Yobu 7 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 7:1-21

1“Kodi munthu sakhala ndi ntchito yowawa pa dziko lapansi?

Kodi masiku ake sali ngati munthu waganyu?

2Monga ngati kapolo wolakalaka mthunzi wa nthawi yamadzulo,

kapena ngati munthu waganyu woyembekezera malipiro ake,

3choncho ine ndapatsidwa nthawi yongovutika pachabe,

ndiponso usiku wamasautso wapatsidwa kwa ine.

4Ndikamagona ndimaganiza kuti, ‘Kodi kucha liti?’

Usikuwo umatalika ndipo sindigona tulo mpaka mmawa.

5Thupi langa ladzala mphutsi ndi zipsera,

khungu langa langʼambika ndipo likutuluka mafinya.

6“Masiku anga ndi othamanga kupambana makina wolukira nsalu,

ndipo amatha wopanda chiyembekezo.

7Inu Mulungu kumbukirani kuti moyo wanga uli ngati mpweya;

sindidzaonanso masiku achisangalalo.

8Amene akundiona tsopano akundiona;

mudzandifunafuna koma sindidzapezekanso.

9Monga mtambo umazimirira ndi kukanganuka,

momwemonso munthu amene walowa mʼmanda sabwerera.

10Iye sadzabweranso ku nyumba kwake

ndipo onse omudziwa adzamuyiwala.

11“Nʼchifukwa chake ine sindidzakhala chete;

ndidzayankhula mopsinjika mtima,

ndidzadandaula mowawidwa mtima.

12Kodi ine ndine nyanja kapena chirombo chamʼnyanja

kuti inu mundiyikire alonda?

13Pamene ndikuganiza kuti ndidzapeza chitonthozo pa bedi panga

ndipo pogona panga padzachepetsa madandawulo anga,

14ngakhale nthawi imeneyo mumandiopseza ndi maloto

ndi kundichititsa mantha ndi masomphenya,

15kotero kuti ndimalakalaka kudzikhweza kapena kufa,

kupambana kupirira zowawa zimene ndikuzimva mʼthupi mwanga.

16Ine ndatopa nawo moyo wanga; sindingakonde kukhala moyo nthawi zonse.

Ndisiyeni ndekha pakuti moyo wanga ulibe tanthauzo.

17“Kodi munthu nʼchiyani kuti muzimuganizira chotere,

kuti muzisamala zochita zake,

18kuti muzimusanthula mmawa uliwonse

ndi kumamuyesa nthawi yonse?

19Kodi simudzaleka kumandizonda

kuti ndipezeko mpata wopumula?

20Ngati ine ndachimwa, ndachita chiyani kwa Inu,

Inu wopenyetsetsa anthu?

Chifukwa chiyani mwachititsa kuti ndikhale ngati choponyera chandamale chanu?

Kodi ndasanduka katundu wolemera kwa Inu?

21Chifukwa chiyani simukundikhululukira zolakwa zanga

ndi kundichotsera machimo anga?

Pakuti posachedwa ndilowa mʼmanda;

mudzandifunafuna ine koma simudzandionanso.”

Hoffnung für Alle

Hiob 7:1-21

Gott, warum lässt du mich nicht in Ruhe?

1»Das Leben der Menschen gleicht der Zwangsarbeit,

von früh bis spät müssen sie sich abmühen!

2Ein Landarbeiter sehnt sich

nach dem kühlen Schatten am Abend;

er wartet darauf, dass ihm sein Lohn bezahlt wird.

3Und was ist mein Lohn?

Monate, die sinnlos dahinfliegen,

und kummervolle Nächte!

4Wenn ich mich schlafen lege,

denke ich: ›Wann kann ich endlich wieder aufstehen?‹

Die Nacht zieht sich in die Länge,

ich wälze mich schlaflos hin und her bis zum Morgen.

5Mein Körper ist von Würmern

und von dreckigem Schorf bedeckt.

Meine Haut platzt auf und eitert.

6Schneller als ein Weberschiffchen sausen meine Tage dahin,

sie schwinden ohne jede Hoffnung.

7O Gott, bedenke, dass mein Leben nur ein Hauch ist!

Mein Glück ist dahin; es kommt nie wieder.

8Noch siehst du mich, doch nicht mehr lange,

und wenn du mich dann suchst, bin ich nicht mehr da.

9-10Wie eine Wolke, die vorüberzieht,

so ist ein Mensch, der stirbt:

Vom Ort der Toten kehrt er nie zurück;

dort, wo er einmal wohnte, ist er bald vergessen.

11Nein – ich kann nicht schweigen!

Der Schmerz wühlt in meinem Innern.

Ich lasse meinen Worten freien Lauf,

ich rede aus bitterem Herzen.

12O Gott, warum lässt du mich so scharf bewachen?

Bin ich denn das Meer oder ein Meeresungeheuer?

13-14Wenn ich dachte: ›Ich will im Schlaf Ruhe finden

und mein Elend vergessen‹,

dann hast du mich bis in die Träume verfolgt

und mir durch Visionen Angst eingejagt.

15Am liebsten würde ich erhängt!

Lieber sterben als noch länger in diesem elenden Körper leben!

16Ich gebe auf! So will ich nicht mehr weiterleben!

Lass mich in Ruhe, denn mein Leben hat keinen Sinn mehr!

17Gott, warum nimmst du einen Menschen so ernst?

Warum beachtest du ihn überhaupt?

18Jeden Morgen verlangst du Rechenschaft von ihm;

du beobachtest ihn jeden Augenblick.

19Wie lange schaust du mich noch prüfend an?

Du lässt mich keinen Augenblick in Ruhe!7,19 Wörtlich: Du lässt mich nicht einmal so lange in Ruhe, bis ich meinen Speichel heruntergeschluckt habe.

20Du Menschenwächter – hat dich meine Sünde denn verletzt?

Warum machst du mich zu deiner Zielscheibe?

Bin ich dir zur Last geworden?

21Warum vergibst du mir mein Unrecht nicht?

Kannst du keine Sünde übersehen?

Denn bald liege ich unter der Erde,

und wenn du mich dann suchst, bin ich nicht mehr da.«