Yobu 5 – Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero CCL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 5:1-27

1“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe?

Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?

2Mkwiyo umapha chitsiru,

ndipo njiru imawononga wopusa.

3Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu,

koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.

4Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe;

amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.

5Anthu anjala amamudyera zokolola zake,

amamutengera ndi za pa minga pomwe,

ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.

6Pakuti masautso satuluka mʼfumbi,

ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.

7Komatu munthu amabadwira kuti azunzike

monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.

8“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu;

ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.

9Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,

zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.

10Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi,

ndipo amathirira minda ya anthu.

11Iye amakweza anthu wamba,

ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.

12Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera,

kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.

13Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,

ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.

14Mdima umawagwera nthawi yamasana;

nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.

15Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo;

amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.

16Choncho osauka ali ndi chiyembekezo,

ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.

17“Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula;

nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.

18Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo;

Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.

19Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi,

mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.

20Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa,

ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.

21Adzakuteteza kwa anthu osinjirira,

ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.

22Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala,

ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.

23Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako,

ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.

24Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa;

udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.

25Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri,

ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.

26Udzafika ku manda utakalamba,

monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.

27“Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona,

choncho uzimvere ndi kuzitsata.”