Yohane 10 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 10:1-42

Mʼbusa Wabwino ndi Nkhosa Zake

1“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani inu Afarisi, kuti munthu amene salowera pa khomo mʼkhola la nkhosa, koma amalowera pena pake ndi wakuba ndi wachifwamba. 2Munthu amene amalowera pa khomo ndi mʼbusa wankhosazo. 3Mlonda amamutsekulira khomo, ndipo nkhosa zimamvera mawu ake. Iye amaziyitana mayina nkhosa zakezo, nazitulutsa. 4Akazitulutsa nkhosa zake zonse, iye amazitsogolera, ndipo nkhosa zakezo zimamutsata chifukwa zimadziwa mawu ake. 5Koma nkhosazo sizidzatsatira mlendo. Izo zidzamuthawa chifukwa sizizindikira mawu a mlendo.” 6Yesu ananena mawu ophiphiritsawa, koma Afarisi sanazindikire zimene ankawawuza.

7Choncho Yesu anatinso, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Ine ndine khomo la nkhosa. 8Onse amene anadza ndisanabwere Ine ndi akuba ndi achifwamba, ndipo nkhosa sizinawamvere. 9Ine ndine khomo, aliyense amene alowa kudzera mwa Ine adzapulumuka. Iye adzalowa ndi kutuluka ndi kupeza msipu. 10Mbala sibwera chabe koma kuti idzabe, kupha ndi kuwononga. Ine ndabwera kuti iwo akhale ndi moyo, ndi kukhala nawo wochuluka.

11“Ine ndine Mʼbusa wabwino. Mʼbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake. 12Wantchito ndi mʼbusa amene nkhosazo si zake. Choncho, pamene aona mmbulu ukubwera, iye amazisiya nkhosazo ndi kuthawa. Ndipo mmbulu umagwira nkhosazo ndikuzibalalitsa. 13Munthuyo amathawa chifukwa ndi wantchito ndipo sasamalira chilichonse cha nkhosazo.

14“Ine ndine mʼbusa wabwino. Ine ndimazidziwa nkhosa zanga ndipo nkhosa zangazo zimandidziwa, 15monga momwe Atate amandidziwa Ine, ndiponso Ine kudziwira Atatewo. Ndimapereka moyo wanga chifukwa cha nkhosa. 16Ine ndili ndi nkhosa zina zimene sizili za gulu ili. Ine ndiyenera kuzibweretsanso. Izonso zidzamvera mawu anga, ndipo zidzakhala gulu limodzi ndi mʼbusa mmodzi. 17Nʼchifukwa chake Atate anga amandikonda, popeza Ine ndikupereka moyo wanga kuti ndiwutengenso. 18Palibe amene angawuchotse mwa Ine, koma ndikuwupereka mwakufuna kwanga. Ine ndili ndi ulamuliro wa kuwupereka ndi ulamuliro wakuwutenganso. Lamulo ili ndinalandira kwa Atate anga.”

19Pa mawu awa Ayuda anagawikananso. 20Ambiri a iwo anati, “Iye ndi wogwidwa ndi ziwanda ndi wamisala. Chifukwa chiyani mukumvera Iye?”

21Koma ena anati, “Awa si mawu a munthu wogwidwa ndi ziwanda. Kodi ziwanda zingathe bwanji kutsekula maso a wosaona?”

Kusakhulupirira kwa Ayuda

22Ku Yerusalemu kunali chikondwerero chokumbukira kupatulidwa kwa Nyumba ya Mulungu. Inali nthawi yozizira, 23ndipo Yesu ankayenda mʼbwalo la Nyumbayo ku malo a Solomoni. 24Ayuda anamuzungulira Iye akunena kuti, “Kodi iwe udzazunguza malingaliro athu mpaka liti? Ngati iwe ndi Khristu, tiwuze momveka.”

