Yohane 16 – CCL & SNC

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 16:1-33

1“Ine ndakuwuzani zonsezi kuti musadzakhumudwe. 2Iwo adzakuchotsani mʼsunagoge mwawo. Kunena zoona, nthawi ikubwera imene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti akutumikira Mulungu. 3Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso. 4Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”

Ntchito ya Mzimu Woyera

5“Tsopano Ine ndikupita kwa Iye amene anandituma koma palibe wina mwa inu akundifunsa kuti, ‘Kodi mukupita kuti?’ 6Muli ndi chisoni kwambiri chifukwa ndakuwuzani zimene. 7Komatu ndakuwuzani zoona. Ine ndikuti kuli bwino kwa inu kuti ndichoke. Ngati sindichoka, Nkhosweyo sidzabwera kwa inu, koma ngati Ine ndipita, ndidzamutumiza kwa inu. 8Iye akabwera, adzatsutsa dziko lapansi za uchimo, zachilungamo ndi zachiweruzo. 9Za uchimo, chifukwa anthu sakhulupirira Ine. 10Za chilungamo, chifukwa Ine ndi kupita kwa Atate, kumene simudzandionanso. 11Za chiweruzo, chifukwa wolamulira dziko lino lapansi waweruzidwa tsopano.

12“Ine ndili ndi zambiri zoti ndiyankhule nanu, koma simungathe kuzilandira tsopano. 13Koma pamene Iye, Mzimu wachoonadi, abwera, adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Iye sadzayankhula mwa Iye yekha, adzayankhula zokhazo zimene wamva ndipo Iye adzakuwuzani zimene zikubwera. 14Iye adzalemekeza Ine chifukwa adzatenga za Ine nadzakudziwitsani. 15Zonse za Atate ndi zanga. Ichi nʼchifukwa chake Ine ndanena kuti Mzimu Woyera adzatenga kwa Ine zanga kuti muzidziwe.”

Chisoni cha Ophunzira Chisandulika Chimwemwe

16Yesu anapitiriza kuyankhula kuti, “Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso, ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso.”

17Ena a ophunzira ake anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi Iye akutanthauza chiyani ponena kuti, ‘Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso,’ ndi ‘ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso,’ ndiponso ‘chifukwa ndikupita kwa Atate?’ ” 18Iwo anapitiriza kufunsana kuti, “Kodi akutanthauza chiyani, ‘kanthawi kochepa?’ Ife sitikumvetsetsa chimene Iye akuyankhula.”

19Yesu anadziwa kuti ankafuna kuti amufunse za zimenezi, choncho anawafunsa kuti, “Kodi mukufunsana wina ndi mnzake chimene Ine ndimatanthauza pamene ndinati, ‘Mwa kanthawi kochepa simudzandionanso,’ ndi ‘patatha nthawi pangʼono mudzandionanso?’ 20Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti inu mudzalira ndi kubuma pomwe dziko lapansi lidzakhale likukondwera. Inu mudzamva chisoni, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe. 21Mayi akamabereka mwana amamva ululu chifukwa nthawi yake yafika; koma mwana wake akabadwa amayiwala ululu wake chifukwa cha chimwemwe chake chakuti mwana wabadwa mʼdziko lapansi. 22Chimodzimodzinso ndi inu. Tsopano ino ndi nthawi yanu yomva chisoni, koma Ine ndidzakuonaninso ndipo inu mudzasangalala, ndipo palibe amene adzachotsa chimwemwe chanu. 23Tsiku limenelo inu simudzandipemphanso kalikonse. Ine ndikukuwuzani zoona kuti Atate anga adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa. 24Mpaka tsopano simunapemphe kalikonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.

25“Ngakhale ndakhala ndikuyankhula mʼmafanizo, nthawi ikubwera imene Ine sindidzagwiritsanso ntchito mafanizo otere koma ndidzakuwuzani momveka za Atate anga. 26Tsiku limenelo inu mudzapempha mʼdzina langa. Ine sindikunena kuti ndidzapempha Atate mʼmalo mwanu ayi. 27Atate mwini anakukondani chifukwa inu mwandikonda Ine ndipo mwakhulupirira kuti Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate. 28Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate ndi kulowa mʼdziko lapansi. Tsopano ndikulisiya dziko lapansi kubwerera kwa Atate.”

29Kenaka ophunzira ake anati, “Tsopano mukuyankhula momveka bwino ndi mopanda mafanizo. 30Tsopano ife tikuona kuti Inu mumadziwa zinthu zonse ndi kuti sipafunika wina aliyense kukufunsani. Mwa ichi ife takhulupirira kuti Inu munachokera kwa Mulungu.”

