Yohane 10 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yohane 10:1-42

Mʼbusa Wabwino ndi Nkhosa Zake

1“Zoonadi, Ine ndikukuwuzani inu Afarisi, kuti munthu amene salowera pa khomo mʼkhola la nkhosa, koma amalowera pena pake ndi wakuba ndi wachifwamba. 2Munthu amene amalowera pa khomo ndi mʼbusa wankhosazo. 3Mlonda amamutsekulira khomo, ndipo nkhosa zimamvera mawu ake. Iye amaziyitana mayina nkhosa zakezo, nazitulutsa. 4Akazitulutsa nkhosa zake zonse, iye amazitsogolera, ndipo nkhosa zakezo zimamutsata chifukwa zimadziwa mawu ake. 5Koma nkhosazo sizidzatsatira mlendo. Izo zidzamuthawa chifukwa sizizindikira mawu a mlendo.” 6Yesu ananena mawu ophiphiritsawa, koma Afarisi sanazindikire zimene ankawawuza.

7Choncho Yesu anatinso, “Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti Ine ndine khomo la nkhosa. 8Onse amene anadza ndisanabwere Ine ndi akuba ndi achifwamba, ndipo nkhosa sizinawamvere. 9Ine ndine khomo, aliyense amene alowa kudzera mwa Ine adzapulumuka. Iye adzalowa ndi kutuluka ndi kupeza msipu. 10Mbala sibwera chabe koma kuti idzabe, kupha ndi kuwononga. Ine ndabwera kuti iwo akhale ndi moyo, ndi kukhala nawo wochuluka.

11“Ine ndine Mʼbusa wabwino. Mʼbusa wabwino amataya moyo wake chifukwa cha nkhosa zake. 12Wantchito ndi mʼbusa amene nkhosazo si zake. Choncho, pamene aona mmbulu ukubwera, iye amazisiya nkhosazo ndi kuthawa. Ndipo mmbulu umagwira nkhosazo ndikuzibalalitsa. 13Munthuyo amathawa chifukwa ndi wantchito ndipo sasamalira chilichonse cha nkhosazo.

14“Ine ndine mʼbusa wabwino. Ine ndimazidziwa nkhosa zanga ndipo nkhosa zangazo zimandidziwa, 15monga momwe Atate amandidziwa Ine, ndiponso Ine kudziwira Atatewo. Ndimapereka moyo wanga chifukwa cha nkhosa. 16Ine ndili ndi nkhosa zina zimene sizili za gulu ili. Ine ndiyenera kuzibweretsanso. Izonso zidzamvera mawu anga, ndipo zidzakhala gulu limodzi ndi mʼbusa mmodzi. 17Nʼchifukwa chake Atate anga amandikonda, popeza Ine ndikupereka moyo wanga kuti ndiwutengenso. 18Palibe amene angawuchotse mwa Ine, koma ndikuwupereka mwakufuna kwanga. Ine ndili ndi ulamuliro wa kuwupereka ndi ulamuliro wakuwutenganso. Lamulo ili ndinalandira kwa Atate anga.”

19Pa mawu awa Ayuda anagawikananso. 20Ambiri a iwo anati, “Iye ndi wogwidwa ndi ziwanda ndi wamisala. Chifukwa chiyani mukumvera Iye?”

21Koma ena anati, “Awa si mawu a munthu wogwidwa ndi ziwanda. Kodi ziwanda zingathe bwanji kutsekula maso a wosaona?”

Kusakhulupirira kwa Ayuda

22Ku Yerusalemu kunali chikondwerero chokumbukira kupatulidwa kwa Nyumba ya Mulungu. Inali nthawi yozizira, 23ndipo Yesu ankayenda mʼbwalo la Nyumbayo ku malo a Solomoni. 24Ayuda anamuzungulira Iye akunena kuti, “Kodi iwe udzazunguza malingaliro athu mpaka liti? Ngati iwe ndi Khristu, tiwuze momveka.”

