Yohane 18 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 18:1-40

Amugwira Yesu

1Yesu atamaliza kupemphera, Iye anachoka ndi ophunzira ake ndi kuwoloka chigwa cha Kidroni. Kumbali inayo kunali munda wa Olivi, ndipo Iye ndi ophunzira ake analowamo.

2Tsopano Yudasi, amene anamupereka amadziwa malowo chifukwa Yesu ankakumana ndi ophunzira ake kumeneko. 3Choncho Yudasi anabwera ku munda, akutsogolera gulu la asilikali ndi akuluakulu ena ochokera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi. Iwo anali atanyamula miyuni, nyale ndi zida.

4Yesu, podziwa zonse zimene zimati zichitike kwa Iye, anatuluka ndi kuwafunsa kuti, “Kodi mukufuna ndani?”

5Iwo anayankha kuti, “Yesu wa ku Nazareti.”

Yesu anati, “Ndine.” (Ndipo Yudasi womuperekayo anali atayima nawo pamenepo). 6Pamene Yesu anati, “Ndine,” iwo anabwerera mʼmbuyo ndi kugwa pansi.

7Iye anawafunsanso kuti, “Kodi mukumufuna ndani?”

Ndipo iwo anati, “Yesu wa ku Nazareti.”

8Yesu anayankha kuti, “Ine ndakuwuzani kuti Ndine. Ngati inu mukufuna Ine, asiyeni anthu awa apite.” 9Izi zinachitika kuti mawu amene Iye anayankhula akwaniritsidwe: “Ine sindinataye ndi mmodzi yemwe mwa iwo amene mwandipatsa.”

10Kenaka Simoni amene anali ndi lupanga analitulutsa ndi kutema nalo wantchito wa wamkulu wa ansembe, nadula khutu lake la kudzanja lamanja. (Dzina la wantchitoyo ndi Makusi).

11Yesu analamula Petro kuti, “Bwezera lupanga mʼchimake! Kodi Ine ndisamwere chikho chimene Atate andipatsa?”

Amutengera Yesu kwa Anasi

12Kenaka gulu la asilikali ndi olamulira wawo ndi akuluakulu a Ayuda anamugwira Yesu. Iwo anamumanga. 13Poyamba anapita naye kwa Anasi amene anali mkamwini wa Kayafa, mkulu wa ansembe chaka chimenecho. 14Kayafa anali amene analangiza Ayuda kuti kukanakhala kwabwino ngati munthu mmodzi akanafera anthu.

Petro Akana Yesu Koyamba

15Simoni Petro ndi ophunzira wina ankamutsatira Yesu chifukwa ophunzira uyu amadziwika kwa mkulu wa ansembe. Iye analowa ndi Yesu mʼbwalo la mkulu wa ansembe 16koma Petro anadikira kunja pa khomo. Ophunzira winayo amene amadziwika kwa mkulu wa ansembe, anatuluka ndi kuyankhula ndi mtsikana amene anali mlonda wa pa khomo ndi kumulowetsa Petro.

17Mtsikanayo anafunsa Petro kuti, “Kodi iwe sindiwe mmodzi wa ophunzira a Munthu uyu?”

Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”

18Popeza kunkazizira, anyamata antchito ndi akuluakulu ena anasonkha moto wamakala namawotha atayimirira mozungulira. Petro nayenso anayimirira pamodzi ndi iwo namawotha nawo motowo.

Mkulu wa Ansembe Amufunsa Yesu

19Pa nthawi imeneyi, mkulu wa ansembe anamufunsa Yesu za ophunzira ake ndi chiphunzitso chake.

20Yesu anayankha kuti, “Ine ndinayankhula poyera ku dziko lapansi. Nthawi zonse ndimaphunzitsa mʼsunagoge kapena mʼNyumba ya Mulungu kumene Ayuda onse amasonkhana pamodzi. Ine sindimanena kanthu mseri. 21Nʼchifukwa chiyani mukundifunsa Ine? Afunseni amene amamva. Zoonadi akudziwa zimene Ine ndinanena.”

22Yesu atanena izi, mmodzi wa akuluakulu amene anali pafupi anamumenya kumaso. Iye anafunsa kuti, “Mayankhidwe awa ndi woti ndi kuyankha mkulu wa ansembe?”

23Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine ndanena kanthu kolakwika, chitirani umboni chimene ndalakwa. Koma ngati ndanena zoona, nʼchifukwa chiyani mwandimenya?” 24Kenaka Anasi anamutumiza Iye, ali womangidwabe, kwa Kayafa, mkulu wa ansembe.

Petro Akana Yesu Kachiwiri ndi Kachitatu

25Pamene Simoni Petro anali chiyimirire kuwotha moto, anafunsidwa kuti, “Kodi iwe si mmodzi wa ophunzira ake?”

Iye anayankha kuti, “Ayi, sindine.”

