Yohane 11 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 11:1-57

Imfa ndi Kuukitsidwa kwa Lazaro

1Tsopano munthu wina dzina lake Lazaro anadwala. Iye anali wa ku Betaniya, mudzi wa Mariya ndi mchemwali wake Marita. 2Mariyayo ndi yemwe uja amene anadzoza Ambuye ndi mafuta onunkhira napukuta mapazi ake ndi tsitsi lake. Lazaro wodwalayo anali mlongo wake. 3Choncho alongo ake anatumiza mawu kwa Yesu kuti, “Ambuye, uja amene Inu mumamukonda akudwala.”

4Atamva izi, Yesu anati, “Kudwalako safa nako. Koma akudwala kuti Mulungu alemekezedwe; ndi kuti Mwana wa Mulungu alemekezedwe chifukwa cha matendawo.” 5Yesu anakonda Marita, mchemwali wake ndi Lazaro. 6Koma atamva kuti Lazaro akudwala, Iye anakhalabe kumene anali masiku ena awiri.

7Kenaka anati kwa ophunzira ake, “Tiyeni tibwerere ku Yudeya.”

8Ophunzira akewo anati, “Rabi, posachedwa pomwepa Ayuda anafuna kukugendani ndi miyala, koma Inu mukupitanso komweko?”

9Yesu anayankha kuti, “Kodi sipali maora khumi ndi awiri pa tsiku? Munthu amene amayenda masana sapunthwa, popeza akuona chifukwa cha kuwala kwa dziko lapansi. 10Koma amene akuyenda usiku amapunthwa, chifukwa kuwalako alibe.”

11Iye atatha kunena izi, anapitirira kuwawuza iwo kuti, “Bwenzi lathu Lazaro wagona tulo; koma Ine ndikupita kumeneko kukamudzutsa.”

12Ophunzira ake anayankha kuti, “Ambuye, ngati wagona adzapeza bwino.” 13Yesu ankayankhula za imfa yake koma ophunzira ake ankaganiza kuti amanena za tulo chabe.

14Ndipo kenaka anawawuza momveka kuti, “Lazaro wamwalira. 15Ine ndikukondwera chifukwa cha inu kuti kunalibe kumeneko; koma kuti mukakhulupirire tiyeni tipiteko.”

16Pamenepo Tomasi, wotchedwa Didimo, anati kwa ophunzira anzake, “Tiyeni nafenso tipite, kuti tikafere naye pamodzi.”

Yesu Atonthoza Alongo a Lazaro

17Yesu atafika, anapeza kuti Lazaro anali atagona mʼmanda masiku anayi. 18Mudzi wa Betaniya unali pafupi ndi Yerusalemu pa mtunda wosachepera makilomita atatu, 19ndipo Ayuda ambiri anabwera kwa Marita ndi Mariya kudzawatonthoza pa imfa ya mʼbale wawo. 20Pamene Marita anamva kuti Yesu akubwera, anapita kukakumana naye. Koma Mariya anatsala ku nyumba.

21Marita anati kwa Yesu, “Ambuye, mukanakhala muli kuno, mlongo wanga sakanamwalira. 22Koma ine ndikudziwa kuti ngakhale tsopano Mulungu adzakupatsani chilichonse chimene mudzamupempha.”

23Yesu anati kwa iye, “Mlongo wako adzauka.”

24Marita anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti adzauka pa kuukanso pa tsiku lomaliza.”

25Yesu anati kwa iye, “Ine ndine kuuka ndi moyo. Wokhulupirira Ine, angakhale amwalira adzakhala ndi moyo. 26Aliyense amene ali ndi moyo ndi kukhulupirira Ine sadzamwalira. Kodi iwe ukukhulupirira izi?”

27Marita anamuwuza Iye kuti, “Inde Ambuye, ine ndikukhulupirira kuti ndinu Khristu, Mwana wa Mulungu, amene abwera mʼdziko lapansi.”

