Yobu 39 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 39:1-30

1“Kodi iwe umadziwa nthawi imene mbalale yayikazi imaswera?

Kodi umaonerera pamene nswala ikubala?

2Kodi umawerenga miyezi imene zimakhala ndi bere?

Kodi nthawi imene zimaswana iwe umayidziwa?

3Zimakhala tsonga ndi kuswa ana awo;

pamenepo ululu wobereka nʼkutha.

4Ana a nyamazi amakhala ndi mphamvu ndipo amakulira mʼthengo;

kenaka amachoka ndipo sabwereranso.

5“Kodi bulu wakuthengo amamupatsa ndani ufulu wongodziyendera?

Ndani amamasula zingwe zake?

6Ine ndinamupatsa chipululu kuti chikhale mudzi wake,

nthaka ya mchere kuti ikhale malo ake okhalamo

7Iye amakhala kutali ndi phokoso la mu mzinda;

ndipo samva kufuwula kwa oyendetsa nyama zakatundu.

8Amayendayenda mʼmapiri kudya msipu

ndipo amafunafuna msipu uliwonse wobiriwira.

9“Kodi njati ingavomere kukutumikira?

Kodi ingagone mu gome lako usiku?

10Kodi ungathe kuyimanga ndi zingwe kuti izilima?

Kodi ingasalaze nthumbira mʼmunda mwako?

11Kodi ungadalire njatiyo chifukwa champhamvu zake?

Kodi ungayilekere kuti igwire ntchito zako zolemetsa?

12Kodi ungadalire kuti idzakubweretsera tirigu wako

ndi kumuyika ku malo opunthira?

13“Nthiwatiwa imakupiza mapiko ake monyadira,

koma mapikowo sangafanane ndi mapiko ndi nthenga za kakowa.

14Nthiwatiwa imakwirira mazira ake pansi

ndipo amafundidwa ndi nthaka,

15nthiwatiwayo sidera nkhawa kuti mazira ake angathe kuswanyidwa,

ndi kuti nyama zakuthengo zitha kuwaponda.

16Nthiwatiwa imachitira nkhanza ana ake ngati anawo si ake;

Imayiwala zoti inavutika powabala.

17Chifukwa Mulungu anayimana nzeru,

simvetsa kanthu kalikonse.

18Komatu nthiwatiwa ikadzambatuka ndi kuyamba kuthamanga,

imamusiya kutali kavalo ndi wokwerapo wake.

19“Kodi ndiwe amene umamupatsa mphamvu kavalo

kapena kumuveka chenjerere mʼkhosi mwake?

20Kodi ndiwe amene umalipatsa dzombe ulemerero wolumphira,

ukali wake nʼkumachititsa mantha?

21Iye amalumphalumpha moopseza, kukondwerera mphamvu zake,

ndipo amapita ku nkhondo ndi mphamvu zake zonse.

22Iye sachita mantha, saopa chilichonse;

sabwerera mʼmbuyo akaona lupanga.

23Zida zankhondo zimachita kwichikwichi mʼchimake pambali pake

pamodzi ndi mkondo wonyezimira ndi nthungo.

24Kavaloyo amanjenjemera ndi ukali ndi kulumphalumpha;

satha kungoyima pamene wamva kulira kwa lipenga.

25Lipenga likalira amati, ‘Twee!’

Amamva fungo la nkhondo ali patali,

kufuwula kwa anthu olamulira nkhondo ndi mfuwu wankhondo.

26“Kodi kabawi amawuluka ndi nzeru zako,

ndi kutambasula mapiko ake kupita kummwera?

27Kodi umalamulira chiwombankhanga ndiwe kuti chiziwuluka

ndi kumanga chisa chake pamwamba penipeni?

28Chimakhala pa phiri ndipo chimakhala pamenepo usiku;

chimakhala pa msonga penipeni pa mwala.

29Chili pamenepo chimayangʼanayangʼana choti chigwire kuti chidye;

maso ake amachionera patali chinthucho.

30Ana ake amayamwa magazi,

ndipo kumene kuli mitembo ndiko chimapezeka.”

La Bible du Semeur

Job 39:1-30

1Connais-tu le moment ╵où les chamois enfantent ?

Et as-tu observé ╵les biches en travail ?

2As-tu compté combien de mois ╵dure leur gestation ?

