Yobu 7 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 7:1-21

1“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi?

Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?

2Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo,

kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,

3choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe,

ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.

4Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’

Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.

5Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera,

khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.

6“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu,

ndipo amatha wopanda chiyembekezo.

7Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya;

sindidzaonanso masiku achisangalalo.

8Amene akundiona tsopano akundiona;

mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.

9Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka,

momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera.

10Iye sadzabweranso ku nyumba kwake

ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.

11“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete;

ndidzayankhula mopsinjika mtima,

ndidzadandaula mowawidwa mtima.

12Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja

kuti inu mundiyikire alonda?

13Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga

ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,

14ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto

ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,

15kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa,

kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.

16Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse.

Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.

17“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere,

kuti muzisamala zochita zake,

18kuti muzimusanthula mmawa uliwonse

ndi kumamuyesa nthawi yonse?

19Kodi simudzaleka kumandizonda

kuti ndipezeko mpata wopumula?

20Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu,

Inu wopenyetsetsa anthu?

Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu?

Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?

21Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga

ndi kundichotsera machimo anga?

Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda;

mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

Luganda Contemporary Bible

Yobu 7:1-21

17:1 a Yob 14:14; Is 40:2 b Yob 5:7 c Yob 14:6“Ebiseera by’omuntu ku nsi, tebyagerebwa?

Ennaku ze tezaagerebwa nga ez’omupakasi?

27:2 Lv 19:13Ng’omuddu eyeegomba ekisiikirize okujja,

ng’omupakasi bwe yeesunga empeera ye;

37:3 Yob 16:7; Zab 6:6bwe ntyo bwe nnaweebwa emyezi egy’okubonaabona,

ebiro ebyokutegana bwe byangererwa.

47:4 Ma 28:67Bwe ngalamira neebake, njogera nti, ‘Ndiyimuka ddi, ekiro kinaakoma ddi?’

Nga nzijudde okukulungutana okutuusa obudde lwe bukya.

57:5 Yob 17:14; Is 14:11Omubiri gwange gujjudde envunyu n’ebikakampa,

n’olususu lwange lukutusekutuse era lulabika bubi.

67:6 a Yob 9:25 b Yob 13:15; 17:11, 15“Ennaku zange zidduka okusinga ekyuma ky’omulusi w’engoye bw’atambuza ky’alusisa engoye ze;

era zikoma awatali ssuubi.

77:7 a Zab 78:39; Yak 4:14 b Yob 9:25Ojjukira Ayi Katonda, nti obulamu bwange tebuliimu, wabula mukka bukka,

amaaso gange tegaliddayo kulaba bulungi.

87:8 Yob 20:7, 9, 21Eriiso ly’oyo eryali lindabyeko teririddayo kundaba;

amaaso gammwe galinnoonya, naye nga sikyaliwo.

97:9 a Yob 11:8 b 2Sa 12:23; Yob 30:15Nga ekire bwe kibulawo ne kigenda,

bw’atyo n’aziikwa mu ntaana talivaayo.

107:10 a Yob 27:21, 23 b Yob 8:18Taliddayo mu nnyumba ye,

amaka ge tegaliddayo kumumanya nate.

117:11 a Zab 40:9 b 1Sa 1:10Noolwekyo sijja kuziyiza kamwa kange, nzija kwogera okulumwa kw’omutima gwange;

nzija kwemulugunyiza mu bulumi bw’emmeeme yange.

127:12 Ez 32:2-3Ndi nnyanja oba ndi lukwata ow’omu buziba,

olyoke onkuume?

137:13 Yob 9:27Bwe ndowooza nti, obuliri bwange bunampa ku mirembe,

ekiriri kyange kinakendeeza ku kulumwa kwange;

147:14 Yob 9:34n’olyoka ontiisa n’ebirooto

era n’onkanga okuyita mu kwolesebwa.

157:15 1Bk 19:4Emmeeme yange ne yeegomba okwetuga,

nfe okusinga okuba omulamu.

167:16 Yob 9:21; 10:1Sikyeyagala, neetamiddwa. Sijja kubeera mulamu emirembe gyonna.

Ndeka; kubanga ennaku zange butaliimu.

177:17 Zab 8:4; 144:3; Beb 2:6Omuntu kye ki ggwe okumugulumiza,

n’omulowoozaako?

187:18 Yob 14:3Bw’otyo n’omwekebejja buli makya,

n’omugezesa buli kaseera?

197:19 Yob 9:18Olituusa ddi nga tonvuddeeko

n’ondeka ne mmira ku malusu?

207:20 a Yob 35:6 b Yob 16:12Nyonoonye;

kiki kye nakukola, ggwe omukuumi w’abantu?

Lwaki onfudde nga akabonero ak’obulabe gy’oli,

ne neefuukira omugugu?

217:21 a Yob 10:14 b Yob 10:9; Zab 104:29Era lwaki tosonyiwa kwonoona kwange,

n’oggyawo obutali butuukirivu bwange?

Kubanga kaakano nzija kwebaka mu ntaana;

era ojja kunnoonya ku makya naye naaba sikyaliwo.”