Yohane 13 – CCL & CRO

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 13:1-38

Yesu Asambitsa Mapazi a Ophunzira Ake

1Inali pafupifupi nthawi ya phwando la Paska. Yesu anadziwa kuti nthawi yafika yoti achoke mʼdziko lapansi ndi kupita kwa Atate. Atawakonda ake amene anali mʼdziko lapansi, Iye anawaonetsa chikondi chake chonse.

2Atayamba kudya mgonero, mdierekezi anali atalowa kale mu mtima wa Yudasi Isikarioti mwana wa Simoni, kuti amupereke Yesu. 3Yesu podziwa kuti Atate anamupatsa Iye zonse mʼmanja mwake, ndi kuti Iye anachokera kwa Mulungu ndipo amabwerera kwa Mulunguyo; 4anayimirira kuchoka pa chakudya navula zovala zake natenga nsalu yopukutira nadzimanga mʼchiwuno mwake. 5Atachita izi, anathira madzi mʼbeseni ndi kuyamba kusambitsa mapazi a ophunzira ake, ndi kuwapukuta ndi chopukutira chimene anachimanga mʼchiwuno mwake.

6Atafika pa Petro, Petroyo anati kwa Iye, “Ambuye, kodi mudzandisambitsa mapazi anga?”

7Yesu anayankha kuti, “Iwe sukuzindikira tsopano chimene ndikuchita, koma udzazindikira mʼtsogolo.”

8Petro anati, “Ayi, Inu simudzandisambitsa konse mapazi anga.”

Yesu anayankha kuti, “Ngati Ine sindisambitsa mapazi ako, ulibe gawo mwa Ine.”

9Simoni Petro anayankha kuti, “Ambuye, osati mapazi okha komanso manja anga ndi mutu wanga womwe!”

10Yesu anayankha kuti, “Munthu amene wasamba amangofunika kusamba mapazi ake okha chifukwa thupi lake lonse ndi loyera. Ndipo inu ndinu oyera, ngakhale kuti si aliyense mwa inu.” 11Pakuti Iye anadziwa amene adzamupereka, ndipo nʼchifukwa chake anati saliyense wa inu ali woyera.

12Iye atamaliza kusambitsa mapazi awo anavala zovala zake ndi kubwerera pamalo pake. Iye anawafunsa kuti, “Kodi mukuzindikira zimene ndakuchitirani inu? 13Inu mumanditcha Ine, ‘Mphunzitsi’ ndi ‘Mbuye,’ ndipo mumakhoza mukamatero, pakuti ichi ndi chimene Ine ndili. 14Tsono ngati Ine, Mbuye wanu ndi Mphunzitsi wanu, ndasambitsa mapazi anu, inunso muyenera kusambitsana mapazi anu. 15Ine ndakupatsani chitsanzo kuti muzichita monga Ine ndachitira. 16Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti wantchito saposa mbuye wake, kapena wotumidwa kuposa amene wamutuma. 17Ngati inu mudziwa zinthu zimenezi, mudzakhala odala mukamazichita.

Yesu Aneneratu za Kuperekedwa Kwake

18“Ine sindikunena za inu nonse. Ine ndikudziwa amene ndinawasankha. Koma izi zikukwaniritsa malemba: ‘Iye amene akudya nawo chakudya changa, ndiye amene anandiwukira.’

19“Ine ndikukuwuzani tsopano zisanachitike zimenezi, kuti pamene zachitika, mudzakhulupirire kuti Ine Ndine. 20Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene alandira amene Ine ndamutuma, alandiranso Ine. Aliyense amene alandira Ine, alandiranso amene anandituma.”

Yesu Aneneratu za Kuperekedwa Kwake

21Yesu atanena izi, anavutika kwambiri mu mzimu ndipo anachitira umboni kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti mmodzi mwa inu adzandipereka.”

22Ophunzira ake anapenyetsetsana wina ndi mnzake, posadziwa kuti amanena za yani. 23Mmodzi wa ophunzira ake amene Yesu anamukonda, anali atatsamira pachifuwa chake. 24Simoni Petro anamukodola wophunzirayo ndi kuti, “Mufunseni akunena za yani.”

