Yohane 18 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 18:1-40

Amugwira Yesu

1Yesu atamaliza kupemphera, Iye anachoka ndi ophunzira ake ndi kuwoloka chigwa cha Kidroni. Kumbali inayo kunali munda wa Olivi, ndipo Iye ndi ophunzira ake analowamo.

2Tsopano Yudasi, amene anamupereka amadziwa malowo chifukwa Yesu ankakumana ndi ophunzira ake kumeneko. 3Choncho Yudasi anabwera ku munda, akutsogolera gulu la asilikali ndi akuluakulu ena ochokera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi. Iwo anali atanyamula miyuni, nyale ndi zida.

4Yesu, podziwa zonse zimene zimati zichitike kwa Iye, anatuluka ndi kuwafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndani?”

5Iwo anayankha kuti, “Yesu wa ku Nazareti.”

Yesu anati, “Ndine.” (Ndipo Yudasi womuperekayo anali atayima nawo pamenepo). 6Pamene Yesu anati, “Ndine,” iwo anabwerera mʼmbuyo ndi kugwa pansi.

7Iye anawafunsanso kuti, “Kodi mukumufuna ndani?”

Ndipo iwo anati, “Yesu wa ku Nazareti.”

8Yesu anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kuti Ndine. Ngati inu mukufuna Ine, asiyeni anthu awa apite.” 9Izi zinachitika kuti mawu amene Iye anayankhula akwaniritsidwe: “Ine sindinataye ndi mmodzi yemwe mwa iwo amene mwandipatsa.”

10Kenaka Simoni amene anali ndi lupanga analitulutsa ndi kutema nalo wantchito wa wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake la kudzanja lamanja. (Dzina la wantchitoyo ndi Makusi).

11Yesu analamula Petro kuti, “Bwezera lupanga mʼchimake! Kodi Ine ndisamwere chikho chimene Atate andipatsa?”

Amutengera Yesu kwa Anasi

12Kenaka gulu la asilikali ndi olamulira wawo ndi akuluakulu a Ayuda anamugwira Yesu. Iwo anamumanga. 13Poyamba anapita naye kwa Anasi amene anali mkamwini wa Kayafa, mkulu wa ansembe chaka chimenecho. 14Kayafa anali amene analangiza Ayuda kuti kukanakhala kwabwino ngati munthu mmodzi akanafera anthu.

Petro Akana Yesu Koyamba

15Simoni Petro ndi ophunzira wina ankamutsatira Yesu chifukwa ophunzira uyu amadziwika kwa mkulu wa ansembe. Iye analowa ndi Yesu mʼbwalo la mkulu wa ansembe 16koma Petro anadikira kunja pa khomo. Ophunzira winayo amene amadziwika kwa mkulu wa ansembe, anatuluka ndi kuyankhula ndi mtsikana amene anali mlonda wa pa khomo ndi kumulowetsa Petro.

17Mtsikanayo anafunsa Petro kuti, “Kodi iwe sindiwe mmodzi wa ophunzira a Munthu uyu?”

Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”

18Popeza kunkazizira, anyamata antchito ndi akuluakulu ena anasonkha moto wamakala namawotha atayimirira mozungulira. Petro nayenso anayimirira pamodzi ndi iwo namawotha nawo motowo.

Mkulu wa Ansembe Amufunsa Yesu

19Pa nthawi imeneyi, mkulu wa ansembe anamufunsa Yesu za ophunzira ake ndi chiphunzitso chake.

20Yesu anayankha kuti, “Ine ndinayankhula poyera ku dziko lapansi. Nthawi zonse ndimaphunzitsa mʼsunagoge kapena mʼNyumba ya Mulungu kumene Ayuda onse amasonkhana pamodzi. Ine sindimanena kanthu mseri. 21Nʼchifukwa chiyani mukundifunsa Ine? Afunseni amene amamva. Zoonadi akudziwa zimene Ine ndinanena.”

22Yesu atanena izi, mmodzi wa akuluakulu amene anali pafupi anamumenya kumaso. Iye anafunsa kuti, “Mayankhidwe awa ndi woti ndi kuyankha mkulu wa ansembe?”

23Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndanena kanthu kolakwika, chitirani umboni chimene ndalakwa. Koma ngati ndanena zoona, nʼchifukwa chiyani mwandimenya?” 24Kenaka Anasi anamutumiza Iye, ali womangidwabe, kwa Kayafa, mkulu wa ansembe.

Petro Akana Yesu Kachiwiri ndi Kachitatu

25Pamene Simoni Petro anali chiyimirire kuwotha moto, anafunsidwa kuti, “Kodi iwe si mmodzi wa ophunzira ake?”

Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”

26Mmodzi wa antchito a mkulu wa ansembe, mʼbale wa munthu amene anadulidwa khutu ndi Petro anamutsutsa iye kuti, “Kodi sindinakuone iwe pamodzi ndi Iye mʼmunda muja?” 27Petro anakananso, ndipo pa nthawi yomweyo tambala analira.

