Yohane 13 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 13:1-38

Yesu Asambitsa Mapazi a Ophunzira Ake

1Inali pafupifupi nthawi ya phwando la Paska. Yesu anadziwa kuti nthawi yafika yoti achoke mʼdziko lapansi ndi kupita kwa Atate. Atawakonda ake amene anali mʼdziko lapansi, Iye anawaonetsa chikondi chake chonse.

2Atayamba kudya mgonero, mdierekezi anali atalowa kale mu mtima wa Yudasi Isikarioti mwana wa Simoni, kuti amupereke Yesu. 3Yesu podziwa kuti Atate anamupatsa Iye zonse mʼmanja mwake, ndi kuti Iye anachokera kwa Mulungu ndipo amabwerera kwa Mulunguyo; 4anayimirira kuchoka pa chakudya navula zovala zake natenga nsalu yopukutira nadzimanga mʼchiwuno mwake. 5Atachita izi, anathira madzi mʼbeseni ndi kuyamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira chimene anachimanga mʼchiwuno mwake.

6Atafika pa Petro, Petroyo anati kwa Iye, “Ambuye, kodi mudzandisambitsa mapazi anga?”

7Yesu anayankha kuti, “Iwe sukuzindikira tsopano chimene ndikuchita, koma udzazindikira mʼtsogolo.”

8Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.”

Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.”

9Simoni Petro anayankha kuti, “Ambuye, osati mapazi okha komanso manja anga ndi mutu wanga womwe!”

10Yesu anayankha kuti, “Munthu amene wasamba amangofunika kusamba mapazi ake okha chifukwa thupi lake lonse ndi loyera. Ndipo inu ndinu oyera, ngakhale kuti si aliyense mwa inu.” 11Pakuti Iye anadziwa amene adzamupereka, ndipo nʼchifukwa chake anati saliyense wa inu ali woyera.

12Iye atamaliza kusambitsa mapazi awo anavala zovala zake ndi kubwerera pamalo pake. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuzindikira zimene ndakuchitirani inu? 13Inu mumanditcha Ine, ‘Mphunzitsi’ ndi ‘Mbuye,’ ndipo mumakhoza mukamatero, pakuti ichi ndi chimene Ine ndili. 14Tsono ngati Ine, Mbuye wanu ndi Mphunzitsi wanu, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi anu. 15Ine ndakupatsani chitsanzo kuti muzichita monga Ine ndachitira. 16Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti wantchito saposa mbuye wake, kapena wotumidwa kuposa amene wamutuma. 17Ngati inu mudziwa zinthu zimenezi, mudzakhala odala mukamazichita.

Yesu Aneneratu za Kuperekedwa Kwake

18“Ine sindikunena za inu nonse. Ine ndikudziwa amene ndinawasankha. Koma izi zikukwaniritsa malemba: ‘Iye amene akudya nawo chakudya changa, ndiye amene anandiwukira.’

19“Ine ndikukuwuzani tsopano zisanachitike zimenezi, kuti pamene zachitika, mudzakhulupirire kuti Ine Ndine. 20Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene alandira amene Ine ndamutuma, alandiranso Ine. Aliyense amene alandira Ine, alandiranso amene anandituma.”

Yesu Aneneratu za Kuperekedwa Kwake

21Yesu atanena izi, anavutika kwambiri mu mzimu ndipo anachitira umboni kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mmodzi mwa inu adzandipereka.”

22Ophunzira ake anapenyetsetsana wina ndi mnzake, posadziwa kuti amanena za yani. 23Mmodzi wa ophunzira ake amene Yesu anamukonda, anali atatsamira pachifuwa chake. 24Simoni Petro anamukodola wophunzirayo ndi kuti, “Mufunseni akunena za yani.”

25Atamutsamiranso Yesuyo, anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndani?”

