Yobu 40 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 40:1-24

1Yehova anati kwa Yobu:

2“Kodi iwe ufuna kukangana ndi Wamphamvuzonse?

Iwe amene unatsutsana ndi Mulungu umuyankhe Iyeyo!”

3Pamenepo Yobu anayankha Yehova:

4“Ine sindili kanthu konse,

kodi ndingathe kukuyankhani chiyani? Ndagwira pakamwa panga.

5Ndinayankhula kamodzi, koma pano ndilibe yankho,

ndinayankha kawiri, koma sindiwonjezeranso mawu ena.”

6Ndipo Yehova anayankha Yobu mʼkamvuluvulu kuti,

7“Tsopano vala dzilimbe ngati mwamuna;

ndikufunsa mafunso

ndipo iwe undiyankhe.

8“Kodi iwe unganyoze chiweruzo changa cholungama?

Kodi ungandidzudzule kuti iweyo ukhale wolungama?

9Kodi uli ndi dzanja monga la Mulungu,

ndipo mawu ako angagunde ngati mphenzi monga a Mulungu?

10Ngati zili choncho udzikometsere ndi ulemerero ndi kukongola,

ndipo udziveke ulemu ndi ulemerero waufumu.

11Tsanula ukali wako wosefukirawo,

uyangʼane aliyense wodzikuza ndipo umuchepetse,

12Uyangʼane aliyense wodzikweza ndipo umutsitse,

uwapondereze oyipa onse pamalo pomwe alilipo.

13Onsewo uwakwirire pamodzi mfumbi;

ukulunge nkhope zawo mʼmanda.

14Ukatero Ine ndidzakuvomereza

kuti dzanja lako lamanja lakupulumutsadi.

15“Taganiza za mvuwu,

imene ndinayipanga monga momwe ndinapangira iwe,

ndipo imadya udzu ngati ngʼombe.

16Mphamvu zake ndi zazikulu kwambiri,

thupi lake ndi lanyonga kwambiri!

17Mchira wake umayima tolotolo ngati mtengo wamkungudza;

mitsempha ya ntchafu zake ndi yogwirana bwino.

18Mafupa ake ali ngati mapayipi amkuwa,

nthiti zake zili ngati mipiringidzo yachitsulo.

19Mvuwuyo ndi yayikulu mwa zolengedwa za Mulungu,

komatu mlengi wake amatha kuyiopseza ndi lupanga lake.

20Imapeza chakudya chake ku mtunda

ndipo nyama zakuthengo zonse zimasewera pambali pake.

21Imagona pa tsinde pa zitsamba za mipeta,

imabisala mʼbango ndiponso pa thawale.

22Imaphimbika ndi mthunzi wazitsamba za mipeta;

imazunguliridwa ndi misondozi ya mu mtsinje.

23Madzi a mu mtsinje akakokoma, sichita mantha,

iyo sitekeseka, ngakhale madzi a mu Yorodani afike mʼkhosi mwake.

24Kodi alipo amene angathe kukola mvuwu ndi mbedza

kapena kuyikola mu msampha?

New Russian Translation

Иов 40:1-27

1И Господь сказал Иову из бури:

2– Препояшь себя, как мужчина;

Я буду спрашивать, а ты отвечай.

3Опровергнешь ли ты Мой суд?

Обвинишь ли Меня, чтобы себя оправдать?

4Есть ли у тебя мощь, как у Бога,

и гремит ли голос твой, как у Него?

5Что ж, укрась себя славой и величием,

оденься в честь и великолепие.

6Дай волю ярости своего гнева,

посмотри на гордого и смири его,

7посмотри на надменного и унизь его,

придави злодеев к земле.

8Зарой их всех вместе в землю

и окутай их лица тьмой40:8 Букв.: «потайными местами»..

9Тогда и Сам Я тебе скажу,

что твоя правая рука тебя спасла.

10Присмотрись к чудовищу40:10 На языке оригинала: «бехемот». Это слово является множественным числом от бехема («зверь») и означает огромного, удивительного зверя. Никто не может с полной уверенностью сказать, что это за животное.,

Я создал его, как и тебя;

он ест траву, как вол.

11Что за сила в бедрах его,

что за крепость в мускулах живота!

12Машет он своим хвостом, как кедром;

жилы бедер его сплетены.

13Ноги его, как медные трубы,

кости его, как железные прутья.

14Он величайшее среди Божьих дел40:14 Букв.: «путей».;

лишь его Творец может меч к нему поднести.

15Горы пищу ему дают,

где резвятся все дикие звери40:15 Смысл этого места в еврейском тексте неясен..

16В зарослях лотоса он лежит,

скрыт среди тростников болотных.

17Лотосы прячут его в тени,

ивы у ручья его окружают.

18Бушует река – не страшно ему;

невозмутим он,

хоть хлынь ему в пасть Иордан.

19Кто схватит его у него же на глазах?40:19 У него же на глазах – или: «крюком».

Кто багор в его нос проденет?

20Можешь ли вытащить удочкой Левиафана40:20 Левиафан – никто не может с полной уверенностью сказать, что это за животное.

и связать веревкой его язык?

21Проденешь ли канат ему в нос

и пронзишь ли челюсть его крюком?

22Станет ли он тебя умолять

и кротко с тобой говорить?

23Заключит ли он с тобой договор,

что пойдет в услужение к тебе навек?

24Станешь ли с ним, как с птичкой, играть,

привяжешь ли на забаву служанкам?

25Станут ли рыбаки о нем торговаться,

купцы – его тушу делить?

26Пронзишь ли ты кожу его копьем

и рыбацкой острогой – голову?

27Тронь его раз – и больше не станешь;

никогда не забудешь ту битву!