Yohane 4 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 4:1-54

Yesu Acheza ndi Mayi wa ku Samariya

1Yesu atazindikira kuti Afarisi amva zoti Iye ankapeza ndi kubatiza ophunzira ambiri kupambana Yohane, 2(ngakhale kuti Yesuyo sankabatiza, koma ophunzira ake). 3Iye anachoka ku Yudeya ndi kubwereranso ku Galileya.

4Ndipo Iye anayenera kudutsa mu Samariya. 5Iye anafika mʼmudzi wa Asamariya wotchedwa Sukari, pafupi ndi malo amene Yakobo anapatsa mwana wake Yosefe. 6Chitsime cha Yakobo chinali pamenepo ndipo Yesu atatopa ndi ulendo anakhala pansi pambali pa chitsimecho. Nthawi inali pafupifupi ora lachisanu ndi chimodzi masana.

7Mayi wa Chisamariya atabwera kudzatunga madzi, Yesu anati kwa iye, “Kodi ungandipatse madzi akumwa.” 8(Ophunzira ake nʼkuti atapita mʼmudzi kukagula chakudya).

9Mayiyo anati kwa Iye, “Inu ndinu Myuda ndipo ine ndine Msamariya. Bwanji mukundipempha madzi akumwa?” (Popeza Ayuda ndi Asamariya sankayanjana).

10Yesu anamuyankha kuti, “Koma iwe ukanadziwa mphatso ya Mulungu ndi Iye amene akukupempha madzi akumwa, ukanamupempha ndipo akanakupatsa madzi amoyo.”

11Mayiyo anati, “Ambuye, Inu mulibe kanthu kotungira madzi ndipo chitsime ndi chakuya. Kodi madzi amoyowo mungawatenge kuti? 12Kodi Inu ndinu wamkulu kuposa kholo lathu Yakobo, amene anatipatsa chitsimechi ndipo iye ankamwanso monga anachita ana ake ndi ziweto zake?”

13Yesu anayankha kuti, “Aliyense amene amamwa madzi awa amamvanso ludzu, 14koma aliyense amene adzamwa madzi amene Ine ndidzamupatsa sadzamvanso ludzu. Ndithudi, madzi amene ndidzamupatsa adzakhala kasupe wamadzi wotumphukira ku moyo wosatha.”

15Mayiyo anati kwa Iye, “Ambuye, patseni madzi amenewo kuti ndisadzamvenso ludzu ndi kumabwerabe kuno kudzatunga madzi.”

16Iye anamuwuza kuti, “Pita kayitane mwamuna wako ndipo ubwere naye.”

17Iye anayankha kuti, “Ine ndilibe mwamuna.”

Yesu anati kwa iye, “Wakhoza ponena kuti ulibe mwamuna. 18Zoona nʼzakuti iwe wakhala pa banja ndi amuna asanu, ndipo mwamuna amene uli naye tsopano si wako. Zimene wanenazi ndi zoona.”

19Mayiyo anati, “Ambuye, ine ndazindikira kuti Inu ndinu mneneri. 20Makolo athu ankapembedza mʼphiri ili koma inu Ayuda mumati malo amene tiyenera kupembedzera ali ku Yerusalemu.”

21Yesu anati, “Mayi inu khulupirira Ine. Nthawi ikubwera pamene inu simudzapembedza Atate mʼphiri ili kapena mu Yerusalemu. 22Inu Asamariya mumapembedza chimene simukuchidziwa. Ife timapembedza chimene tikuchidziwa, pakuti chipulumutso nʼchochokera kwa Ayuda. 23Koma nthawi ikubwera ndipo yafika kale tsopano pamene opembedza woona adzapembedza Atate mu mzimu ndi mʼchoonadi, pakuti opembedza otere ndiwo amene Atate akuwafuna. 24Mulungu ndi Mzimu, ndipo omupembedza Iye ayenera kumupembedza mu mzimu ndi mʼchoonadi.”

25Mayiyo anati, “Ine ndikudziwa kuti Mesiya (wotchedwa Khristu) akubwera. Akabwera, Iye adzafotokoza zonse kwa ife.”