28Ndipo iye atanena izi anabwerera ndi kukayitana mchemwali wake Mariya namuyankhula monongʼona pambali, nati, “Aphunzitsi abwera ndipo akukuyitana.” 29Mariya atamva izi, anayimirira mofulumira napita kwa Iye. 30Tsopano nʼkuti Yesu asanalowe mʼmudzi, koma anali akanali pa malo pamene Marita anakumana naye. 31Ayuda amene ankamutonthoza Mariya mʼnyumba, anaona mmene iye anayimira mofulumira ndi kutuluka kunja, iwo anamutsata akuganizira kuti ankapita ku manda kukalirira kumeneko.

32Mariya anafika pamalo pamene panali Yesu ndipo atamuona, anagwa pa mapazi ake ndipo anati, “Ambuye mukanakhala muli kuno mlongo wanga sakanamwalira.”

33Yesu ataona iye akulira, ndi Ayuda amene anabwera naye akuliranso, anakhudzidwa kwambiri ndi kuvutika mu mzimu. 34Iye anafunsa kuti, “Kodi mwamuyika kuti?”

Iwo anayankha kuti, “Ambuye tiyeni mukaone.”

35Yesu analira.

36Pamenepo Ayuda anati, “Taonani mmene Iye anamukondera Lazaro!”

37Koma ena a iwo anati, “Iye amatsekula maso a munthu wosaona, kodi sakanakhoza kuletsa kuti munthu uyu asamwalire?”

Yesu Aukitsa Lazaro

38Yesu atakhudzidwanso kwambiri anafika ku manda. Manda akewo anali phanga ndipo anatsekapo ndi mwala. 39Yesu anati, “Chotsani mwala.”

Marita mlongo wa womwalirayo anati, “Koma Ambuye, nthawi ino wayamba kununkha, pakuti wakhala mʼmenemu masiku anayi.”

40Kenaka Yesu anati, “Kodi Ine sindinakuwuze kuti ngati iwe ukhulupirira, udzaona ulemerero wa Mulungu?”

41Choncho iwo anachotsa mwalawo. Kenaka Yesu anayangʼana kumwamba ndikuti, “Atate, Ine ndikukuthokozani chifukwa mumandimvera. 42Ine ndimadziwa kuti Inu mumandimvera nthawi zonse, koma Ine ndanena izi chifukwa cha anthu amene ayima pano, kuti iwo akhulupirire kuti Inu munandituma Ine.”

43Yesu atanena izi, Iye anayitana ndi mawu ofuwula kuti, “Lazaro, tuluka!” 44Munthu womwalirayo anatuluka, womangidwa miyendo ndi manja ndi nsalu za ku manda, ndi nkhope yake yokulungidwa nsalu.

Yesu anawawuza kuti, “Mʼmasuleni, ndipo muloleni apite.”

Ayuda Apangana za Kupha Yesu

45Choncho Ayuda ambiri amene anabwera kudzamuchereza Mariya ndi kuona zimene Yesu anachita anamukhulupirira Iye. 46Koma ena a iwo anapita kwa Afarisi ndi kukawawuza zimene Yesu anachita. 47Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anayitanitsa msonkhano wa akulu olamulira.

Iwo anafunsa kuti, “Kodi ife tikuchita chiyani? Pano pali munthu uyu akuchita zizindikiro zodabwitsa zambiri. 48Ngati ife timuleka kuti apitirize chotere, aliyense adzamukhulupirira Iye, ndipo kenaka Aroma adzabwera ndi kudzatenga malo athu pamodzi ndi dziko lathu.”

49Kenaka mmodzi wa iwo, dzina lake Kayafa, amene anali mkulu wa ansembe chaka chimenecho, anayankhula kuti, “Inu simukudziwa kanthu kalikonse! 50Inu simukuzindikira kuti kuli bwino kwa inu kuti munthu mmodzi afe mʼmalo mwa anthu kusiyana ndi kuti mtundu wonse uwonongeke.”

51Iye sananene izi mwa iye yekha, koma monga mkulu wa ansembe chaka chimenecho ananenera kuti Yesu anayanera kufera mtundu wa Ayuda, 52ndipo osati mtundu okhawo komanso kwa ana ena a Mulungu onse obalalikana, kuti awabweretse pamodzi ndi kuwapanga kukhala amodzi. 53Choncho kuyambira tsiku limeneli iwo anakonzekera za kuti amuphe.