Yesu ku Bwalo la Pilato

28Kenaka Ayuda anamutenga Yesu kuchoka kwa Kayafa ndi kupita ku nyumba yaufumu ya bwanamkubwa wa Chiroma. Tsopano kunali mmamawa, ndipo polewa kudetsedwa monga mwa mwambo Ayuda sanalowe mʼnyumba yaufumuyo; iwo anafuna kuti adye Paska. 29Choncho Pilato anatuluka napita kwa iwo ndipo anati, “Kodi ndi milandu yanji imene mukumuzenga munthu uyu?”

30Iwo anayankha kuti, “Ngati Iye akanakhala kuti si wolakwa, ife sitikanamupereka kwa inu.”

31Pilato anati, “Mutengeni inu eni ake ndi kumuweruza Iye monga mwa malamulo anu.”

Ayuda anatsutsa nati, “Koma tilibe ulamuliro wakupha aliyense.” 32Izi zinachitika kuti mawu a Yesu amene anayankhula kusonyeza mtundu wa imfa imene Iye anati adzafe nayo akwaniritsidwe.

33Kenaka Pilato anapita mʼkati mwa nyumba yaufumu nayitanitsa Yesu, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi iwe ndi mfumu ya Ayuda?”

34Yesu anafunsa kuti, “Kodi amenewo ndi maganizo anu wokha? Kapena kuti ena anakuwuzani za Ine?”

35Pilato anayankha kuti, “Kodi iwe ukuganiza kuti ine ndine Myuda? Ndi anthu ako ndi akulu a ansembe ako amene akupereka iwe kwa ine. Kodi walakwanji?”

36Yesu anati, “Ufumu wanga si wa dziko lapansi lino. Ukanakhala wa pansi pano, antchito anga akanachita nkhondo kulepheretsa Ayuda kundigwira. Koma tsopano ufumu wanga ndi wochokera kumalo ena.”

37Pilato anati, “Kani ndiwe mfumu!”

Yesu anayankha kuti, “Inu mwalondola ponena kuti, Ine ndine mfumu. Kunena zoona, Ine ndinabadwa chifukwa cha chimenechi, ndipo nʼchifukwa chake ndinabwera mʼdziko lapansi, kudzachitira umboni choonadi. Aliyense amene ali mbali yachoonadi amamvera mawu anga.”

38Pilato anafunsa kuti, “Kodi choonadi nʼchiyani?” Ndi mawu awa iye anapitanso kwa Ayuda ndipo anati, “Ine sindikupeza mlandu mwa Iye. 39Koma ndi mwambo wanu kuti pa nthawi ya Paska, ine ndikumasulireni wamʼndende mmodzi. Kodi mufuna ndikumasulireni ‘Mfumu ya Ayuda?’ ”

40Iwo anafuwula nati, “Ameneyu ayi! Mutipatse ife Baraba!” Barabayo anali wachifwamba.

New Russian Translation

Иоанна 18:1-40

Иисус предан и арестован

(Мат. 26:47-56; Мк. 14:43-50; Лк. 22:47-53)

1Сказав это, Иисус пошел со Своими учениками на другую сторону Кедронской долины, где был сад, в который они и вошли. 2Предатель Иуда знал это место, так как Иисус часто собирался там со Своими учениками. 3Поэтому Иуда привел туда с собой отряд римских воинов, а также слуг, посланных первосвященниками и фарисеями. Они пришли с фонарями, факелами и оружием. 4Иисус знал все, что должно было с Ним произойти. Он вышел вперед и спросил:

– Кого вы ищете?

5– Иисуса из Назарета, – ответили те.

– Это Я18:5 Букв.: «Я есть» (ср. Исх. 3:14); также в ст. 6, 8., – сказал Иисус.

Предатель Иуда тоже стоял с ними. 6Когда Иисус сказал: «Это Я», они отступили назад и упали на землю.

7Он опять спросил их:

– Кого вы ищете?

– Иисуса из Назарета, – сказали они.

8– Я же вам сказал, что это Я, – ответил Иисус. – Если вы ищете Меня, то отпустите остальных.

9Он сказал это, чтобы исполнились Его слова: «Я не потерял никого из тех, кого Ты дал Мне»18:9 См. 6:39; 17:12..

10У Симона Петра был меч, он выхватил его, ударил слугу первосвященника и отсек ему правое ухо. Слугу звали Малх. 11Тогда Иисус сказал Петру:

– Вложи меч в ножны! Разве Я не должен выпить чашу, которую дал Мне Отец?

Иисус на допросе у Анны

(Мат. 26:57; Мк. 14:53-54; Лк. 22:54)

12Отряд римских воинов, их командир и иудейские стражники арестовали Иисуса и связали Его. 13Они привели Его вначале к Анне. Анна был тестем Кайафы, который был в тот год первосвященником18:13 Анна был первосвященником в период с 6 по 15 гг. и не утратил своего влияния и после этого. А его зять Кайафа занимал этот пост с 18 по 36 гг.. 14Это был Кайафа, который убеждал иудеев, что будет лучше, если один человек умрет за народ18:14 См. 11:49-51..

