Yobu 9 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 9:1-35

Mawu a Yobu

1Ndipo Yobu anayankha kuti,

2“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona.

Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?

3Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye,

Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.

4Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka.

Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?

5Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa,

ndipo amawagubuduza ali wokwiya.

6Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake

ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.

7Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala;

Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.

8Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba

ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.

9Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana,

nsangwe ndi kumpotosimpita.

10Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,

zodabwitsa zimene sizingawerengeke.

11Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona;

akadutsa, sindingathe kumuzindikira.

12Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa?

Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’

13Mulungu sabweza mkwiyo wake;

ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.

14“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji?

Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?

15Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe;

ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.

16Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera,

sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.

17Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho,

ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.

18Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso

koma akanandichulukitsira zowawa.

19Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi!

Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?

20Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa;

ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.

21“Ngakhale ine ndili wosalakwa,

sindidziyenereza ndekha;

moyo wanga ndimawupeputsa.

22Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti,

‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’

23Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi,

Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.

24Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa

Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo.

Ngati si Iyeyo, nanga ndani?

25“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro;

masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.

26Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja,

ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.

27Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga,

ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’

28ndikuopabe mavuto anga onse,

popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.

29Popeza ndapezeka kale wolakwa

ndivutikirenji popanda phindu?

30Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri

ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,

31mutha kundiponyabe pa dzala,

kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.

32“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha,

sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.

33Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu,

kuti atibweretse ife tonse pamodzi,

34munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine

kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!

35Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo,

koma monga zililimu, sindingathe.

Ketab El Hayat

أيوب 9:1-35

أيوب

1فَقَالَ أَيُّوبُ: 2«قَدْ عَلِمْتُ يَقِيناً أَنَّ الأَمْرَ كَذَلِكَ، وَلَكِنْ كَيْفَ يَتَبَرَّرُ الإِنْسَانُ أَمَامَ اللهِ؟ 3إِنْ شَاءَ الْمَرْءُ أَنْ يَتَحَاجَّ مَعَهُ، فَإِنَّهُ يَعْجِزُ عَنِ الإِجَابَةِ عَنْ حُجَّةٍ مِنْ أَلْفٍ. 4هُوَ حَكِيمُ الْقَلْبِ وَعَظِيمُ الْقُوَّةِ، فَمَنْ تَصَلَّبَ أَمَامَهُ وَسَلِمَ؟ 5هُوَ الَّذِي يُزَحْزِحُ الْجِبَالَ، فَلا تَدْرِي حِينَ يَقْلِبُهَا فِي غَضَبِهِ. 6هُوَ الَّذِي يُزَعْزِعُ الأَرْضَ مِنْ مُسْتَقَرِّهَا فَتَتَزَلْزَلُ أَعْمِدَتُهَا. 7هُوَ الَّذِي يُصْدِرُ أَمْرَهُ إِلَى الشَّمْسِ فَلا تُشْرِقُ، وَيَخْتِمُ عَلَى النُّجُومِ. 8يَبْسُطُ وَحْدَهُ السَّمَاوَاتِ، وَيَمْشِي عَلَى أَعَالِي الْبَحْرِ. 9هُوَ الَّذِي صَنَعَ النَّعْشَ وَالْجَبَّارَ وَالثُّرَيَّا وَمَخَادِعَ الْجَنُوبِ، 10صَانِعُ عَظَائِمَ لَا تُسْتَقْصَى وَعَجَائِبَ لَا تُحْصَى.

11اللهُ يَمُرُّ بِي فَلا أَرَاهُ وَيَجْتَازُ فَلا أَشْعُرُ بِهِ. 12إِذَا خَطَفَ مَنْ يَرُدُّهُ، أَوْ يَقُولُ لَهُ: مَاذَا تَفْعَلُ؟

