Yohane 21 – CCL & HHH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 21:1-25

Yesu Aonekera kwa Ophunzira ku Nyanja ya Tiberiya

1Zitatha izi Yesu anaonekeranso kwa ophunzira ake, mʼmbali mwa nyanja ya Tiberiya. Anadzionetsera motere: 2Simoni Petro, Tomasi (otchedwa Didimo), Natanieli wochokera ku Kana wa ku Galileya, ana a Zebedayo, ndi ophunzira ena awiri anali limodzi. 3Simoni Petro anawawuza iwo kuti, “Ine ndikupita kukasodza,” ndipo iwo anati, “ife tipita nawe.” Choncho anapita ndi kulowa mʼbwato, koma usiku umenewo sanagwire kanthu.

4Mmamawa, Yesu anayimirira mʼmbali mwa nyanja, koma ophunzira ake sanazindikire kuti anali Yesu.

5Yesu anawafunsa iwo kuti, “Anzanga, kodi muli nsomba?”

Iwo anayankha kuti, “Ayi.”

6Iye anati, “Ponyani khoka lanu kudzanja lamanja la bwato lanu ndipo mupha kanthu.” Atatero, iwo analephera kukoka ukonde chifukwa chakuchuluka kwa nsomba.

7Kenaka ophunzira amene Yesu amamukonda anati kwa Petro, “Ndi Ambuye!” Petro atangomva iye akunena kuti ndi Ambuye, iye anavala chovala chake (pakuti anali atavula) ndipo analumphira mʼnyanja. 8Ophunzira enawo analowa mʼbwato akukoka ukonde odzaza ndi nsomba, popeza iwo sanali kutali kuchokera ku mtunda, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi. 9Atafika pa mtunda, iwo anaona moto wamakala pamenepo ndi nsomba, ndi buledi.

10Yesu anawawuza kuti, “Tabweretsa nsomba zina mwagwirazo.”

11Simoni Petro anakwera mʼbwato ndi kukokera khoka ku gombe, lodzaza ndi nsomba zikuluzikulu 153, komabe ndi nsomba zochuluka chotero khoka silinangʼambike. 12Yesu anawawuza kuti, “Bwerani mudzalandire chakudya chammawa.” Palibe mmodzi wa ophunzira anayesa kumufunsa Iye, “Kodi ndinu ndani?” Iwo anadziwa kuti anali Ambuye. 13Yesu anabwera, natenga buledi ndikuwapatsa iwo, ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsomba. 14Aka kanali tsopano kachitatu Yesu akuonekera kwa ophunzira ake Iye ataukitsidwa kwa akufa.

Yesu Abwezeretsa Petro

15Iwo atamaliza kudya chakudya chammawa, Yesu anati kwa Simoni Petro, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikonda Ine kuposa mmene amandikondera awa?”

Iye anati, “Inde Ambuye, Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.”

Yesu anati, “Samala ana ankhosa anga.”

16Yesu anatinso, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?”

Iye anayankha kuti, “Inde, Ambuye, Inu mukudziwa kuti ine ndimakukondani.”

Yesu anati, “Weta nkhosa zanga.”

17Yesu anati kwa iye kachitatu, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?”

Petro anadzimvera chisoni chifukwa Yesu anamufunsa kachitatu kuti, “Kodi umandikonda Ine?” Iye anati, “Ambuye, Inu mudziwa zinthu zonse. Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.”

Yesu anati, “Dyetsa nkhosa zanga. 18Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti uli wamngʼono unkadziveka wekha lamba ndi kupita kumene unkafuna; koma ukadzakalamba udzatambasula manja ako ndipo wina wake adzakuveka ndikukutsogolera kupita kumene sukufuna kupita.” 19Yesu ananena izi kumuzindikiritsa mtundu wa imfa imene Petro adzalemekezera nayo Mulungu. Kenaka Iye anati kwa Petro, “Nditsate Ine!”

20Petro anatembenuka ndi kuona kuti ophunzira amene Yesu amamukonda amawatsatira iwo. (Uyu ndi amene anatsamira pachifuwa cha Yesu pa chakudya chamadzulo ndipo iye anati, “Ambuye, kodi ndi ndani amene adzakuperekani Inu?” 21Petro atamuona iye, anafunsa kuti, “Ambuye, nanga uyu?”

22Yesu anayankha kuti, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo? Iwe uyenera kunditsata Ine.” 23Chifukwa cha ichi mbiri inafala pakati pa abale kuti wophunzira uyu sadzafa. Koma Yesu sananene kuti iye sadzafa. Iye anati, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo?”

24Uyu ndi wophunzira amene akuchitira umboni ndipo ndi amene analemba. Ife tidziwa kuti umboni wake ndi woona.

