Yohane 21 – CCL & CARSA

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 21:1-25

Yesu Aonekera kwa Ophunzira ku Nyanja ya Tiberiya

1Zitatha izi Yesu anaonekeranso kwa ophunzira ake, mʼmbali mwa nyanja ya Tiberiya. Anadzionetsera motere: 2Simoni Petro, Tomasi (otchedwa Didimo), Natanieli wochokera ku Kana wa ku Galileya, ana a Zebedayo, ndi ophunzira ena awiri anali limodzi. 3Simoni Petro anawawuza iwo kuti, “Ine ndikupita kukasodza,” ndipo iwo anati, “ife tipita nawe.” Choncho anapita ndi kulowa mʼbwato, koma usiku umenewo sanagwire kanthu.

4Mmamawa, Yesu anayimirira mʼmbali mwa nyanja, koma ophunzira ake sanazindikire kuti anali Yesu.

5Yesu anawafunsa iwo kuti, “Anzanga, kodi muli nsomba?”

Iwo anayankha kuti, “Ayi.”

6Iye anati, “Ponyani khoka lanu kudzanja lamanja la bwato lanu ndipo mupha kanthu.” Atatero, iwo analephera kukoka ukonde chifukwa chakuchuluka kwa nsomba.

7Kenaka ophunzira amene Yesu amamukonda anati kwa Petro, “Ndi Ambuye!” Petro atangomva iye akunena kuti ndi Ambuye, iye anavala chovala chake (pakuti anali atavula) ndipo analumphira mʼnyanja. 8Ophunzira enawo analowa mʼbwato akukoka ukonde odzaza ndi nsomba, popeza iwo sanali kutali kuchokera ku mtunda, pafupifupi mamita makumi asanu ndi anayi. 9Atafika pa mtunda, iwo anaona moto wamakala pamenepo ndi nsomba, ndi buledi.

10Yesu anawawuza kuti, “Tabweretsa nsomba zina mwagwirazo.”

11Simoni Petro anakwera mʼbwato ndi kukokera khoka ku gombe, lodzaza ndi nsomba zikuluzikulu 153, komabe ndi nsomba zochuluka chotero khoka silinangʼambike. 12Yesu anawawuza kuti, “Bwerani mudzalandire chakudya chammawa.” Palibe mmodzi wa ophunzira anayesa kumufunsa Iye, “Kodi ndinu ndani?” Iwo anadziwa kuti anali Ambuye. 13Yesu anabwera, natenga buledi ndikuwapatsa iwo, ndipo anachita chimodzimodzi ndi nsomba. 14Aka kanali tsopano kachitatu Yesu akuonekera kwa ophunzira ake Iye ataukitsidwa kwa akufa.

Yesu Abwezeretsa Petro

15Iwo atamaliza kudya chakudya chammawa, Yesu anati kwa Simoni Petro, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikonda Ine kuposa mmene amandikondera awa?”

Iye anati, “Inde Ambuye, Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.”

Yesu anati, “Samala ana ankhosa anga.”

16Yesu anatinso, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?”

Iye anayankha kuti, “Inde, Ambuye, Inu mukudziwa kuti ine ndimakukondani.”

Yesu anati, “Weta nkhosa zanga.”

17Yesu anati kwa iye kachitatu, “Simoni, mwana wa Yohane, kodi umandikondadi Ine?”

Petro anadzimvera chisoni chifukwa Yesu anamufunsa kachitatu kuti, “Kodi umandikonda Ine?” Iye anati, “Ambuye, Inu mudziwa zinthu zonse. Inu mukudziwa kuti Ine ndimakukondani.”

Yesu anati, “Dyetsa nkhosa zanga. 18Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti uli wamngʼono unkadziveka wekha lamba ndi kupita kumene unkafuna; koma ukadzakalamba udzatambasula manja ako ndipo wina wake adzakuveka ndikukutsogolera kupita kumene sukufuna kupita.” 19Yesu ananena izi kumuzindikiritsa mtundu wa imfa imene Petro adzalemekezera nayo Mulungu. Kenaka Iye anati kwa Petro, “Nditsate Ine!”

20Petro anatembenuka ndi kuona kuti ophunzira amene Yesu amamukonda amawatsatira iwo. (Uyu ndi amene anatsamira pachifuwa cha Yesu pa chakudya chamadzulo ndipo iye anati, “Ambuye, kodi ndi ndani amene adzakuperekani Inu?” 21Petro atamuona iye, anafunsa kuti, “Ambuye, nanga uyu?”

22Yesu anayankha kuti, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo? Iwe uyenera kunditsata Ine.” 23Chifukwa cha ichi mbiri inafala pakati pa abale kuti wophunzira uyu sadzafa. Koma Yesu sananene kuti iye sadzafa. Iye anati, “Ine nditafuna kuti akhalebe ndi moyo mpaka nditabweranso, zikukukhudza bwanji zimenezo?”