26Mmodzi wa antchito a mkulu wa ansembe, mʼbale wa munthu amene anadulidwa khutu ndi Petro anamutsutsa iye kuti, “Kodi sindinakuone iwe pamodzi ndi Iye mʼmunda muja?” 27Petro anakananso, ndipo pa nthawi yomweyo tambala analira.

Yesu ku Bwalo la Pilato

28Kenaka Ayuda anamutenga Yesu kuchoka kwa Kayafa ndi kupita ku nyumba yaufumu ya bwanamkubwa wa Chiroma. Tsopano kunali mmamawa, ndipo polewa kudetsedwa monga mwa mwambo Ayuda sanalowe mʼnyumba yaufumuyo; iwo anafuna kuti adye Paska. 29Choncho Pilato anatuluka napita kwa iwo ndipo anati, “Kodi ndi milandu yanji imene mukumuzenga munthu uyu?”

30Iwo anayankha kuti, “Ngati Iye akanakhala kuti si wolakwa, ife sitikanamupereka kwa inu.”

31Pilato anati, “Mutengeni inu eni ake ndi kumuweruza Iye monga mwa malamulo anu.”

Ayuda anatsutsa nati, “Koma tilibe ulamuliro wakupha aliyense.” 32Izi zinachitika kuti mawu a Yesu amene anayankhula kusonyeza mtundu wa imfa imene Iye anati adzafe nayo akwaniritsidwe.

33Kenaka Pilato anapita mʼkati mwa nyumba yaufumu nayitanitsa Yesu, ndipo anamufunsa kuti, “Kodi iwe ndi mfumu ya Ayuda?”

34Yesu anafunsa kuti, “Kodi amenewo ndi maganizo anu wokha? Kapena kuti ena anakuwuzani za Ine?”

35Pilato anayankha kuti, “Kodi iwe ukuganiza kuti ine ndine Myuda? Ndi anthu ako ndi akulu a ansembe ako amene akupereka iwe kwa ine. Kodi walakwanji?”

36Yesu anati, “Ufumu wanga si wa dziko lapansi lino. Ukanakhala wa pansi pano, antchito anga akanachita nkhondo kulepheretsa Ayuda kundigwira. Koma tsopano ufumu wanga ndi wochokera kumalo ena.”

37Pilato anati, “Kani ndiwe mfumu!”

Yesu anayankha kuti, “Inu mwalondola ponena kuti, Ine ndine mfumu. Kunena zoona, Ine ndinabadwa chifukwa cha chimenechi, ndipo nʼchifukwa chake ndinabwera mʼdziko lapansi, kudzachitira umboni choonadi. Aliyense amene ali mbali yachoonadi amamvera mawu anga.”

38Pilato anafunsa kuti, “Kodi choonadi nʼchiyani?” Ndi mawu awa iye anapitanso kwa Ayuda ndipo anati, “Ine sindikupeza mlandu mwa Iye. 39Koma ndi mwambo wanu kuti pa nthawi ya Paska, ine ndikumasulireni wamʼndende mmodzi. Kodi mufuna ndikumasulireni ‘Mfumu ya Ayuda?’ ”

40Iwo anafuwula nati, “Ameneyu ayi! Mutipatse ife Baraba!” Barabayo anali wachifwamba.

Knijga O Kristu

Ivan 18:1-40

Isusovo uhićenje

(Mt 26:47-56; Mk 14:43-50; Lk 22:47-53)

1Rekavši to, Isus sa svojim učenicima prijeđe na drugu stranu potoka Kedrona te uđe s njima u maslinik. 2A izdajnik Juda poznavao je to mjesto jer je Isus često onamo odlazio sa svojim učenicima. 3Svećenički poglavari i farizeji dali su Judi četu vojnika i stražare da odu onamo. Oni stignu do maslinika sa zapaljenim bakljama, svjetiljkama i oružjem.

4Isus je znao što će se sve dogoditi. On istupi pred njih i upita: “Koga tražite?”

5“Isusa iz Nazareta!” odgovore oni.

“Ja sam”, reče Isus. S njima je stajao i njegov izdajnik Juda. 6Kad im je rekao “Ja sam”, svi ustuknu i popadaju na zemlju. 7Ponovno ih upita: “Koga tražite?”

Opet odgovore: “Isusa iz Nazareta!”

8“Rekao sam vam: ja sam”, odgovori Isus. “Ja sam taj kojega tražite. Pustite druge neka idu.” 9Rekao je to da bi se ispunilo proročanstvo koje je upravo spomenuo: “Nisam izgubio nijednoga od ovih koje si mi dao.”18:9 Vidjeti: Ivan 6:39; 17:12.

10Tada Šimun Petar potegne mač i odsiječe desno uho sluzi velikog svećenika, koji se zvao Malko. 11Ali Isus reče Petru: “Spremi mač u korice! Zar da ne ispijem čašu koju mi je Otac dao?”