25Yesu anayankha kuti, “Ine ndimakuwuzani, koma inu simukhulupirira. Ntchito zimene ndikuchita mʼdzina la Atate anga zikundichitira umboni, 26koma inu simukhulupirira chifukwa simuli a gulu lankhosa zanga. 27Nkhosa zanga zimamva mawu anga, Ine ndimazidziwa, ndipo zimanditsata Ine. 28Ine ndimazipatsa moyo wosatha ndipo sizidzawonongeka. Palibe amene adzazikwatula mʼdzanja langa. 29Atate anga, amene anandipatsa Ine, ndi akulu kuposa onse. Palibe amene angazikwatule mʼdzanja la Atate anga. 30Ine ndi Atate ndife amodzi.”

31Ayuda anatolanso miyala kuti amugende Iye, 32koma Yesu anawawuza kuti, “Ine ndakuonetsani zinthu zambiri zabwino zodabwitsa kuchokera kwa Atate. Nʼchifukwa chiti mwa izi chimene mukundigendera?”

33Ayuda anayankha kuti, “Ife sitikukugenda chifukwa cha izi, koma popeza ukunyoza Mulungu, chifukwa iwe, munthu wamba, ukuti ndiwe Mulungu.”

34Yesu anawayankha kuti, “Kodi sizinalembedwa mʼmalamulo anu kuti, ‘Ine ndanena kuti ndinu milungu?’ 35Ngati anawatcha milungu anthu amene analandira mawu a Mulungu, pajatu Malemba sangasweke, 36nanga bwanji uyu amene Atate anamuyika padera monga wake weniweni ndi kumutuma ku dziko lapansi? Nanga ndi chifukwa chiyani mukundinena Ine kuti ndikuchita chipongwe? Kodi nʼchifukwa choti ndanena kuti, ‘Ine ndine Mwana wa Mulungu?’ 37Musandikhulupirire Ine ngati sindichita ntchito za Atate anga. 38Koma ngati Ine ndikuchita zimenezi, ngakhale kuti simundikhulupirira, khulupirirani ntchito zodabwitsazo, ndipo mudziwe ndi kuzindikira kuti Atate ali mwa Ine, ndiponso Ine ndili mwa Atate.” 39Iwo anafuna kumugwiranso koma anawapulumuka mʼmanja mwawo.

40Kenaka Yesu anabwereranso kutsidya la mtsinje wa Yorodani kumalo kumene Yohane ankabatiza mʼmasiku akale. Iye anakhala kumeneko 41ndipo anthu ambiri anabwera kwa Iye. Iwo anati, “Ngakhale kuti Yohane sanachite chizindikiro chodabwitsa, zonse zimene Yohane ananena za munthu uyu zinali zoona.” 42Ndipo pamalo amenewo ambiri anakhulupirira Yesu.

Священное Писание

Иохан 10:1-42

Иса Масих – хороший пастух10:1-21 Политических и духовных вождей Исраила иногда называли «пастухами», от них требовалось заботиться о своём «стаде», т. е. народе. Но когда они стали угнетать «стадо», Всевышний обличил их (см. Езек. 34; Ис. 56:9-12) и обещал послать хорошего Пастуха, Масиха (см. Езек. 34:23). Данную притчу нужно понимать в свете этого исторического контекста.

1– Говорю вам истину: тот, кто входит в овечий загон не через ворота, а проникает другим путём, тот вор и разбойник. 2Но кто входит через ворота, тот настоящий пастух этих овец. 3Сторож открывает ему ворота, и овцы слышат его голос. Он зовёт своих овец по именам10:3 По всей вероятности, во времена Исы пастухи в Палестине любили давать овцам клички. и выводит их. 4Когда он выведет всех своих, то идёт впереди них, и овцы идут за ним10:4 В Палестине пастухи и до сегодняшнего дня пасут своих овец, идя впереди стада., потому что знают его голос. 5Они никогда не пойдут за чужим, они убегут от него, потому что не знают его голоса.

6Иса использовал эту притчу, но они не поняли, о чём Он говорил.

7Тогда Иса сказал:

– Говорю вам истину: Я – дверь для овец. 8Все, кто приходили до Меня, – воры и разбойники, и овцы их не послушали. 9Я – дверь; кто входит через Меня, тот будет спасён. Он сможет входить и выходить, и найдёт пастбище. 10Вор приходит только для того, чтобы украсть, убить и разрушить, а Я пришёл, чтобы дать жизнь, и притом в избытке.

