Yohane 20 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 20:1-31

Yesu Auka kwa Akufa

1Mmamawa tsiku loyamba la sabata, kukanali kamdimabe, Mariya wa ku Magadala anapita ku manda ndipo anaona kuti mwala unali utachotsedwa pa khomo la manda. 2Choncho anabwerera akuthamanga kwa Simoni Petro ndi wophunzira winayo, amene Yesu anamukonda, ndipo anati, “Iwo amuchotsa Ambuye mʼmanda, ndipo ife sitikudziwa kumene iwo amuyika Iye!”

3Choncho Petro ndi wophunzira winayo ananyamuka kupita ku manda. 4Onse awiri anathamanga pamodzi koma wophunzira winayo anamupitirira Petro, nafika ku manda moyambirira. 5Ndipo mmene anawerama nasuzumira mʼkati mwa manda anaona nsalu zili potero koma sanalowemo. 6Kenaka Simoni Petro, amene anali pambuyo pake, anafika ndi kulowa mʼmanda. Iye anaona nsaluzo zili pamenepo, 7pamodzinso ndi nsalu imene anakulungira nayo mutu wa Yesu. Nsaluyi inali yopindidwa pa yokha yosiyanitsidwa ndi inayo. 8Pomaliza wophunzira winayo, amene anafika ku manda moyambirira, analowanso mʼkati, iye anaona ndi kukhulupirira. 9(Iwo sanazindikire kuchokera mʼmalemba kuti Yesu anayanera kuuka kuchokera kwa akufa).

Yesu Aonekera kwa Mariya wa ku Magadala

10Kenaka ophunzira anabwerera ku nyumba zawo, 11koma Mariya anayima kunja kwa manda akulira. Pamene akulira, anawerama ndi kusuzumira mʼmanda 12ndipo anaona angelo awiri atavala zoyera, atakhala pamene panali mtembo wa Yesu, mmodzi kumutu ndi wina kumapazi.

13Iwo anamufunsa iye kuti, “Amayi, nʼchifukwa chiyani mukulira?”

Iye anati, “Amuchotsa Mbuye wanga, ndipo ine sindikudziwa kumene iwo amuyika.” 14Atanena izi, iye anatembenuka ndipo anaona Yesu atayima potero koma iye sanazindikire kuti anali Yesu.

15Iye anati, “Amayi, mukulira chifukwa chiyani? Ndani amene mukumufunafuna?”

Poganiza kuti anali mwini munda, iye anati, “Bwana, ngati inu mwamuchotsa, ndiwuzeni kumene mwamuyika, ndipo ine ndikamutenga.”

16Yesu anati kwa iye, “Mariya.”

Anatembenukira kwa Iye nafuwula mu Chiaramaiki kuti, “Raboni!” (kutanthauza Mphunzitsi).

17Yesu anati, “Usandigwire Ine, pakuti sindinapite kwa Atate. Mʼmalo mwake pita kwa abale anga ndikukawawuza kuti, ndikupita kwa Atate ndi kwa Atate anunso, kwa Mulungu wanga ndi Mulungu wanunso.”

18Mariya wa ku Magadala anapita kwa ophunzira ndi uthenga wakuti, “Ndamuona Ambuye!” Iye anawawuza iwo kuti Yesu ananena zinthu izi kwa iye.

Yesu Aonekera kwa Ophunzira ake Tomasi Palibe

19Madzulo a tsiku limenelo limene linali loyamba la Sabata ophunzira ake ali pamodzi, atatseka ndi kukhoma zitseko chifukwa choopa Ayuda, Yesu anabwera ndi kuyima pakati pawo nati, “Mtendere ukhale nanu!” 20Iye atatha kunena izi, anawaonetsa manja ake ndi mʼnthiti mwake. Ophunzira anasangalala kwambiri pamene anaona Ambuye.

21Yesu anatinso, “Mtendere ukhale nanu! Monga Atate anandituma Ine, Inenso ndikukutumani.” 22Ndi mawu amenewo Iye anawapumira ndipo anati, “Landirani Mzimu Woyera. 23Ngati mukhululukira aliyense machimo ake, iwo akhululukidwa; ngati simuwakhululukira, iwo sanakhululukidwe.”

Yesu Aonekera kwa Tomasi

24Koma Tomasi (otchedwa Didimo), mmodzi wa khumi ndi awiriwo, sanali ndi ophunzira pamene Yesu anabwera. 25Ophunzira enawo atamuwuza Tomasi kuti iwo anaona Ambuye, iye ananenetsa kuti, “Pokhapokha nditaona zizindikiro za misomali mʼmanja ake ndi kuyikamo chala changa mʼmene munali misomali ndi kukhudza dzanja langa mʼnthiti mwake, ine sindidzakhulupirira.”

26Patapita sabata, ophunzira ake analinso mʼnyumbamo ndipo Tomasi anali nawo. Ngakhale makomo anali otsekedwa, Yesu anabwera nayima pakati pawo, ndipo anati, “Mtendere ukhale nanu!” 27Kenaka anati kwa Tomasi, “Ika chala chako apa; ona manja anga. Tambasula dzanja lako ndi kukhudza mʼnthiti mwanga. Leka kukayika, khulupirira.”

28Tomasi anati kwa Iye, “Ambuye wanga ndi Mulungu wanga!”

