

4”איך אתה רוצה להתפרסם בעודך מסתתר כאן? אם אתה מחולל ניסים ונפלאות, גלה את עצמך לעולם.“ 5גם אחיו לא האמינו בו. 6”עדיין לא הגיע הזמן שאלך, אולם אתם יכולים ללכת בכל זמן שתרצו“, השיב ישוע. 7”כי העולם אינו יכול לשנוא אתכם, אבל הוא שונא אותי, משום שאני מוכיח אותו במעשיו המושחתים. 8לכו אתם לחוג את החג בירושלים. איני הולך עתה, כי טרם הגיע זמני.“ 9וישוע נשאר בגליל.

10אולם לאחר שהלכו אחיו הלך גם ישוע לירושלים, אם כי בסתר, כדי שלא יכירו אותו. 11בינתיים חיפשוהו המנהיגים בין החוגגים וחקרו: ”היכן הוא?“ 12דעת הקהל הייתה חלוקה עליו; אחדים אמרו: ”הוא אדם נפלא!“ ואילו אחרים טענו: ”הוא רמאי!“ 13אך איש לא העז להשמיע את דעתו עליו ברבים, מפחד מנהיגי היהודים.

14בעיצומו של החג הלך ישוע לבית־המקדש ולימד את העם. 15”כיצד הוא יודע כל־כך הרבה?“ תמהו היהודים. ”הרי הוא לא למד אף פעם בבית מדרש!“

16”איני מלמד אתכם את תורתי, כי אם את תורת האלוהים אשר שלחני“, השיב ישוע. 17”מי שרוצה לעשות את רצון האלוהים יודע אם אני מדבר בשם אלוהים או בשם עצמי. 18מי שמשמיע את דעתו האישית מצפה לשבחים ותהילה, אולם מי שרוצה בכבוד שולחו הוא אדם ישר ונאמן. 19משה נתן לכם את התורה אבל איש מביניכם אינו מקיים את התורה. מדוע אתם רוצים להרוג אותי על הפרת התורה?“ 20”היצאת מדעתך“, קרא הקהל. ”מי רוצה להרוג אותך?“

21”אני עשיתי נס אחד בשבת וכולכם התפלאתם והשתוממתם על כך“, אמר ישוע. 22”אבל גם אתם עובדים בשבת! הרי אתם עושים ברית־מילה לפי מצוות משה, מצוה שניתנה לנו למעשה מהאבות וקדמה לתורת משה, גם בשבת. 23אם אתם מתירים קיום ברית־מילה בשבת, כדי לא להפר את התורה, מדוע אתם מתרגזים על שריפאתי מישהו בשבת? 24אל תשפטו רק לפי מה שאתם רואים בעיניכם, אלא בחנו ושפטו בצדק!“

25אחדים מתושבי ירושלים שאלו: ”האם אין זה האיש שהם רוצים להרוג? 26הנה הוא מדבר בציבור ואיש אינו פוגע בו. אולי מנהיגינו הגיעו למסקנה שהוא באמת המשיח! 27אולם כיצד ייתכן הדבר? הרי אנחנו יודעים מאין בא, ואילו המשיח אמור לבוא מאי־שם, ממקום בלתי ידוע.“

28”ודאי שיודעים אתם מי אני ומאין באתי,“ קרא ישוע בקול בבית־המקדש, ”אבל דעו לכם שלא באתי אליכם על דעת עצמי, אלא נשלחתי על־ידי האלוהים שאותו אינכם מכירים. 29אולם אני מכיר אותו, כי אני בא ממנו והוא שלח אותי.“

30ההמון רצה לתפוס אותו, אך איש לא הרים עליו אצבע, כי טרם הגיע זמנו. 31אנשים רבים מן העם האמינו בישוע, ואמרו: ”לאילו ניסים מצפים אתם מהמשיח שאדם זה לא חולל?“

32כאשר נוכחו הפרושים כי העם נוטה להאמין בישוע, הם שלחו יחד עם ראשי הכוהנים סוכנים לתפוס אותו. 33אולם ישוע אמר להם: ”אני אהיה אתכם עוד זמן־מה, ואחר כך אחזור לשולחי. 34תחפשו אותי ולא תמצאוני, כי לא תוכלו לבוא אל המקום שאהיה בו.“

35היהודים נבוכו מדבריו. ”לאן הוא עומד ללכת?“ תמהו. ”אולי בכוונתו לעזוב את הארץ וללכת ללמד את היהודים בתפוצות או אף את הגויים! 36למה התכוון כשאמר כי נחפש אותו ולא נוכל למצוא אותו, ואף לא נוכל לבוא למקום הימצאו?“

37ביום האחרון והגדול של החג עמד ישוע וקרא בקול: ”כל הצמא שיבוא אלי וישתה! 38כי כמו שכתוב, המאמין בי, יזרמו מקרבו נהרות מים חיים.“ 39ישוע התכוון לרוח הקודש שהמאמינים בשמו היו עתידים לקבל. עד לאותו זמן לא ניתן רוח הקודש, כי ישוע עדיין לא נתפאר ולא חזר לשמים. 40אנשים רבים בהמון קראו לאחר ששמעו את דבריו: ”הוא באמת הנביא!“ 41אחרים קראו: ”זהו המשיח!“ היו שלגלגו: ”האם המשיח יבוא מהגליל? 42הלא כתוב כי המשיח יהיה מזרע דוד וכי יבוא מבית לחם, עיר דוד.“ 43דעת הקהל עליו הייתה חלוקה. 44אחדים מהם רצו לתפסו, אך איש לא שלח בו יד.

45אנשי החוק שנשלחו לאסרו חזרו אל שולחיהם בידיים ריקות. ”היכן הוא? מדוע לא הבאתם אותו?“ שאלו הפרושים וראשי הכוהנים.

46”הוא דיבר דברים נפלאים כל־כך; מעולם לא שמענו דברים כאלה!“ השיבו. 47”גם אתם הלכתם שולל?“ כעסו הפרושים. 48”האם ראיתם מישהו בינינו, המנהיגים או הפרושים, אשר מאמין כי הוא המשיח? 49רק ההמון מקרב העם הזה מאמין בו, כי הם אינם יודעים את התורה. ארורים הם!“

50נקדימון היה ביניהם; הוא זה שבא אל ישוע בלילה, וכששמע את דברי הפרושים אמר: 51”האם תורתנו מתירה לנו לשפוט אדם לפני ששמענו מה בפיו וידענו מה שהוא עושה?“

52”גם אתה מהגליל?“ שאלו בלעג. ”דרוש בכתובים וראה שאף נביא אינו בא מהגליל!“ 53בזאת הם נפרדו והלכו איש לביתו.