11Я – хороший пастух. Хороший пастух отдаёт жизнь свою за овец. 12Наёмному пастуху овцы не принадлежат, и, когда он видит, что пришёл волк, он бросает овец и убегает. Тогда волк хватает овец и разгоняет всё стадо. 13Наёмник убегает, потому что он нанят и не заботится об овцах.

14Я – хороший пастух. Я знаю Своих, и они знают Меня, 15подобно тому, как Отец знает Меня, и Я знаю Отца. Я отдаю жизнь Мою за овец. 16У Меня есть и другие овцы, не из этого загона10:16 Имеются в виду представители других народов, не иудеи, которые поверят в Ису Масиха., их Я тоже должен привести. Они тоже будут послушны Моему голосу, и будет одно стадо и один пастух. 17Отец потому любит Меня, что Я отдаю Свою жизнь, чтобы потом опять взять её. 18Никто её у Меня не может отнять, Я отдаю её добровольно. У Меня есть власть отдать её и взять её опять. Так было Мне определено Моим Отцом.

19После этих слов мнения слушавших иудеев опять разделились. 20Многие говорили:

– Он одержимый и бредит, зачем Его слушать?

21Другие говорили:

– Одержимый так бы не говорил. Разве может демон открывать глаза слепым?

Религиозные вожди расспрашивают Ису Масиха в храме

22В Иерусалиме наступил праздник Очищения храма10:22 Праздник Очищения храма – этот праздник отмечался в память об освящении храма Маккавеями в 165 г. до н. э., после его осквернения Антиохом Епифаном.. Была зима. 23Иса ходил по храму, в колоннаде Сулеймана. 24Вокруг Него собрался народ.

– Сколько Ты ещё будешь держать нас в недоумении? – говорили они. – Если Ты обещанный Масих, то так и скажи нам.

25Иса ответил:

– Я уже говорил вам, но вы не поверили. Обо Мне свидетельствуют дела, которые Я совершаю от имени Моего Отца. 26Вы же не верите Мне потому, что вы не из Моих овец. 27Мои овцы слышат Мой голос, Я знаю их, и они идут за Мной. 28Я даю им жизнь вечную, и они никогда не погибнут10:28 То есть не попадут в ад., их у Меня никто не отнимет. 29Отец Мой, который дал их Мне, превыше всех10:29 Или: «То, что даровал мне Отец Мой, больше всего остального»., и никто не может забрать их из рук Моего Отца. 30Я и Отец – одно.

31Тогда люди опять схватили камни, чтобы побить Его, 32но Иса сказал им:

– Я показал вам много добрых дел от Отца. За какое из них вы хотите побить Меня камнями?

33Они ответили:

– Мы Тебя не за это хотим побить камнями, а за оскорбление Всевышнего, потому что Ты, будучи обыкновенным человеком, выдаёшь Себя за Всевышнего.

34Иса ответил:

– Разве в Писании вашем не написано: «Я сказал: вы – боги»?10:34 Заб. 81:6. В этом отрывке из Забура словом «боги» (евр. элохим) названы не божественные существа, а судьи Исраила, как представители Самого Всевышнего, поставленные Им решать земные дела. Дело в том, что еврейское слово «элохим» имеет более широкое значение, чем в русском языке слово «бог». 35Если богами названы те, кому было доверено слово Всевышнего (а Писание не может быть упразднено), 36то как же вы смеете говорить, что Я, Тот, Кого Сам Отец приготовил для святой цели и послал в мир, оскорбляю Всевышнего, говоря: «Я – Сын Всевышнего»? 37Если Я не делаю то же, что делает Мой Отец, – не верьте Мне. 38Если же Я совершаю дела Моего Отца, то даже если вы не верите Моим словам, верьте делам, чтобы вы поняли и знали, что Отец во Мне и Я в Нём.

39Они опять попытались схватить Его, но Иса ускользнул из их рук.

40Затем Иса отправился на другую сторону Иордана, туда, где раньше Яхия совершал над народом обряд погружения в воду10:40 Или: «обряд омовения»., и там оставался. 41Туда к Нему приходило много людей.

– Хотя Яхия и не творил знамений, но всё, что Яхия говорил об Этом Человеке, верно, – говорили они.

42И многие там поверили в Ису.