29Kenaka Yesu anamuwuza kuti, “Kodi wakhulupirira chifukwa wandiona Ine? Ndi odala amene amakhulupirira ngakhale asanaone.”

Cholinga cha Uthenga Wabwino wa Yohane

30Yesu anachita zodabwitsa zambiri pamaso pa ophunzira ake zimene sizinalembedwe mʼbuku lino. 31Koma izi zalembedwa kuti mukhulupirire kuti Yesu ndi Khristu, Mwana wa Mulungu, ndi kuti mukakhulupirira mukhale nawo moyo mʼdzina lake.

Knijga O Kristu

Ivan 20:1-31

Isusovo uskrsnuće

(Mt 28:1-10; Mk 16:1-8; Lk 24:1-12)

1U nedjelju20:1 U grčkome: prvoga dana u tjednu. rano ujutro, još za mraka, dođe na grob Marija Magdalena i opazi da je odvaljen kamen s ulaza u grob. 2Otrči stoga pronaći Šimuna Petra i još jednog učenika, koga je Isus osobito volio, pa im reče: “Uzeli su Gospodinovo tijelo iz groba i ne znam kamo su ga stavili!”

3Petar tada iziđe s drugim učenikom te potrče prema grobu. 4Drugi učenik prestigne Petra i stigne onamo prvi, 5sagne se, zaviri unutra te spazi povoje od lanena platna gdje leže, ali ne uđe. 6Tada pristigne i Šimun Petar pa uđe u grob. I on ugleda povoje gdje leže 7i platno u koje je bila umotana Isusova glava kako presavijeno leži sa strane. 8Tada je ušao i drugi učenik, vidio i povjerovao— 9jer sve do tada nisu shvatili da Sveto pismo govori kako će Isus ustati od mrtvih. 10Vrate se kući.

Isus se pojavljuje pred Marijom Magdalenom

(Mt 28:9-10; Mk 16:9-11)

11Marija se vratila na grob i stajala vani plačući. Zaplakana se sagne i zaviri u grob 12te ugleda dva anđela obučena u bijelo kako sjede, jedan do glave, a drugi do nogu na mjestu gdje je ležalo Isusovo tijelo. 13“Zašto plačeš?” upitaju anđeli.

“Zato što su mi uzeli Gospodina,” odgovori ona, “a ne znam kamo su ga stavili!”

14Obazre se i ugleda da netko stoji iza nje. Bio je to Isus, ali ga nije prepoznala. 15“Zašto plačeš?” upita on. “Koga tražiš?”

Ona pomisli da je to vrtlar. “Gospodine,” reče, “ako ste ga vi odnijeli, recite mi kamo ste ga stavili pa ću otići i uzeti ga.”

16“Marijo!” reče joj Isus.

Ona se okrene prema njemu i uzvikne na hebrejskome: “Rabbuni!” (što znači: “Učitelju!”)

17“Nemoj me dulje zadržavati”, upozori ju, “jer još nisam uzišao k Ocu. Idi, nađi moju braću i javi im da uzlazim svojemu Ocu i vašemu Ocu, svojemu Bogu i vašemu Bogu.”

18Marija Magdalena ode javiti učenicima da je vidjela Gospodina i prenese im njegovu poruku.

Isus se pojavljuje pred učenicima

(Mt 28:16-20; Mk 16:14-18; Lk 24:36-49)

19Te su se večeri prvoga dana u tjednu učenici sastali iza zaključanih vrata zbog straha od židovskih vođa kad odjednom među njih stane Isus. Pozdravi ih: “Mir vama!” 20Kad im je to rekao, pokaže im svoje ruke i bok. Učenici se razvesele kad ugledaju svojega Gospodina. 21Isus im opet reče: “Mir vama! Kao što je mene poslao Otac, tako i ja šaljem vas.” 22Zatim dahne u njih i reče: “Primite Svetoga Duha! 23Kojima oprostite grijehe, oprošteni su im. Kojima ne oprostite grijehe, nisu im oprošteni.”

Isus se pojavljuje pred Tomom

24Jedan od Dvanaestorice, Toma zvani Blizanac, nije tada bio s drugima. 25“Vidjeli smo Gospodina”, rekli su mu, a on odgovori: “Ne vjerujem sve dok ne vidim rane od čavala na njegovim rukama, dok u njih ne stavim prste i dok ne stavim ruku u ranu na njegovu boku.”

26Nakon osam dana učenici su ponovno bili skupa. Taj je put s njima bio i Toma. Iako su vrata bila zatvorena, Isus stane među njih i pozdravi ih: “Mir vama!” 27Zatim reče Tomi: “Daj ovamo prst; evo mojih ruku! Stavi ruku u moj bok. Ne budi više nevjernik. Vjeruj!”

28“Moj Gospodin i moj Bog!” uzvikne Toma.

29Isus mu reče: “Ti vjeruješ jer si me vidio. Ali blago onima koji me nisu vidjeli, a vjeruju.”

Svrha ove knjige

30Isusovi učenici vidjeli su kako Isus čini i mnoga druga čuda osim zapisanih u ovoj knjizi. 31Ova su zapisana da vjerujete20:31 U nekim rukopisima: da i dalje vjerujete. da je Isus Mesija, Božji Sin, te da vjerujući u njega imate život.