54Chifukwa cha ichi Yesu sanayendenso moonekera pakati pa Ayuda. Mʼmalo mwake Iye anapita ku chigawo cha kufupi ndi chipululu, ku mudzi wa Efereimu, kumene Iye anakhalako ndi ophunzira ake.

55Nthawi ya Paska wa Ayuda itayandikira, ambiri anakwera kupita ku Yerusalemu kuchokera ku madera a ku midzi chifukwa cha mwambo wa kuyeretsedwa Paska asanafike. 56Iwo anapitiriza kumufunafuna Yesu, ndipo pamene ankayimirira mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafunsana wina ndi mnzake kuti, “Kodi ukuganiza chiyani? Kodi Iye sabwera konse kuphwando?” 57Koma akulu a ansembe ndi Afarisi anapereka lamulo kuti ngati wina aliyense adziwe kumene kunali Yesu, iye akawawuze kuti akamugwire.

New Russian Translation

Иоанна 11:1-57

Болезнь и смерть Лазаря

1Один человек, которого звали Лазарь, был болен. Он был из Вифании, селения, где жили Мария и ее сестра Марфа. 2Мария и была той женщиной, что помазала Господа ароматическим маслом и вытерла Его ноги своими волосами. И вот ее брат Лазарь был болен. 3Сестры передали Иисусу:

– Господи, тот, кого Ты любишь, болен.

4Когда Иисус услышал об этом, Он сказал:

– Эта болезнь не к смерти, она для славы Божьей, чтобы Сын Бога был прославлен через нее.

5Иисус любил Марфу, ее сестру Марию и Лазаря. 6Однако когда Он узнал, что Лазарь болен, то пробыл там, где Он тогда находился, еще два дня. 7Затем Он сказал Своим ученикам:

– Пойдем обратно в Иудею.

8– Рабби, – сказали они Ему, – иудеи ведь еще недавно хотели побить Тебя камнями, а Ты хочешь туда возвратиться?

9Иисус ответил:

– Разве не двенадцать часов в сутках светло? Тот, кто ходит днем, не споткнется, потому что он видит свет этого мира. 10А тот, кто ходит ночью, споткнется, потому что в это время темно.

11Сказав это, Иисус добавил:

– Наш друг Лазарь заснул, но Я иду разбудить его.

12Ученики Его сказали:

– Господи, если он спит, значит, выздоровеет.

13Иисус говорил им о том, что Лазарь умер, но ученики думали, что Он говорит о сне обыкновенном. 14Тогда Он сказал им прямо:

– Лазарь умер. 15Ради вас и ради того, чтобы вы поверили, Я рад, что Меня там не было. Но сейчас пойдем к нему.

16Тогда Фома, которого еще называли Близнец, сказал остальным ученикам:

– Пойдем и мы и умрем с Ним!

Иисус утешает Марию и Марфу

17Придя туда, Иисус узнал, что тело Лазаря уже четыре дня в могиле. 18Вифания была стадиях в пятнадцати11:18 То есть менее чем в трех километрах. от Иерусалима, 19и к Марфе с Марией пришло много иудеев, чтобы выразить свое соболезнование по поводу смерти их брата. 20Когда Марфа услышала, что пришел Иисус, она пошла встретить Его, а Мария осталась дома.

21– Господи, – сказала Марфа Иисусу, – если бы Ты был здесь, то мой брат не умер бы. 22Но я знаю, что Бог и сейчас даст Тебе все, что бы Ты ни попросил.

23Иисус сказал ей:

– Твой брат воскреснет.

24Марфа ответила:

– Я знаю, что он воскреснет в День воскресения, в последний День.

25Иисус сказал ей:

– Я – воскресение и жизнь. Тот, кто верит в Меня, если и умрет – оживет, 26а кто живет и верит в Меня, тот никогда не умрет. Ты этому веришь?

27– Да, Господи, – сказала она, – я верю, что Ты Христос, Сын Бога, Который пришел в мир.

28Сказав это, Марфа вернулась, отозвала свою сестру в сторону и сказала:

– Учитель здесь, Он зовет тебя.