Et connais-tu l’époque ╵où elles mettent bas,

3quand elles s’accroupissent, ╵déposent leurs petits

et sont délivrées des douleurs ?

4Leurs faons se fortifient, ╵grandissant en plein air

et ils s’en vont loin d’elles ╵pour ne plus revenir.

5Qui a laissé l’onagre ╵courir en liberté ?

Qui a rompu les liens ╵qui retenaient l’âne sauvage ?

6Moi je lui ai donné ╵le désert pour demeure

et des plateaux salés39.6 Les terres salées sont opposées aux terres à fruits (Ps 107.34). L’âne sauvage se nourrit des herbes salées croissant dans les steppes d’Arabie et de Syrie. ╵pour résidence.

7Il ne veut rien savoir ╵des villes populeuses,

et il n’entend pas les cris ╵du conducteur de l’âne.

8Il parcourt les montagnes ╵pour trouver sa pâture,

à la recherche de toute verdure.

9L’aurochs39.9 L’urus ou l’aurochs, variété éteinte aujourd’hui, était un animal grand et puissant, souvent pris comme symbole de la force (Nb 23.22 ; 24.8 ; Dt 33.17). daignera-t-il ╵se mettre à ton service ?

Passera-t-il ses nuits ╵auprès de ta mangeoire ?

10Lui feras-tu suivre un sillon ╵en l’attachant avec des cordes ?

Va-t-il traîner la herse ╵derrière toi dans les vallons ?

11Mettras-tu ta confiance ╵dans sa force extraordinaire ?

Et lui remettras-tu ╵le soin de tes travaux ?

12Compteras-tu sur lui ╵pour rapporter ton grain

et l’amasser ╵sur l’aire de battage ?

13Les ailes de l’autruche ╵se déploient avec joie,

mais son aile et ses plumes ╵ne sont pas comparables ╵à celles des cigognes.

14Or l’autruche abandonne ╵ses œufs dans la poussière,

et laisse au sable chaud ╵le soin de les couver,

15ne pensant pas à ceux ╵qui marcheraient dessus,

aux animaux sauvages ╵qui les piétineraient.

16Elle est dure pour ses petits ╵comme s’ils n’étaient pas les siens,

et elle ne s’inquiète pas ╵d’avoir peiné en vain.

17Pourquoi ? Parce que Dieu ╵l’a privée de sagesse,

et qu’il ne lui a pas donné ╵l’intelligence.

18Mais qu’elle se redresse ╵et prenne son élan,

pour elle c’est un jeu ╵de laisser derrière elle ╵cheval et cavalier.

19Serait-ce toi qui donnes ╵la puissance au cheval ?

Ou est-ce toi qui pares ╵son cou d’une crinière ?

20Ou le fais-tu bondir ╵comme la sauterelle ?

Son fier hennissement ╵inspire la frayeur !

21Dans le vallon, il piaffe, ╵tout joyeux de sa force.

Le voilà qui s’élance ╵en plein dans la mêlée.

22Il se rit de la peur ╵et ne s’effraie de rien.

Il ne recule pas ╵en face de l’épée,

23lorsqu’au-dessus de lui ╵cliquette le carquois,

la lance étincelante ╵ou bien le javelot.

24Tout frémissant d’ardeur, ╵il dévore l’espace,

il ne tient plus en place ╵dès qu’il a entendu ╵le son du cor.

25Dès qu’il entend la charge, ╵il hennit : « En avant »,

lorsqu’il est loin encore, ╵il flaire la bataille,

la voix tonitruante ╵des commandants de troupes ╵et les cris des guerriers.

26Serait-ce grâce ╵à ton intelligence ╵que l’épervier prend son essor

et qu’il déploie ses ailes ╵en direction du sud39.26 L’épervier migrateur s’arrête dans cette région au cours de son vol vers le sud au début de l’hiver. ?

27Serait-ce à ton commandement ╵que l’aigle monte dans les airs

et qu’il bâtit son nid ╵sur les sommets ?

28Il fait du rocher sa demeure ╵et y passe la nuit,

il établit sa forteresse ╵sur une dent rocheuse.

29De là-haut, il épie sa proie,

de loin, il l’aperçoit.

30Ses petits s’abreuvent de sang.

Où que soient les cadavres, ╵il est présent39.30 Voir Mt 24.28 ; Lc 17.37..