31Yesu anawafunsa kuti, “Kodi tsopano mwakhulupirira?” 32Koma nthawi ikubwera ndipo yafika, pamene inu mudzabalalitsidwa, aliyense ku nyumba yake. Inu mudzandisiya ndekhandekha. Koma Ine sindili ndekha, pakuti Atate anga ali nane.

33“Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi.”

Slovo na cestu

Jan 16:1-33

1Těmito slovy jsem vás chtěl varovat, abyste nepodlehli zmatku z budoucích událostí. 2Nejdříve vás vyženou ze synagog. Pak vás budou dokonce zabíjet v domnění, že tím slouží Bohu. 3Budou to dělat, protože nepoznali Otce ani mne. 4Říkám to proto, abyste se na má slova rozpomněli, až se naplní.

Zatím jsem o tom nemluvil, protože jsem byl s vámi.

Ježíš učí o Duchu svatém

5-6Můj čas se však naplnil a já brzy odejdu k tomu, který mne poslal. Vidím však, že nechápete, kam jdu. Místo abyste se radovali, jste stísněni smutkem a starostmi. 7Věřte mi, že pro vás bude lepší, když odejdu. Kdybych zůstal, Zastánce by k vám nepřišel. Odejdu-li, pošlu ho k vám.

8Až přijde, ukáže lidem, v čem spočívá hřích, zda existuje spravedlnost a koho je třeba soudit.

9Hřích je v tom, že lidé ve mne nevěří. 10Spravedlnost je v tom, že Bůh potrestal Krista jako zástupce hříšníků, vzkřísil ho a přijal do své slávy. 11A soud znamená, že uchvatitel tohoto světa je již odsouzen.

12Je toho ještě mnoho, co bych vám chtěl říci, ale vy to nemůžete v této chvíli pochopit. 13Teprve až přijde Duch svatý, odkryje vám plnou pravdu. 14On bude jejím věrným tlumočníkem. Oznámí vám i to, co má přijít.

15Nebude zdůrazňovat sebe, ale vyvyšovat mne, protože mně Otec svěřil všechno. A tak co vám sdělí Duch, bude ukazovat vždycky ke mně.

Ježíš učí o užívání jeho jména v modlitbě

16Zanedlouho již mezi vámi nebudu, ale brzy potom mě znovu uvidíte. Pak půjdu zase k Otci.“

17-18„O čem to jen mluví?“ ptali se učedníci jeden druhého. „Kde bude zanedlouho? Kdy ho zase uvidíme? Co to znamená, že půjde k Otci? Tomu nerozumíme.“

19Ježíš poznal, že si učedníci s jeho slovy nevědí rady. „Vysvětlím vám to,“ řekl. 20„Brzy se svět bude radovat z mého utrpení, zatímco vy budete plakat. Ale váš pláč se záhy promění v radost, protože mne opět uvidíte. 21Vaše radost se bude podobat radosti ženy, která zapomněla na všechnu úzkost a porodní bolesti, protože se jí narodilo dítě. 22-23Nyní jste smutní, ale budete se zase radovat, až se setkáme. O tuto radost vás nikdo nepřipraví. Pak všechno pochopíte.

24Znovu vás vyzývám, abyste se ve svých modlitbách k Otci na mne odvolávali a on vás vyslyší. Proste, Bůh vás obdaruje a vaše radost bude plná.

25Dosud jsem o těchto věcech mluvil v podobenstvích, ale brzy budu o Otci hovořit otevřeně. 26Nespoléhejte se na to, že já budu prosit Otce za vás, ale vy se modlete a odvolávejte na mne. 27Vždyť vás Otec miluje pro vaši lásku ke mně a pro víru, se kterou jste mne přijali jako Božího Syna.

28Pravda je nejen to, že jsem od Otce přišel, ale i to, že se k němu opět vrátím.“

29„Teď už ti rozumíme,“ přisvědčili učedníci. „Co jsi dříve říkal v náznacích, pověděl jsi teď jasně. 30Pochopili jsme, že víš všechno a rozumíš už napřed našim otázkám. Teď opravdu věříme, že jsi přišel od Boha.“

31„Opravdu tomu věříte?“ otázal se jich Ježíš. 32„Nastane čas, vlastně už nastal, kdy se rozprchnete do svých domovů a necháte mne samotného. Já však nebudu sám, protože Otec je se mnou. 33Toto všechno jsem vám řekl proto, abyste ve spojení se mnou našli jistotu a klid. Svět vám připraví mnoho těžkostí, ale neztrácejte odvahu. Já jsem nad ním zvítězil.“