29Когда Мария это услышала, она тут же побежала Ему навстречу. 30Иисус еще не вошел в селение и стоял там, где Марфа Его встретила. 31Когда иудеи, бывшие с ней в доме и утешавшие ее, заметили, как она быстро встала и вышла, они пошли за ней, решив, что она пошла к могиле плакать.

32Мария пришла туда, где был Иисус, и, увидев Его, упала к Его ногам, говоря:

– Господи, если бы Ты был здесь, мой брат бы не умер.

33Иисус, видя, что плачет и она, и иудеи, которые с ней, и Сам сильно расстроился и опечалился11:33 Сильно опечалился – возможен другой перевод: «вознегодовал». В этом случае, Иисус мог вознегодовать на людей, видя их неверие; или же Он негодовал на действия сатаны, ведущие к смерти..

34– Куда вы его положили? – спросил Он.

– Пойдем, и Ты Сам увидишь, Господин, – сказали они.

35Иисус заплакал. 36Иудеи говорили между собой:

– Смотрите, как Он его любил.

Иисус воскрешает Лазаря из мертвых

37Некоторые, однако же, говорили:

– Неужели Он, Который открыл глаза слепому, не мог сделать так, чтобы этот человек не умер?

38Иисус, все еще печальный11:38 Печальный – или «негодуя»., пошел к могиле. Это была пещера в скале, ко входу которой был привален камень.

39– Уберите камень, – велел Он.

Марфа, сестра умершего, сказала:

– Господи, но там ведь уже тяжелый запах – Лазарь четыре дня как в могиле.

40Тогда Иисус сказал:

– Разве Я не говорил тебе, что если ты будешь верить, то увидишь Божью славу?

41Тогда камень убрали. Иисус же посмотрел на небо и сказал:

– Отец, благодарю Тебя за то, что Ты услышал Меня. 42Я знаю, что Ты всегда слышишь Меня, но Я сказал это ради тех, кто стоит здесь, чтобы они поверили, что Ты послал Меня.

43Сказав это, Иисус громко позвал:

– Лазарь, выходи!

44Умерший вышел. Его руки и ноги были обвязаны погребальными полотнами, а лицо закрыто платком.

– Развяжите его, пусть он идет, – сказал Иисус.

Заговор религиозных вождей

45Многие из иудеев, которые пришли навестить Марию и видели, что сделал Иисус, поверили в Него. 46Но некоторые из них пошли к фарисеям и рассказали им обо всем, что сделал Иисус. 47Первосвященники и фарисеи тогда созвали совет.

– Что нам делать? – спрашивали они. – Этот Человек творит много знамений. 48Если мы позволим Ему продолжать, то все поверят в Него, и тогда римляне придут и уничтожат и наш храм, и наш народ11:48 Высший Совет полагал, что если народ поверит в то, что Иисус – это обещанный Богом Мессия, и возведет Его на царство, то это может вызвать репрессивные меры со стороны Рима..

49Кайафа11:49 Кайафа занимал пост первосвященника с 18 по 36 гг., один из них, который в тот год был первосвященником, сказал:

– Вы ничего не понимаете! 50Вы не можете понять, что лучше для вас, чтобы один человек умер за народ, чем погиб бы весь народ.

51Он сказал это не от себя, но, будучи в тот год первосвященником, он изрек пророчество о том, что Иисус умрет за народ, 52и не только за иудейский народ, но и для того, чтобы собрать воедино рассеянных повсюду детей Божьих.

53С этого дня они стали думать, как убить Иисуса. 54И поэтому Иисус уже не ходил открыто среди иудеев. Он ушел в местность, расположенную недалеко от пустыни, в город Ефрем. Там Он и остался со Своими учениками. 55Приближался иудейский праздник Пасхи, и многие жители страны шли в Иерусалим для обрядового очищения11:55 Ритуально нечистые люди не могли принимать участие в этом праздновании (см. Чис. 9:6). перед Пасхой. 56Они искали Иисуса и, стоя в храме, спрашивали друг друга:

– Как вы думаете? Он, наверняка, не придет на праздник?

57А первосвященники и фарисеи отдали распоряжение о том, что если кто-либо узнает, где находится Иисус, то должен сообщить им, чтобы они могли арестовать Его.