25Yesu anayankha kuti, “Ine ndimakuwuzani, koma inu simukhulupirira. Ntchito zimene ndikuchita mʼdzina la Atate anga zikundichitira umboni, 26koma inu simukhulupirira chifukwa simuli a gulu lankhosa zanga. 27Nkhosa zanga zimamva mawu anga, Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsata Ine. 28Ine ndimazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongeka. Palibe amene adzazikwatula mʼdzanja langa. 29Atate anga, amene anandipatsa Ine, ndi akulu kuposa onse. Palibe amene angazikwatule mʼdzanja la Atate anga. 30Ine ndi Atate ndife amodzi.”

31Ayuda anatolanso miyala kuti amugende Iye, 32koma Yesu anawawuza kuti, “Ine ndakuonetsani zinthu zambiri zabwino zodabwitsa kuchokera kwa Atate. Nʼchifukwa chiti mwa izi chimene mukundigendera?”

33Ayuda anayankha kuti, “Ife sitikukugenda chifukwa cha izi, koma popeza ukunyoza Mulungu, chifukwa iwe, munthu wamba, ukuti ndiwe Mulungu.”

34Yesu anawayankha kuti, “Kodi sizinalembedwa mʼmalamulo anu kuti, ‘Ine ndanena kuti ndinu milungu?’ 35Ngati anawatcha milungu anthu amene analandira mawu a Mulungu, pajatu Malemba sangasweke, 36nanga bwanji uyu amene Atate anamuyika padera monga wake weniweni ndi kumutuma ku dziko lapansi? Nanga ndi chifukwa chiyani mukundinena Ine kuti ndikuchita chipongwe? Kodi nʼchifukwa choti ndanena kuti, ‘Ine ndine Mwana wa Mulungu?’ 37Musandikhulupirire Ine ngati sindichita ntchito za Atate anga. 38Koma ngati Ine ndikuchita zimenezi, ngakhale kuti simundikhulupirira, khulupirirani ntchito zodabwitsazo, ndipo mudziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndiponso Ine ndili mwa Atate.” 39Iwo anafuna kumugwiranso koma anawapulumuka mʼmanja mwawo.

40Kenaka Yesu anabwereranso kutsidya la mtsinje wa Yorodani kumalo kumene Yohane ankabatiza mʼmasiku akale. Iye anakhala kumeneko 41ndipo anthu ambiri anabwera kwa Iye. Iwo anati, “Ngakhale kuti Yohane sanachite chizindikiro chodabwitsa, zonse zimene Yohane ananena za munthu uyu zinali zoona.” 42Ndipo pamalo amenewo ambiri anakhulupirira Yesu.

New Russian Translation

Иоанна 10:1-42

Иисус – хороший пастух

1– Говорю вам истину: тот, кто входит в овечий загон не через ворота, а проникает другим путем, тот вор и разбойник. 2Но кто входит через ворота, тот настоящий пастух10:2 Политических и духовных вождей Израиля иногда называли «пастухами», от них требовалось заботиться о своем «стаде», т. е. народе. Но когда они стали угнетать «стадо», Бог обличил их (см. Иез. 34; Ис. 56:9-12) и обещал послать хорошего Пастуха, Христа (см. Иез. 34:23). Данную притчу нужно понимать в свете этого исторического контекста. этих овец. 3Сторож открывает ему ворота, и овцы слышат его голос. Он зовет своих овец по именам10:3 По всей вероятности, во времена Иисуса пастухи в Израиле любили давать овцам имена (клички). и выводит их. 4Когда он выведет всех своих, то идет впереди них, и овцы идут за ним, потому что знают его голос. 5Они никогда не пойдут за чужим, они убегут от него, потому что не знают его голоса.

6Иисус использовал эту притчу, но они не поняли, о чем Он говорил.

7Тогда Иисус сказал:

– Говорю вам истину: Я – дверь для овец. 8Все, кто приходили до Меня, – воры и разбойники, и овцы их не послушали10:8 Здесь имеются в виду те, кто входил в «овечий загон» не через «ворота» (см. 10:1) – политические и духовные вожди Иудеи, которые думали лишь о своем благе.. 9Я – дверь: кто входит через Меня, тот будет спасен. Он сможет входить и выходить и найдет пастбище. 10Вор приходит только для того, чтобы украсть, убить и разрушить, а Я пришел, чтобы дать жизнь, и притом в избытке.