25Atamutsamiranso Yesuyo, anamufunsa Iye kuti, “Ambuye, kodi ndani?”

26Yesu anayankha kuti, “Iye amene ndidzamupatsa buledi amene ndanyema ndikususa ndi ameneyo.” Kenaka, atasunsa gawo la buledi, Iye anapereka kwa Yudasi Isikarioti, mwana wa Simoni. 27Nthawi yomweyo Yudasi atangodya bulediyo, Satana analowa mwa Iye.

Yesu anamuwuza Iye kuti, “Chomwe ukufuna kuchita, chita msanga.” 28Koma panalibe ndi mmodzi yemwe pa chakudyapo amene anamvetsa chifukwa chimene Yesu ananenera izi kwa iye. 29Popeza Yudasi amasunga ndalama, ena amaganiza kuti Yesu amamuwuza iye kuti akagule zomwe zimafunika pa phwando, kapena kukapereka kanthu kena kake kwa osauka. 30Nthawi yomweyo Yudasi atangodya buledi, anatuluka, ndipo unali usiku.

Yesu Aneneratu kuti Petro Adzamukana

31Yudasi atatuluka, Yesu anati, “Tsopano Mwana wa Munthu walemekezedwa, ndipo mwa Iyeyu Mulungu walemekezedwanso. 32Ngati Mulungu walemekezedwa mwa Iye, Mulungu mwini adzalemekezanso Mwana, ndipo amulemekeza nthawi yomweyo.

33“Ana anga, Ine ndikhala nanu kwa nthawi yochepa chabe. Inu mudzandifunafuna Ine, ndipo monga momwe ndinawawuzira Ayuda, choncho Ine ndikukuwuzani tsopano kuti, kumene Ine ndikupita, inu simungabwereko.

34“Lamulo latsopano limene ndikukupatsani ndi lakuti: Kondanani wina ndi mnzake, monga momwe Ine ndinakonda inu. Nanunso mukondane wina ndi mnzake. 35Mukamakondana aliyense adzadziwa kuti ndinu ophunzira anga.”

36Simoni Petro anafunsa kuti, “Ambuye, kodi mukupita kuti?”

Yesu anayankha kuti, “Kumene Ine ndikupita iwe sunganditsatire tsopano, koma udzanditsatira mʼtsogolo.”

37Petro anafunsa kuti, “Ambuye, nʼchifukwa chiyani ine sindingakutsatireni tsopano? Ine ndidzapereka moyo wanga chifukwa cha Inu.”

38Kenaka Yesu anayankha kuti, “Kodi iwe udzalolera kutaya moyo chifukwa cha Ine? Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti tambala asanalire, iwe udzandikana katatu!”

Knijga O Kristu

Ivan 13:1-38

Isus pere noge učenicima

1Večer uoči Pashe, znajući da je došao trenutak da ode sa zemlje svojemu Ocu i voleći svoje koji su na svijetu, Isus je vokio svoje učenike do samoga kraja. 2Za vrijeme večere đavao je već dao mig Judi Iškariotskomu, Šimunovu sinu, da je to noć u kojoj će izdati Isusa. 3A Isus, svjestan da mu je Otac predao sve u ruke, da je od Boga došao i da mu se vraća, 4ustane od stola, skine gornju odjeću, opaše se ručnikom, 5nalije vode te počne učenicima prati noge i brisati ih ručnikom kojim se opasao.

6Kad je došao do Šimuna Petra, on mu reče: “Učitelju, nećeš valjda ti meni prati noge!”

7Isus mu odgovori: “Sada još ne razumiješ zašto to radim, ali jednog ćeš dana shvatiti.”

8“Ne,” prosvjedovao je Petar, “nikad ti nećeš meni prati noge!”

“Ali ako te ne operem, ne možeš biti jedan od mojih”, odgovori mu Isus.

9Šimun Petar nato poviče: “Gospodine, operi mi onda i ruke i glavu, a ne samo noge!”