26Yesu anayankha kuti, “Iye amene ndidzamupatsa buledi amene ndanyema ndikususa ndi ameneyo.” Kenaka, atasunsa gawo la buledi, Iye anapereka kwa Yudasi Isikarioti, mwana wa Simoni. 27Nthawi yomweyo Yudasi atangodya bulediyo, Satana analowa mwa Iye.

Yesu anamuwuza Iye kuti, “Chomwe ukufuna kuchita, chita msanga.” 28Koma panalibe ndi mmodzi yemwe pa chakudyapo amene anamvetsa chifukwa chimene Yesu ananenera izi kwa iye. 29Popeza Yudasi amasunga ndalama, ena amaganiza kuti Yesu amamuwuza iye kuti akagule zomwe zimafunika pa phwando, kapena kukapereka kanthu kena kake kwa osauka. 30Nthawi yomweyo Yudasi atangodya buledi, anatuluka, ndipo unali usiku.

Yesu Aneneratu kuti Petro Adzamukana

31Yudasi atatuluka, Yesu anati, “Tsopano Mwana wa Munthu walemekezedwa, ndipo mwa Iyeyu Mulungu walemekezedwanso. 32Ngati Mulungu walemekezedwa mwa Iye, Mulungu mwini adzalemekezanso Mwana, ndipo amulemekeza nthawi yomweyo.

33“Ana anga, Ine ndikhala nanu kwa nthawi yochepa chabe. Inu mudzandifunafuna Ine, ndipo monga momwe ndinawawuzira Ayuda, choncho Ine ndikukuwuzani tsopano kuti, kumene Ine ndikupita, inu simungabwereko.

34“Lamulo latsopano limene ndikukupatsani ndi lakuti: Kondanani wina ndi mnzake, monga momwe Ine ndinakonda inu. Nanunso mukondane wina ndi mnzake. 35Mukamakondana aliyense adzadziwa kuti ndinu ophunzira anga.”

36Simoni Petro anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukupita kuti?”

Yesu anayankha kuti, “Kumene Ine ndikupita iwe sunganditsatire tsopano, koma udzanditsatira mʼtsogolo.”

37Petro anafunsa kuti, “Ambuye, nʼchifukwa chiyani ine sindingakutsatireni tsopano? Ine ndidzapereka moyo wanga chifukwa cha Inu.”

38Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe udzalolera kutaya moyo chifukwa cha Ine? Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti tambala asanalire, iwe udzandikana katatu!”

New Russian Translation

Иоанна 13:1-38

Иисус омывает ноги ученикам

1Приближался праздник Пасхи. Иисус знал, что настал час Ему покинуть этот мир и вернуться к Отцу. Полюбив Своих, находящихся в этом мире, Он полюбил их до конца.

2Во время ужина, когда дьявол уже побудил Иуду Искариота, сына Симона, предать Иисуса, 3Иисус, зная, что Отец отдал все в руки Его и что Он пришел от Бога и теперь возвращается к Богу, 4встал из-за стола, снял с Себя верхнюю одежду и опоясался полотенцем. 5Потом Он налил воды в таз и начал мыть Своим ученикам ноги и вытирать их полотенцем, которым был опоясан. 6Когда Он подошел к Симону Петру, тот сказал Ему:

– Господи, Тебе ли мыть мне ноги?!

7Иисус сказал ему:

– Сейчас ты не понимаешь, что Я делаю, но позже поймешь.

8– Ты никогда не вымоешь моих ног! – возразил Петр.

Иисус ответил:

– Если Я не омою тебя, то у тебя нет со Мной ничего общего.

9Симон Петр ответил:

– Тогда, Господи, омой мне не только ноги, но и руки и голову!

10Иисус ответил:

– Омытого нет нужды мыть, разве только ноги, так как все его тело чисто. Вы ведь чисты, хотя и не все.

11Он знал, кто предаст Его, и поэтому сказал, что не все чисты.

12Окончив мыть ученикам ноги, Иисус снова оделся и, возвратившись, возлег на Своем месте за столом.