24Uyu ndi wophunzira amene akuchitira umboni ndipo ndi amene analemba. Ife tidziwa kuti umboni wake ndi woona.

25Koma palinso zina zambiri zimene Yesu anachita. Zikanalembedwa zonsezi, ndikhulupirira dziko lonse lapansi likanasowa malo osungirako mabuku onse amene akanalembedwa.

Священное Писание (Восточный перевод), версия с «Аллахом»

Иохан 21:1-25

Чудесный улов рыбы

1Позже Иса опять явился Своим ученикам. Это было у Тивериадского озера. Произошло всё так: 2Шимон Петир, Фома, называемый Близнец, Нафанаил из Каны Галилейской, сыновья Завдая и два других ученика собрались вместе.

3– Я пойду ловить рыбу, – сказал Шимон Петир.

– Мы тоже пойдём с тобой, – решили остальные.

Они отплыли на лодке, но в ту ночь ничего не поймали.

4Рано утром Иса стоял на берегу, но ученики не узнали Его.

5Он позвал их:

– Друзья, ну как, есть у вас рыба?

– Нет, – ответили они.

6Он сказал:

– Забросьте сеть с правого борта и поймаете.

Они забросили и поймали столько рыбы, что не могли вытащить сеть. 7Ученик, которого любил Иса, сказал тогда Петиру:

– Это Повелитель!

Как только Петир услышал, что это Повелитель, он обвязался верхней одеждой, так как был раздет, и прыгнул в воду. 8Другие ученики поплыли за ним на лодке, подтягивая сеть, полную рыбы. Они были на расстоянии около девяноста метров21:8 Букв.: «около двухсот локтей». от берега. 9Когда они вышли на берег, то увидели горящие угли, на которых пеклась рыба, и рядом лежали лепёшки. 10Иса сказал им:

– Принесите несколько рыб из тех, что вы сейчас поймали.

11Шимон Петир зашёл в лодку и вытащил сеть на берег. В ней было сто пятьдесят три большие рыбы, однако сеть не порвалась! 12Иса сказал им:

– Идите сюда и позавтракайте.

Никто из учеников не осмеливался спросить Его: «Кто Ты?» Они знали, что это Повелитель. 13Иса подошёл, взял лепёшки и дал им, а также и рыбу. 14Это уже в третий раз Иса пришёл к Своим ученикам после того, как Он воскрес из мёртвых.

Разговор Исы аль-Масиха с Петиром

15Когда они закончили есть, Иса сказал Шимону Петиру:

– Шимон, сын Ионы21:15 Или: «Иохана». Иохан – второе имя Ионы. Также в ст. 16 и 17., ты действительно любишь Меня больше, чем они?

– Да, Повелитель, – ответил тот, – Ты знаешь, что я люблю Тебя.

Иса сказал:

– Тогда паси Моих ягнят21:15-17 Ягнята, овцы – так здесь аллегорически названы последователи Исы..

16И во второй раз Иса спросил его:

– Шимон, сын Ионы, любишь ли ты Меня?

Петир ответил:

– Да, Повелитель, Ты знаешь, что я люблю Тебя.

Иса сказал:

– Заботься о Моих овцах.

17Потом Иса в третий раз спросил Петира:

– Шимон, сын Ионы, ты любишь Меня?

Петир опечалился, что Иса спросил его в третий раз: «Любишь ли ты Меня?» – и ответил:

– Повелитель, Ты знаешь всё, Ты знаешь, что я люблю Тебя.

Иса сказал ему:

– Паси Моих овец. 18Говорю тебе истину: когда ты был молод, ты сам подпоясывался и шёл, куда хотел; но когда ты состаришься, то протянешь руки, и другой подпояшет тебя и поведёт туда, куда ты не захочешь.

19Иса сказал это, имея в виду, какой смертью Петир прославит Аллаха. Потом Он сказал ему:

– Следуй за Мной!

20Петир обернулся и увидел ученика, которого Иса любил, тот тоже шёл за ними. Это был тот самый ученик, который на ужине откинулся назад к Исе и спросил: «Повелитель, кто предаст Тебя?» 21Когда Петир его увидел, он спросил Ису:

– Повелитель, а с ним как будет?

22Иса ответил:

– Если даже Я захочу, чтобы он был жив, пока Я не приду21:22 Имеется в виду второе пришествие Исы аль-Масиха., то что тебе до этого? Ты следуй за Мной.

23После этих слов среди братьев распространился слух, что этот ученик не умрёт, но Иса не сказал, что он не умрёт; Он сказал лишь: «Если даже Я захочу, чтобы он был жив, пока Я не приду, то что тебе до этого?»

24Он и есть тот ученик, который свидетельствует об этом и который это записал. И мы знаем, что это свидетельство истинно.

25Иса сделал ещё и многое другое, и если бы всё это описать, то, я думаю, и всему миру не вместить написанных книг.