25Koma palinso zina zambiri zimene Yesu anachita. Zikanalembedwa zonsezi, ndikhulupirira dziko lonse lapansi likanasowa malo osungirako mabuku onse amene akanalembedwa.

Habrit Hakhadasha/Haderekh

הבשורה על-פי יוחנן 21:1-25

1כעבור זמן מה שוב נראה ישוע אל תלמידיו, הפעם ליד הכינרת, וכך התרחש הדבר:

2שמעון פטרוס, תומא התאום, נתנאל מכפר קנה שבגליל, בני זבדי, ועוד שניים אחרים היו ביחד.

3”אני הולך לדוג“, אמר שמעון פטרוס.

”גם אנחנו באים“, אמרו האחרים. הם עלו לסירה, אולם לא לכדו דבר במשך כל הלילה.

4עם זריחת החמה ראו מישהו על החוף, אך לא ידעו שישוע היה האיש.

5”בני, האם לכדתם משהו?“ שאל.

”לא!“ השיבו פה אחד.

6”אם תשליכו את הרשת לימין הסירה תלכדו דגים רבים“, אמר ישוע. הם עשו כדבריו, ודגים רבים כל־כך נלכדו ברשת, עד שלא היה להם כוח להעלות את הרשת חזרה לסירה.

7התלמיד שהיה אהוב על ישוע אמר לפטרוס: ”זהו האדון!“ כאשר שמע פטרוס את דבריו, לבש את חולצתו שהסיר קודם לכן, וקפץ למים. 8ואילו יתר התלמידים הפליגו לחוף שהיה במרחק מאה מטר בערך, ואיתם הרשת המלאה בדגים. 9כשעלו לחוף ראו מדורה שעליה נצלים דגים, ובצד היה לחם.

10”הביאו כמה מהדגים שלכדתם“, ביקש ישוע. 11שמעון פטרוס משך את הרשת ליבשה, וכאשר ספר את השלל הוא מנה 153 דגים גדולים. למרות מספרם ומשקלם לא נקרעה הרשת!

12”בואו, איכלו ארוחת בוקר“, הזמינם ישוע. איש מהם לא העז לשאול אותו אם הוא באמת האדון, כי כולם היו בטוחים בכך. 13ישוע הגיש להם את הלחם והדגים.

14זאת הייתה הפעם השלישית שבה נגלה אליהם ישוע לאחר שקם מהמתים.

15לאחר ארוחת הבוקר שאל ישוע את שמעון פטרוס: ”שמעון בן־יונה, האם אתה אוהב אותי יותר מכל אלה?“

”כן,“ השיב פטרוס, ”אתה יודע שאני אוהב אותך.“

”אם כן, רעה את טלאי“, אמר ישוע.

16ישוע שאל אותו שנית: ”שמעון בן־יונה, האם אתה באמת אוהב אותי?“

”כן, אדוני, אתה יודע שאני אוהב אותך“, השיב פטרוס שנית.

”אם כן, נהג את צאני“, אמר ישוע.

17ישוע שאל פעם שלישית: ”שמעון בן־יונה, האם אתה באמת אוהב אותי?“ פטרוס נעצב משאלתו החוזרת של ישוע ואמר: ”אדוני, הכול אתה יודע. אתה יודע שאני אוהב אותך.“

”אם כן, רעה את צאני“, חזר ישוע על בקשתו. 18”כשהיית צעיר יכולת לעשות כרצונך וללכת לאן שרצית. אולם כאשר תזדקן תושיט את ידיך – אנשים אחרים ילבישוך ויובילוך לאן שהם ירצו, ולא לאן שאתה תרצה.“ 19ישוע אמר לו דברים אלה כדי להכינו לקראת צורת מותו בעתיד, שבו יכבד את האלוהים. כאשר סיים ישוע לדבר, אמר לפטרוס: ”בוא אחרי.“

20פטרוס הביט לאחור וראה שגם התלמיד האהוב על ישוע הולך אחריהם – אותו תלמיד שישב ליד ישוע בסעודה האחרונה ושאל מי מהם עמד להסגירו.

21”מה בקשר אליו, אדוני?“ שאל פטרוס.

22ישוע השיב: ”אם אני רוצה שהוא יישאר בחיים עד בואי, מה זה לך? בוא אתה אחרי.“

23משום כך התפשטה השמועה בין האחים שהתלמיד הזה לא ימות. אבל למעשה ישוע כלל לא אמר זאת; הוא אמר: ”אם אני רוצה שהוא יישאר בחיים עד בואי, מה זה לך?“

24זהו התלמיד שראה את כל ההתרחשויות האלה, העיד עליהן, וכתב אותן. כולנו יודעים שעדותו אמת. 25ישוע חולל עוד מעשים נפלאים רבים, אך העולם כולו צר מלהכיל את כל הספרים שהיה אפשר לכתוב עליהם.