26Ndipo Yesu anamuwuza kuti, “Amene ndikukuyankhulane, ndine amene.”

Ophunzira Abweranso kwa Yesu

27Pa nthawi yomweyo ophunzira ake anabwerera ndipo anadabwa kupeza Iye akuyankhula ndi mayi. Koma palibe amene anamufunsa kuti, “Kodi mukufuna chiyani?” kapena, “Nʼchifukwa chiyani mukuyankhula naye?”

28Kenaka mayiyo anasiya mtsuko wamadzi, nabwerera ku mzinda ndipo anati kwa anthu, 29“Tiyeni mukaone munthu amene wandiwuza ine zilizonse zimene ndinazichita. Kodi ameneyu sangakhale Khristu?” 30Iwo anatuluka mʼmudziwo ndi kupita kumene kunali Iye.

31Pa nthawi imeneyi ndi kuti ophunzira ake akumukakamiza kuti, “Rabi idyani.”

32Koma Iye anawawuza kuti, “Ine ndili ndi chakudya choti ndidye chimene inu simukuchidziwa.”

33Ndipo ophunzira ake anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi alipo wina amene anamubweretsera Iye chakudya?”

34Yesu anati, “Chakudya changa ndikuchita chifuniro cha Iye amene anandituma Ine ndi kumaliza ntchito yake. 35Kodi inu simunena kuti, ‘Kwatsala miyezi inayi ndipo kenaka kukolola?’ Ine ndikukuwuzani kuti, tsekulani maso anu ndipo muyangʼane mʼminda! Mbewu zacha kale kuti zikololedwe. 36Ngakhale tsopano amene akukolola akulandira malipiro ake, ndipo akututa mbewu ku moyo wosatha kuti wofesa ndi wokolola asangalale pamodzi. 37Nʼchifukwa chake mawu akuti, ‘Wina amafesa ndipo wina amakolola’ ndi woona. 38Ine ndinakutumani kukakolola zimene simunagwirire ntchito. Ena anagwira ntchito yolemetsa ndipo inu mwatuta phindu la ntchito yawo.”

Asamariya Ambiri Akhulupirira

39Asamariya ambiri ochokera mʼmudziwo anakhulupirira Iye chifukwa cha umboni wa mayiyo wakuti, “Iye anandiwuza ine zonse ndinazichita.” 40Choncho Asamariya atabwera kwa Iye, anamuwumiriza Iye kuti akhale nawo, ndipo Iye anakhala nawo masiku awiri. 41Ndipo chifukwa cha mawu ake, ena ambiri anakhulupirira.

42Iwo anati kwa mayiyo, “Ife sitikukhulupirira chifukwa cha mawu ako okha, koma tsopano ife tadzimvera tokha, ndipo tikudziwa kuti munthu uyu ndithu ndi Mpulumutsi wa dziko lapansi.”

Yesu Achiritsa Mwana wa Nduna ya Mfumu

43Patatha masiku awiri Iye anachoka napita ku Galileya. 44(Tsopano Yesu mwini ananena kale kuti mneneri salandira ulemu mʼdziko lake). 45Iye atafika ku Galileya, Agalileya anamulandira. Iwo anali ataona zonse zimene anazichita mu Yerusalemu pa phwando la Paska, pakuti iwonso anali komweko.

46Iye anakafikanso ku Kana wa ku Galileya, kumene anasanduliza madzi kukhala vinyo. Ndipo kumeneko kunali nduna ina ya mfumu imene mwana wake wamwamuna anali chigonere akudwala ku Kaperenawo. 47Munthu uyu atamva kuti Yesu wafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya, anapita kwa Iye, namupempha kuti apite akachiritse mwana wakeyo, amene anali pafupi kufa.

48Yesu anawawuza iwo kuti, “Anthu inu pokhapokha mutaona zizindikiro zodabwitsa, simudzakhulupirira.”

49Nduna ya mfumuyo inati, “Ambuye tiyeni mwana wanga asanafe.”

50Yesu anayankha kuti, “Pita. Mwana wako adzakhala ndi moyo.”