Первое отречение Петра

(Мат. 26:69-70; Мк. 14:66-68; Лк. 22:54-57)

15Симон Петр и еще один ученик шли следом за Иисусом. Первосвященник знал этого ученика, и поэтому тот смог пройти с Иисусом во двор, 16а Петр остался снаружи у ворот. Ученик, который был знаком первосвященнику, вышел, поговорил с привратницей и провел Петра внутрь.

17– Ты случайно не один из учеников Этого Человека? – спросила привратница.

– Нет, – ответил Петр.

18Было холодно. Слуги и стражники разложили костер и грелись у него. Петр тоже стоял у костра и грелся.

Иисус на допросе у Анны

19Тем временем первосвященник допрашивал Иисуса о Его учениках и учении.

20– Я открыто говорил миру, – отвечал Иисус, – Я всегда учил в синагогах или в храме, там, где собираются все иудеи. Тайного Я ничего не говорил. 21Зачем ты Меня допрашиваешь? Спроси тех, кто Меня слушал, они наверняка знают, что Я говорил.

22Когда Иисус это сказал, один из стоявших поблизости служителей ударил Иисуса по лицу.

– Ты как разговариваешь с первосвященником! – возмутился он.

23– Если Я сказал что-то не так, то укажи, что не так, – ответил Иисус. – Если же Я прав, то зачем ты бьешь Меня?

24Анна отослал Иисуса связанным к первосвященнику Кайафе.

Второе и третье отречение Петра

(Мат. 26:71-75; Мк. 14:69-72; Лк. 22:58-62)

25Симон Петр все стоял и грелся у костра, когда его еще раз спросили:

– Ты случайно не один из Его учеников?

Петр отрицал.

– Нет, – сказал он.

26Тогда один из слуг первосвященника, родственник того, которому Петр отсек ухо, сказал:

– Разве не тебя я видел с Ним в саду?

27Петр снова стал все отрицать, и в этот момент пропел петух.

Иисус на допросе у Пилата

(Мат. 27:11-14; Мк. 15:2-5; Лк. 23:2-5)

28От Кайафы Иисуса повели в резиденцию наместника. Было раннее утро, и иудеи, опасаясь оскверниться, не вошли в здание, иначе они не смогли бы потом есть пасхальный ужин18:28 Как такового запрета входить в дома, принадлежащие не иудеям, в Законе нет. Этот запрет (см. Деян. 10:28) был дан иудеям их религиозными учителями. Говоря же о праздничном ужине, надо помнить, что часто, когда иудеи говорили о Пасхе, они имели в виду и сам праздник Пасхи, и следующий за ним праздник Пресных хлебов (см. Лк. 22:1).. 29Поэтому Пилат18:29 Пилат – Понтий Пилат был римским наместником в Иудее с 26 по 36 гг. вышел к ним.

– В чем вы обвиняете Этого Человека? – спросил он.

30– Не будь Он преступником, мы бы не привели Его к тебе, – ответили они.

31Пилат сказал:

– Берите Его сами и судите по вашему Закону.

– Но у нас нет права никого казнить, – возразили иудеи.

32Так должны были исполниться слова Иисуса о том, какой смертью Он умрет18:32 То есть смерть на кресте (см. 3:14; 8:28; 12:32). Крест был римским орудием казни. Иудеи же, если бы имели на то право от римских властей, скорее всего, побили бы Иисуса камнями (см. Лев. 24:16).. 33Тогда Пилат вошел внутрь своей резиденции, вызвал Иисуса и спросил Его:

– Ты Царь иудеев?

34– Ты это от себя говоришь, или тебе обо Мне сказали другие? – спросил в ответ Иисус.

35– Я что, иудей? – ответил Пилат. – Это Твой народ и первосвященники передали Тебя мне. Что Ты сделал?

36Иисус сказал:

– Царство Мое – не одно из царств этого мира. Если бы оно было таким, то Мои подданные сражались бы за Меня, чтобы Я не был передан иудеям. Но сейчас Мое Царство не отсюда.

37– Так значит, Ты все-таки Царь? – спросил Пилат.

– Ты сам говоришь, что Я Царь, – ответил Иисус. – Я родился и пришел в мир, чтобы свидетельствовать об истине. Всякий, кто на стороне истины, слушает Меня.

38Пилат спросил:

– Что есть истина?

Потом он опять вышел к иудеям и сказал:

– Я не нахожу в Нем никакой вины.

Пилат осуждает Иисуса на распятие

(Мат. 27:15-31; Мк. 15:6-20; Лк. 23:13-25)

39– У вас есть обычай, чтобы я на Пасху отпускал на свободу одного из заключенных. Хотите, чтобы я отпустил вам «Царя иудеев»?

40Они в ответ закричали:

– Нет! Не Его! Отпусти нам Варавву!18:40 Это имя переводится как «сын отца».

Варавва же был мятежником18:40 Или: «разбойником»..