10Isus odgovori: “Tko je sav okupan, ne treba mu prati drugo osim nogu da bude posve čist. Sada ste čisti, ali ipak ne svi.” 11Isus je, naime, znao tko će ga izdati. Zato je i rekao: “Niste svi čisti.”

12Kad im opere noge, ponovno se obuče, sjedne i upita: “Razumijete li što sam vam učinio? 13Vi me zovete ‘Učiteljem’ i ‘Gospodinom’. Imate pravo! To i jesam. 14I zato, ako sam ja, Gospodin i Učitelj, vama oprao noge, trebate i vi prati noge jedni drugima. 15Dao sam vam primjer, činite kao što sam i ja učinio. 16Zaista vam kažem, nije sluga veći od svojega gospodara niti je poslanik veći od onoga koji ga šalje. 17To znate, a blago vama budete li tako i činili!”

Isus pretkazuje da će biti izdan

(Mt 26:17-30; Mk 14:12-26; Lk 22:7-23)

18“Ne govorim o svima vama, iako dobro poznajem vas koje sam odabrao. Sveto pismo kaže:

‘Onaj koji je sa mnom blagovao,

podiže se na me.’13:18 Psalam 41:10.

19Velim vam ovo već sada, prije nego što se dogodi, da kad se dogodi, vjerujete da Ja jesam. 20Zaista vam kažem, tko lijepo primi onoga koga ja šaljem, prima mene. A primi li tko mene, znači da je primio Oca koji me je poslao.”

21Rekavši to, duboko potresen u duhu, Isus im otvoreno reče: “Zaista vam kažem, jedan od vas će me izdati!”

22Učenici pogledaju jedan drugoga pitajući se na koga bi se to moglo odnositi. 23Jedan od Isusovih učenika, onaj kojega je Isus osobito volio,13:23 Najvjerojatnije Ivan. sjedio je za stolom odmah uz Isusa. 24Šimun Petar mu dade znak da upita Isusa tko bi mogao učiniti takvo strašno djelo. 25On se nagne prema Isusu13:25 U grčkome: naslonio Isusu na prsa. i upita ga: “Tko je taj, Gospodine?”

26Isus odgovori: “Kojemu dâm umočen kruh.” Umoči zatim kruh i dade ga Judi, sinu Šimuna Iškariotskoga. 27Čim Juda pojede kruh, u njega uđe Sotona. Tada mu Isus reče: “Brzo čini to što kaniš učiniti!” 28Nitko od nazočnih za stolom nije razumio zašto je Isus to rekao. 29Kako im je Juda bio blagajnik, neki pomisle da ga Isus šalje kupiti hrane za blagdane ili podijeliti novac siromašnima. 30Čim je uzeo kruh, Juda iziđe u noć.

Isus pretkazuje da će ga se Petar odreći

(Mt 26:31-35; Mk 14:27-31; Lk 22:31-34)

31Čim je Juda izišao, Isus reče: “Sada je vrijeme da ja, Sin Čovječji, uđem u svoju slavu, a Bog će biti proslavljen svime što će se meni dogoditi. 32Bog će me proslaviti u sebi, i to odmah.13:32 U nekim rukopisima: Ako je Bog proslavljen u njemu, i Bog će njega proslaviti u sebi 33Draga moja djeco, kako su kratki ovi trenuci prije nego što ću morati otići i ostaviti vas! A onda, budete li me i tražili, i kao što sam rekao i Židovima: ‘Kamo ja idem, vi ne možete doći.’ 34Dajem vam novu zapovijed: da volite jedni druge. Volite se međusobno onako kako sam ja volio vas. 35Budete li imali ljubavi jedni prema drugima, po tomu će svi znati da ste moji učenici.”

36“Kamo ideš, učitelju?” upita ga Šimun Petar.

Isus mu odgovori: “Sada ne možeš poći sa mnom, ali poslije ćeš me slijediti.”

37Petar upita: “Zašto sada ne mogu s tobom? Ja sam za tebe spreman i umrijeti!”

38Isus mu odgovori: “Umrijeti za mene? Zaista ti kažem, prije nego što pijetao zakukuriče, triput ćeš zanijekati da me uopće poznaješ.”