Ana ispituje Isusa

(Mt 26:57, 69-70; Mk 14:66-68; Lk 22:54-57)

12Tako židovski stražari s četom vojnika i njihovim zapovjednikom uhvate Isusa i svežu ga. 13Odvedu ga najprije Ani, tastu Kajfe, koji je te godine bio veliki svećenik. 14Kajfa je bio taj koji je savjetovao židovskim vođama: “Bolje da jedan čovjek umre za narod.”

Petar se prvi put odriče Isusa

15Šimun Petar i još jedan učenik koji je poznavao velikog svećenika izdaleka su ih slijedili. Tako je taj drugi učenik mogao ući u dvorište velikog svećenika skupa s Isusom, 16a Petar je ostao vani, pred vratima. Drugi učenik tada porazgovara sa sluškinjom koja je pazila kraj vrata pa ona uvede i Petra. 17Ta sluškinja, vratarica, upita Petra: “Nisi li i ti jedan od Isusovih učenika?”

“Nisam”, odvrati Petar.

18Stražari i služinčad stajali su pokraj vatre koju su naložili i grijali se jer je bilo hladno. I Petar je stajao ondje s njima grijući se.

Veliki svećenik ispituje Isusa

19Unutra veliki svećenik počne ispitivati Isusa o njegovim učenicima i o onome što ih je poučavao. 20Isus odgovori: “Što sam poučavao, naširoko je poznato jer sam redovito poučavao u sinagogi i u Hramu. Čuli su me svi Židovi i ništa nisam poučavao tajno a da to nisam i javno rekao. 21Zašto to mene pitaš? Pitaj one koji su me slušali. Oni znaju što sam govorio!”

22Jedan od vojnika koji je ondje stajao šakom udari Isusa po licu. “Zar se tako odgovara velikom svećeniku?” upita.

23“Ako sam pogrešno rekao, dokaži da je pogrešno”, odgovori Isus. “Zar ćeš udarati čovjeka samo zato što govori istinu?”

24Tada Ana pošalje svezanoga Isusa velikome svećeniku Kajfi.

Petar se drugi put odriče Isusa

(Mt 26:71-75; Mk 14:69-72; Lk 22:58-62)

25U međuvremenu, dok se Šimun Petar grijao kraj vatre, ponovno ga upitaju: “Da nisi i ti jedan od njegovih učenika?”

“Nisam!” odgovori on.

26Ali jedan od slugu velikoga svećenika, rođak onoga kojemu je Petar odsjekao uho, upita ga: “Zar te nisam vidio ondje u masliniku skupa s Isusom?” 27Petar opet zaniječe. A pijetao odmah zakukuriče.

Isus pred Pilatom

28Isusovo preslušanje pred Kajfom završilo je u rane jutarnje ure. Zatim ga odvedu u palaču rimskoga upravitelja. Njegovi tužitelji nisu sâmi onamo ulazili jer bi ih ulazak onečistio pa ne bi smjeli jesti pashalnu večeru. 29Zato Pilat, upravitelj, iziđe k njima te ih upita: “Za što optužujete ovog čovjeka?”

30“Ne bismo ga predali tebi da nije zločinac!” odgovore oni.

31“Onda ga odvedite i sami mu sudite po svojim zakonima”, reče Pilat.

“Ali nama nije dopušteno ubiti čovjeka!”—kazaše. 32Time se ispunilo Isusovo proročanstvo o njegovu smaknuću.18:32 Vidjeti: Ivan 12:32-33.

33Tada se Pilat vrati u palaču i naredi da mu dovedu Isusa. “Jesi li ti kralj Židova?” upita ga.

34“Jesi li se tog pitanja dosjetio sam ili su ti drugi govorili o meni?” upita ga Isus.

35“Zar sam ja Židov?” odgovori Pilat. “Tvoj vlastiti narod i svećenički poglavari predali su te meni. Zašto? Što si učinio?”

36Isus odgovori: “Moje kraljevstvo ne pripada ovomu svijetu. Kad bi mu pripadalo, moji bi se podanici borili da ne budem predan Židovima. Ali moje kraljevstvo nije od ovoga svijeta!”

37Pilat upita: “Ti dakle jesi kralj?” “Ti to kažeš”, odgovori Isus. “Da, ja sam kralj; rodio sam se da bih svjedočio za istinu. Svaki onaj koji voli istinu poslušat će moj glas.”

38Pilat upita: “A što je istina?” Tada ponovno iziđe pred židovski narod i reče im: “Ja na njemu nisam našao nikakve krivnje. 39A vi svake godine u vrijeme Pashe imate običaj tražiti da vam pustim nekoga iz zatvora. Hoćete li da oslobodim židovskoga kralja?”

40Ali oni nato poviču: “Ne! Ne njega, nego Barabu!” A Baraba je bio prevratnik.