– Вы понимаете, что Я сделал для вас? – спросил Он их. – 13Вот вы называете Меня Учителем и Господом, и правильно, потому что Я и есть Учитель и Господь. 14Поэтому если Я, ваш Господь и Учитель, омыл вам ноги, то вы тоже должны мыть ноги друг другу. 15Я показал вам пример, чтобы и вы делали то же, что Я сделал вам. 16Говорю вам истину: слуга не больше своего господина, и посланный не больше пославшего его. 17Если вы это знаете и так поступаете, то вы блаженны.

18Я не говорю о всех вас. Тех, кого Я избрал, Я знаю, но слова Писания: «Тот, кто ест Мой хлеб, поднял свою пяту против Меня»13:18 Пс. 40:10. – должны исполниться. 19Говорю вам обо всем заранее, чтобы, когда это произойдет, вы поверили, что Я и есть Тот,13:19 Букв.: «Я есть». Часто в Писании, когда Бог говорил о Себе, Он употреблял это же самое выражение (см., напр., Исх. 3:14; Втор. 32:39; Ис. 41:4; 43:10-13 и сноски на эти стихи). Здесь виден явный намек Иисуса на то, Кем Он в действительности является. за Кого Себя выдаю. 20Говорю вам истину, кто принимает посланного Мною, тот принимает и Меня, и кто принимает Меня, тот принимает и Пославшего Меня.

Последний пасхальный ужин Иисуса с учениками

(Мат. 26:20-25; Мк. 14:17-21; Лк. 22:21-23)

21Сказав это, Иисус произнес в большом волнении:

– Говорю вам истинную правду: один из вас предаст Меня.

22Ученики стали растерянно переглядываться между собой, недоумевая, кого Он имеет в виду. 23Один из учеников, которого Иисус любил, возлежал у стола рядом с Ним. 24Симон Петр показал ему жестом:

– Спроси, кого Он имеет в виду?

25Откинувшись назад к Иисусу, ученик спросил:

– Господи, кто это?

26Иисус ответил:

– Тот, кому Я подам этот кусок хлеба, обмакнув его в блюдо.

И, обмакнув кусок, Иисус протянул его Иуде Искариоту, сыну Симона. 27Как только Иуда взял хлеб, в него вошел сатана.

– Делай быстро то, что собираешься делать, – сказал ему Иисус.

28Никто за столом не понял, зачем Иисус сказал ему это. 29Иуда отвечал за ящик с общими деньгами, и некоторые подумали, что Иисус попросил его купить необходимое к празднику или же раздать часть денег бедным. 30Взяв хлеб, Иуда сразу же вышел. Была ночь.

Иисус дает ученикам заповедь любви

31Когда Иуда вышел, Иисус сказал:

– Теперь Сын Человеческий прославлен, а в Нем прославлен Бог. 32Если Бог прославлен в Нем, то Бог прославит в Себе и Его, и немедленно прославит. 33Дети Мои, недолго Мне еще быть с вами. Вы будете искать Меня, и, как Я говорил иудеям, так говорю и вам: «Туда, куда Я иду, вы не можете прийти».

34Я даю вам новую заповедь: любите друг друга. Как Я вас полюбил, так и вы любите друг друга. 35Все узнают, что вы Мои ученики, если вы будете любить друг друга!

Иисус предсказывает отречение Петра

(Мат. 26:33-35; Мк. 14:29-31; Лк. 22:33-34)

36Симон Петр спросил Его:

– Господи, куда Ты идешь?

Иисус ответил:

– Туда, куда Я иду, ты сейчас со Мной пойти не сможешь, но позже ты пойдешь.

37Петр спросил:

– Господи, почему я не могу идти за Тобой сейчас? Да я готов даже жизнь отдать за Тебя.

38Иисус тогда сказал:

– Ты отдашь за Меня свою жизнь? Говорю тебе истинную правду: не успеет сегодня и петух пропеть, как ты трижды отречешься от Меня.