Yobu 42 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 42:1-17

Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,

2“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse;

chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.

3Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru?

Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse,

zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.

4“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula;

ndidzakufunsa

ndipo iwe udzandiyankhe.’

5Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga,

koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.

6Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi,

ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”

Mulungu Adalitsa Yobu

7Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu. 8Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.” 9Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.

10Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale. 11Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.

12Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000. 13Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu. 14Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki. 15Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.

16Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi. 17Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.

Hoffnung für Alle

Hiob 42:1-17

Gott wendet Hiobs Schicksal zum Guten

(Kapitel 42)

Hiobs letztes Wort

1Da antwortete Hiob:

2»Herr, ich erkenne, dass du alles zu tun vermagst;

nichts und niemand kann deinen Plan vereiteln.

3Du hast gefragt:

›Wer bist du, dass du meine Weisheit anzweifelst

mit Worten ohne Verstand?‹

Ja, es ist wahr:

Ich habe von Dingen geredet, die ich nicht begreife,

sie sind zu hoch für mich und übersteigen meinen Verstand.

4Du hast gesagt:

›Hör mir zu, jetzt rede ich, ich will dich fragen,

und du sollst mir antworten!‹

5Herr, ich kannte dich nur vom Hörensagen,

jetzt aber habe ich dich mit eigenen Augen gesehen!

6Darum widerrufe ich meine Worte,

ich bereue in Staub und Asche!«

Gott stellt sich hinter Hiob

7Nachdem der Herr dies alles zu Hiob gesagt hatte, wandte er sich an Elifas aus Teman: »Ich bin voller Zorn über dich und deine beiden Freunde, ihr habt nicht die Wahrheit über mich gesagt, so wie mein Diener Hiob es tat! 8Bringt nun sieben junge Stiere und sieben Schafböcke, geht damit zu meinem Diener Hiob und bringt sie als Brandopfer dar! Hiob soll für euch beten, denn nur ihn will ich erhören und euch um seinetwillen nichts Böses tun. Denn ihr habt nicht wie er die Wahrheit über mich gesagt.«

9Da taten Elifas aus Teman, Bildad aus Schuach und Zofar aus Naama, was ihnen der Herr befohlen hatte. Und Gott erhörte Hiobs Gebet.

10Als Hiob für seine Freunde betete, da wendete der Herr für ihn alles zum Guten. Er gab ihm doppelt so viel, wie er früher besessen hatte. 11Alle seine Brüder und Schwestern und die früheren Bekannten besuchten ihn wieder. Sie aßen mit ihm in seinem Haus und trösteten ihn wegen des Unglücks, das der Herr über ihn gebracht hatte. Jeder schenkte ihm ein Silberstück und einen Ring aus Gold.

12Der Herr segnete Hiob von jetzt an mehr als zuvor. Bald besaß er 14.000 Schafe und Ziegen, 6000 Kamele, 1000 Rindergespanne und 1000 Esel. 13Er bekam auch wieder sieben Söhne und drei Töchter. 14Die erste nannte er Jemima (»Täubchen«), die zweite Kezia (»Zimtblüte«) und die dritte Keren-Happuch (»Schminkdöschen«). 15Im ganzen Land gab es keine schöneren Frauen als Hiobs Töchter; sie durften mit ihren Brüdern das Erbe teilen.

16Hiob lebte noch 140 Jahre, er sah Kinder und Enkel bis in die vierte Generation. 17Schließlich starb er in hohem Alter nach einem reichen und erfüllten Leben.