Munthuyo anakhulupirira mawu a Yesu ndipo ananyamuka. 51Iye ali pa njira, antchito ake anakumana naye, namuwuza kuti mwana wanu uja wachira. 52Iye atafunsa kuti ndi nthawi yanji imene mwana wake anapeza bwino, iwo anati kwa iye, “Malungo anamusiya iye dzulo pa ora lachisanu ndi chiwiri.”

53Ndipo bamboyo anazindikira kuti iyi inali nthawi yomweyo imene Yesu anati kwa iye, “Mwana wako adzakhala ndi moyo.” Choncho iye ndi onse a pa banja lake anakhulupirira.

54Ichi ndiye chinali chizindikiro chodabwitsa chachiwiri chimene Yesu anachita atafika ku Galileya kuchokera ku Yudeya.

Священное Писание

Иохан 4:1-54

Самарянка у колодца

1Блюстители Закона услышали о том, что Иса приобретал и погружал в воду4:1 Или: «омывал». больше учеников, чем Яхия, 2хотя на самом деле обряд совершал не Иса, а Его ученики. 3Когда Иса узнал, что о Нём говорят, Он покинул Иудею и направился обратно в Галилею. 4Путь Его лежал через Самарию, 5и Он пришёл в самарийский город Сихарь, расположенный недалеко от участка земли, который Якуб некогда дал своему сыну Юсуфу4:5 См. Нач. 33:18-19; 48:21-22.. 6Там был колодец Якуба, и Иса, уставший после дороги, сел у колодца отдохнуть. Это было около полудня.

7К колодцу пришла за водой одна самарийская4:7 Самаряне – этот народ имеет смешанное происхождение. Потомки десяти северных родов Исраила и переселенцев из других частей Ассирийской империи, они признают только Таурат, но не другие книги Писания. женщина.

– Дай Мне, пожалуйста, напиться воды, – попросил её Иса.

8Ученики Его в это время пошли в город купить еды.

9Самарянка удивилась:

– Ты иудей, а я самарянка, как это Ты можешь просить у меня напиться? (Дело в том, что иудеи не общаются с самарянами4:9 Или: «иудеи не пользуются общей посудой с самарянами». Для иудея самаряне были ритуально нечистым народом, и поэтому пользование их посудой влекло за собой церемониальное осквернение..)

10Иса ответил ей:

– Если бы ты знала о даре Всевышнего и о том, Кто просит у тебя напиться, ты бы сама попросила Его, и Он дал бы тебе живой воды4:10 На языке оригинала выражение «живая вода» означает как «воду, дающую жизнь», так и простую проточную воду..

11Женщина сказала:

– Господин, Тебе и зачерпнуть-то нечем, а колодец глубок. Откуда же у Тебя живая вода? 12Неужели Ты больше нашего предка Якуба, который оставил нам этот колодец и сам пил из него, и его сыновья пили, и стада его пили?

13Иса ответил:

– Кто пьёт эту воду, тот опять захочет пить. 14Тот же, кто пьёт воду, которую Я дам ему, никогда больше не будет мучим жаждой. Вода, которую Я ему дам, станет в нём источником, текущим в вечную жизнь.

15Женщина сказала Ему:

– Господин, так дай же мне такой воды, чтобы я больше не хотела пить и мне не нужно было приходить сюда за водой.

16Он сказал ей:

– Пойди, позови своего мужа и возвращайся сюда.

17– У меня нет мужа, – ответила женщина.

Иса сказал ей:

– Ты права, когда говоришь, что у тебя нет мужа. 18Ведь у тебя было пять мужей, и тот, с кем ты сейчас живёшь, не муж тебе; это ты правду сказала.

19– Господин, – сказала женщина, – я вижу, что Ты пророк. 20Так объясни же мне, почему наши отцы поклонялись на этой горе4:20 Самаряне поклонялись Всевышнему на горе Геризим, которая находится на расстоянии более 40 км севернее от Иерусалима., а вы, иудеи, говорите, что Всевышнему следует поклоняться в Иерусалиме?