11Я – хороший пастух. Хороший пастух отдает жизнь свою за овец. 12Наемному пастуху овцы не принадлежат, и, когда он видит, что пришел волк, он бросает овец и убегает. Тогда волк хватает овец и разгоняет все стадо. 13Наемник убегает, потому что он нанят и не заботится об овцах.

14Я – хороший пастух. Я знаю Своих, и они знают Меня. 15Так же и Отец знает Меня, и Я знаю Отца. Я отдаю жизнь Мою за овец. 16У Меня есть и другие овцы, не из этого загона10:16 Имеются в виду представители других народов, не иудеи, которые поверят в Иисуса., их Я тоже должен привести. Они тоже будут послушны Моему голосу, и будет одно стадо и один пастух. 17Отец любит Меня потому, что Я отдаю Свою жизнь, чтобы потом опять взять ее. 18Никто ее у Меня не может отнять, Я отдаю ее добровольно. У Меня есть власть отдать ее и взять ее опять. Так было Мне определено Моим Отцом.

19После этих слов мнения слушавших иудеев опять разделились. 20Многие говорили:

– Он одержимый и бредит, зачем Его слушать?

21Другие говорили:

– Одержимый так бы не говорил. Разве может демон открывать глаза слепым?

Религиозные вожди расспрашивают Иисуса в храме

22В Иерусалиме наступил праздник Обновления10:22 Праздник Обновления храма – праздновался в память об очищении храма Маккавеями в 165 г. до н. э., после его осквернения Антиохом Епифаном. храма. Была зима. 23Иисус ходил по храму в колоннаде Соломона. 24Вокруг Него собрался народ.

– Сколько Ты еще будешь держать нас в недоумении? – говорили они. – Если Ты Христос, то так и скажи нам.

25Иисус ответил:

– Я уже говорил вам, но вы не поверили. Обо Мне свидетельствуют дела, которые Я совершаю от имени Моего Отца. 26Вы же не верите Мне потому, что вы не из Моих овец. 27Мои овцы слышат Мой голос, Я знаю их, и они идут за Мной. 28Я даю им жизнь вечную, и они никогда не погибнут10:28 Не погибнут – т. е. не попадут в ад., их у Меня никто не отнимет. 29Отец Мой, Который дал их Мне, превыше всех, и никто не может забрать их из рук Моего Отца. 30Я и Отец – одно.

31Тогда иудеи опять схватили камни, чтобы побить Его, 32но Иисус сказал им:

– Я показал вам много добрых дел от Отца. За какое из них вы хотите побить Меня камнями?

33Иудеи ответили:

– Мы Тебя не за это хотим побить камнями, а за кощунство, потому что Ты, человек, выдаешь Себя за Бога.

34Иисус ответил:

– Разве в вашем Законе не написано: «Я сказал: вы – боги»?10:34 Пс. 81:6. В этом отрывке из Псалтыри, по мнению различных толкователей, словом «боги» (евр. «элохим») названы либо судьи, поставленные Богом решать земные дела, либо народ Израиля, либо ангелы. Дело в том, что еврейское слово «элохим» имеет более широкое значение, чем в русском языке слово «бог». И, конечно же, здесь не подразумевалось, что у тех, кто назван «богами», была божественная природа. 35Если богами названы те, кому было дано слово Божье, а Писание не может быть упразднено, 36то как же вы смеете говорить, что Тот, Кого Бог освятил и послал в мир, кощунствует, потому что Я сказал: «Я – Сын Бога»? 37Если Я не делаю то же, что делает Мой Отец, – не верьте Мне. 38Если же Я совершаю дела Моего Отца, то даже если вы не верите Моим словам, верьте делам, чтобы вы поняли и знали, что Отец во Мне и Я в Нем.

39Они опять попытались схватить Его, но Он ушел у них из рук.

40Затем Иисус отправился на другую сторону Иордана, туда, где Иоанн раньше крестил, и там оставался. 41Туда к Нему приходило много людей.

– Хотя Иоанн и не творил ни одного знамения, но все, что Иоанн говорил о Нем, верно, – говорили они.

42И многие там поверили в Иисуса.