Yobu 9 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 9:1-35

Mawu a Yobu

1Ndipo Yobu anayankha kuti,

2“Zoonadi, ndikudziwa kuti zimenezi ndi zoona.

Koma munthu angathe bwanji kukhala wolungama pamaso pa Mulungu?

3Ngakhale wina atafuna kutsutsana naye,

Iye sangamuyankhe munthuyo ngakhale mawu amodzi omwe.

4Mulungu ndi wa nzeru zambiri ndipo mphamvu zake ndi zochuluka.

Ndani analimbana naye popanda kupwetekeka?

5Iye amasuntha mapiri, mapiriwo osadziwa,

ndipo amawagubuduza ali wokwiya.

6Iye amagwedeza dziko lapansi kulisuntha pamalo pake

ndipo amanjenjemeretsa mizati yake.

7Iye amayankhula ndi dzuwa ndipo siliwala;

Iyeyo amaphimba kuwala kwa nyenyezi.

8Ndi Mulungu yekha amene anayala mayiko akumwamba

ndipo amayenda pa mafunde a pa nyanja.

9Iye ndiye mlengi wa nyenyezi zamlalangʼamba ndi akamwiniatsatana,

nsangwe ndi kumpotosimpita.

10Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,

zodabwitsa zimene sizingawerengeke.

11Akapita pafupi ndi ine sindingathe kumuona;

akadutsa, sindingathe kumuzindikira.

12Ngati Iye alanda zinthu, ndani angathe kumuletsa?

Ndani anganene kwa Iye kuti, ‘Mukuchita chiyani?’

13Mulungu sabweza mkwiyo wake;

ngakhale gulu lankhondo la Rahabe linawerama pa mapazi ake.

14“Nanga ine ndingathe kukangana naye bwanji?

Ndingawapeze kuti mawu oti nʼkutsutsana naye?

15Ngakhale nditakhala wosalakwa, sindingamuyankhe;

ndikanangopempha chifundo kwa woweruza wanga.

16Ngakhale ndikanamuyitana ndipo Iye ndi kuvomera,

sindikhulupirira kuti akanamva mawu angawo.

17Iye akanandikantha ndi mphepo yamkuntho,

ndipo akanandipweteka popanda chifukwa.

18Mulungu sakanandilola kuti ndipumenso

koma akanandichulukitsira zowawa.

19Tikanena za mphamvu, Iye ndi wamphamvudi!

Ndipo tikanena za chiweruzo cholungama, ndani angamuzenge mlandu?

20Ngakhale ndikanakhala wosalakwa, zoyankhula zanga zikananditsutsa;

ndikanakhala wopanda cholakwa, pakamwa panga pakanandipeza wolakwa.

21“Ngakhale ine ndili wosalakwa,

sindidziyenereza ndekha;

moyo wanga ndimawupeputsa.

22Zonse nʼzofanana; nʼchifukwa chake ndikuti,

‘Iye amawononga anthu osalakwa ndi anthu oyipa omwe.’

23Pamene mkwapulo ubweretsa imfa yadzidzidzi,

Iye amaseka tsoka la munthu wosalakwayo.

24Pamene dziko lagwa mʼmanja mwa anthu oyipa

Iye amawatseka maso anthu oweruza dzikolo.

Ngati si Iyeyo, nanga ndani?

25“Masiku anga ndi othamanga kwambiri kupambana munthu waliwiro;

masikuwo amapita ine osaonapo zabwino.

26Amayenda ngati mabwato a njedza pa nyanja,

ngati mphungu zothamangira nyama zoti zidye.

27Nʼtanena kuti, ‘Ndidzayiwala madandawulo anga,

ndidzasintha nkhope yanga ndipo ndidzasekerera,’

28ndikuopabe mavuto anga onse,

popeza ndikudziwa kuti simudzavomereza kuti ndine wosalakwa.

29Popeza ndapezeka kale wolakwa

ndivutikirenji popanda phindu?

30Ngakhale nditasamba mʼmadzi oyera kwambiri

ndi kusamba mʼmanja mwanga ndi sopo,

31mutha kundiponyabe pa dzala,

kotero kuti ngakhale zovala zanga zomwe zidzandinyansa.

32“Mulungu si munthu ngati ine kuti ndithe kumuyankha,

sindingathe kutsutsana naye mʼbwalo la milandu.

33Pakanapezeka munthu wina kuti akhale mʼkhalapakati wathu,

kuti atibweretse ife tonse pamodzi,

34munthu wina woti achotse ndodo ya Mulungu pa ine

kuti kuopsa kwake kusandichititsenso mantha!

35Pamenepo ine ndikanatha kuyankhula mosamuopa Mulunguyo,

koma monga zililimu, sindingathe.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

約伯記 9:1-35

約伯的回應

1約伯回答說:

2「不錯,我知道你所言不虛,

但人怎能在上帝面前算為義人?

3人若想與祂辯駁,

千次也不能勝一次。

4祂充滿智慧,能力無比,

誰能抗拒祂還可平安無恙?

5祂可猝然挪動群山,

在怒氣中把山翻倒。

6祂震動大地,使其挪位,

以致地的支柱搖撼。

7祂一聲令下,

太陽便不再升起,

眾星也不再發光。

8祂獨自鋪展穹蒼,

步行在海浪之上。

9祂創造了北斗星、參星、昴星及南天的星座。

10祂行的奇事不可測度,

奇蹟不可勝數。

11祂經過我身旁,我卻看不見;

祂從旁邊掠過,我也無法察覺。

12祂若奪取,誰能阻擋?

誰敢問祂,『你做什麽?』

13上帝不會忍怒不發,

海怪9·13 海怪」希伯來文是「拉哈伯」,下同26·12的幫手必屈膝在祂腳前。

14「因此,我怎敢與祂辯駁?

怎敢措辭與祂理論?

15我縱然無辜,也無法申訴,

只能乞求我的審判者施恩。

16即使我呼喚祂的時候,祂回應我,

我仍不相信祂會垂聽我的聲音。

17祂用暴風摧毀我,

無故地使我飽受創傷。

18祂不肯讓我喘息,

祂使我嚐盡苦頭。

19若論力量,祂甚強大;

若上公堂,誰敢傳祂?

20即使我清白無辜,我的口也會認罪;

即使我純全無過,祂也會判我有罪。

21我雖純全無過,也已毫不在乎,

我厭惡我的生命。

22因為,我認為都是一樣,

純全無過的人和惡人都會被祂毀滅。

23災禍突然奪走人命時,

祂嘲笑無辜者的遭遇。

24大地落入惡人手中,

蒙蔽審判官眼睛的不是祂是誰?

25「我的年日比信差還快,

匆匆而過,不見幸福。

26我的歲月疾馳如快船,

快如急降抓食的老鷹。

27即使我說要忘掉怨恨,

拋開愁容,強顏歡笑,

28諸多的患難仍使我懼怕,

我知道祂9·28 」希伯來文是「你」,下同31節。不承認我無辜。

29既然我被定為有罪,

又何必徒然掙扎?

30即使我用雪水淨身,

用鹼水洗手,

31祂仍會把我扔進污坑,

連我的衣服也嫌棄我。

32祂並非我的同類,

我無法與祂爭辯,一起對簿公堂。

33我倆中間沒有仲裁者,

無人為我們斷定是非9·33 為我們斷定是非」希伯來文是「把手按在我們身上」。

34若能拿開祂責打我的刑杖,

使我不再受祂的驚嚇,

35我就會放膽發言,不必對祂心存恐懼,

但現在我卻不能這樣9·35 但現在我卻不能這樣」或譯「因為我知道自己的清白」。