21Иса ответил:

– Поверь Мне, женщина, настанет время, когда вы будете поклоняться Отцу не на этой горе и не в Иерусалиме. 22Вы, самаряне, и сами толком не знаете, чему вы поклоняетесь, мы же знаем, чему поклоняемся, ведь спасение – от иудеев. 23Но наступит время, и уже наступило, когда истинные поклонники будут поклоняться Небесному Отцу в духе и истине, потому что именно таких поклонников ищет Себе Отец. 24Всевышний есть Дух, и поклоняющиеся Ему должны поклоняться в духе и истине.

25Женщина сказала:

– Я знаю, что должен прийти Масих4:25 Масих – самаряне, так же как и иудеи, ожидали Масиха. Но, признавая только Таурат, они не могли считать Его Царём из потомков Давуда. По их понятиям Масих, Которого они называли Тахеб, должен был быть пророком, учителем и законодателем, подобным Мусе, Который разрешит все их проблемы (см. Втор. 18:15-18). (то есть «Помазанник»); вот когда Он придёт, Он нам всё и объяснит.

26Иса сказал ей:

– Это Я, Тот, Кто говорит с тобой.

О духовной жатве

27В это время возвратились Его ученики и удивились, что Иса разговаривает с женщиной. Но никто, однако, не спросил, что Он хотел и почему Он с ней говорил. 28Женщина оставила свой кувшин для воды, вернулась в город и сказала людям:

29– Идите и посмотрите на Человека, Который рассказал мне всё, что я сделала. Не Масих ли Он?

30Народ из города пошёл к Исе. 31В это время Его ученики настаивали:

– Учитель, поешь что-нибудь.

32Но Он сказал им:

– У Меня есть пища, о которой вы не знаете.

33Тогда ученики стали переговариваться:

– Может, кто-то принёс Ему поесть?

34– Пища Моя состоит в том, – сказал Иса, – чтобы исполнить волю Пославшего Меня и совершить Его дело.

35– Разве вы не говорите: «Ещё четыре месяца, и будет жатва»? А Я говорю вам: поднимите глаза и посмотрите на поля, как они уже созрели для жатвы! 36Жнец получает свою награду! Он собирает урожай для жизни вечной, чтобы радовались вместе и сеятель, и жнец. 37В этом случае верно изречение: один сеет, а другой жнёт. 38Я послал вас жать то, над чем вы не трудились. Другие много поработали, вы же пожинаете плоды их трудов.

Уверование самарян

39Многие самаряне, жители этого города, уверовали в Ису, потому что женщина сказала:

– Он рассказал мне всё, что я сделала.

40Самаряне пришли к Нему и стали упрашивать Его остаться с ними, и Иса провёл там два дня. 41И ещё больше людей уверовали в Него из-за Его слов. 42Они говорили женщине:

– Мы уже не с твоих слов верим, а потому, что сами слышали и знаем, что Этот Человек действительно Спаситель мира.

Исцеление сына придворного

43Через два дня Иса отправился оттуда в Галилею. 44Он и Сам говорил, что пророк не имеет чести у себя на родине. 45Однако когда Он пришёл в Галилею, галилеяне Его радушно приняли, но только потому, что были в Иерусалиме на празднике Освобождения и видели все чудеса, которые Иса там совершил.

46Иса ещё раз посетил Кану Галилейскую, где Он превратил воду в вино. В Капернауме был один придворный, у которого болел сын. 47Когда этот человек услышал о том, что Иса пришёл из Иудеи в Галилею, он пришёл к Нему и умолял Его исцелить сына, который был при смерти.

48Иса сказал ему:

– Люди, почему вы не можете поверить, пока не увидите чудес и знамений?

49Но придворный лишь умолял:

– Господин, пойдём, пока сын мой ещё не умер.

50Иса ответил:

– Иди, твой сын будет жить.

Человек поверил слову Исы и пошёл. 51Он был ещё в пути, когда рабы встретили его и сообщили, что мальчику полегчало. 52Он спросил, в котором часу ему стало легче, и они сказали:

– Вчера в час дня жар у него прошёл.

53Отец понял, что это произошло именно тогда, когда Иса сказал ему: «Твой сын будет жить».

Придворный и все его домашние уверовали. 54Это было второе знамение, сотворённое Исой в Галилее по приходе Его из Иудеи.