13لَا يَرُدُّ اللهُ غَضَبَهُ؛ تَخْضَعُ لَهُ كِبْرِيَاءُ الأَشْرَار 14فَكَيْفَ إِذاً يُمْكِنُنِي أَنْ أُجِيبَهُ، وَأَتَخَيَّرَ كَلِمَاتِي فِي مُخَاطَبَتِهِ؟ 15لأَنِّي عَلَى الرَّغْمِ مِنْ بَرَاءَتِي لَا أَقْدِرُ أَنْ أُجِيبَهُ، إِنَّمَا أَسْتَرْحِمُ دَيَّانِي. 16حَتَّى لَوْ دَعَوْتُ وَاسْتَجَابَ لِي، فَإِنِّي لَا أُصَدِّقُ أَنَّهُ قَدِ اسْتَمَعَ لِي. 17يَسْحَقُنِي بِالْعَاصِفَةِ وَيُكْثِرُ جُرُوحِي مِنْ غَيْرِ سَبَبٍ. 18لَا يَدَعُنِي أَلْتَقِطُ أَنْفَاسِي بَلْ يُشْبِعُنِي مَرَائِرَ. 19إِنْ كَانَتِ الْقَضِيَّةُ قَضِيَّةَ قُوَّةٍ، فَهُوَ يَقُولُ مُتَحَدِّياً: هَأَنَذَا. وَإِنْ كَانَتِ الْقَضِيَّةُ قَضِيَّةَ الْقَضَاءِ، فَمَنْ يُحَاكِمُهُ؟ 20إِنْ ظَنَنْتُ نَفْسِي بَرِيئاً، فَإِنَّ فَمِي يَحْكُمُ عَلَيَّ، وَإِنْ كُنْتُ كَامِلاً، فَإِنَّهُ يُجَرِّمُنِي.

21أَنَا كَامِلٌ، لِذَا لَا أُبَالِي بِنَفْسِي، أَمَّا حَيَاتِي فَقَدْ كَرِهْتُهَا. 22وَلَكِنَّ الأَمْرَ سِيَّانِ، لِذَلِكَ قُلْتُ: إِنَّهُ يُفْنِي الْكَامِلَ والشِّرِّيرَ عَلَى حَدٍّ سَواءٍ! 23عِنْدَمَا تُؤَدِّي ضَرَبَاتُ السَّوْطِ إِلَى الْمَوْتِ الْمُفَاجِئِ يَسْخَرُ مِنْ بُؤْسِ الأَبْرِيَاءِ 24فَقَدْ عَهِدَ بِالأَرْضِ إِلَى يَدِ الشِّرِّيرِ، وَأَعْمَى عُيُونَ قُضَاتِهَا. إِنْ لَمْ يَكُنْ هُوَ الْفَاعِلُ، إِذاً مَنْ هُوَ؟

25أَيَّامِي أَسْرَعُ مِنْ عَدَّاءٍ، تَفِرُّ مِنْ غَيْرِ أَنْ تُصِيبَ خَيْراً 26تَمُرُّ كَسُفُنِ الْبَرْدِيِّ، وَكَنَسْرٍ يَنْقَضُّ عَلَى صَيْدِهِ. 27إِنْ قُلْتُ: أَنْسَى ضِيقَتِي، وَأُطْلِقُ أَسَارِيرِي، وَأَبْتَسِمُ وَأُبْدِي بِشْراً، 28فَإِنِّي أَظَلُّ أَخْشَى أَوْجَاعِي، عَالِماً أَنَّكَ لَنْ تُبْرِئَنِي. 29أَنَا مُسْتَذْنَبٌ، فَلِمَاذَا أُجَاهِدُ عَبَثاً؟ 30وَحَتَّى لَوِ اغْتَسَلْتُ بِالثَّلْجِ وَنَظَّفْتُ يَدَيَّ بِالْمُنَظِّفَاتِ، 31فَإِنَّكَ تَطْرَحُنِي فِي مُسْتَنْقَعٍ نَتِنٍ حَتَّى تَكْرَهَنِي ثِيَابِي 32لأَنَّهُ لَيْسَ إِنْسَاناً مِثْلِي فَأُجَاوِبَهُ، وَنَمْثُلَ مَعاً لِلْمُحَاكَمَةِ. 33وَلَيْسَ مِنْ حَكَمٍ بَيْنَنَا يَضَعُ يَدَهُ عَلَى كِلَيْنَا. 34لِيَكُفَّ عَنِّي عَصَاهُ فَلا يُرَوِّعَنِي رُعْبُهُ، 35عِنْدَئِذٍ أَتَكَلَّمُ مِنْ غَيْرِ أَنْ أَخْشَاهُ، لأَنَّ نَفْسِي بَرِيئَةٌ مِمَّا أُتَّهَمُ بِهِ.