Yobu 37 – CCL & NTLR

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 37:1-24

1“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso

ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.

2Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,

kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.

3Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse

ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.

4Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.

Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.

Pamene wabangula,

palibe chimene amalephera kuchita.

5Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa

Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.

6Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’

ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’

7Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.

Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.

8Zirombo zimakabisala

ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.

9Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,

kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.

10Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi

ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.

11Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,

amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.

12Mulungu amayendetsa mitamboyo

mozungulirazungulira dziko lonse lapansi

kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.

13Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,

kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.

14“Abambo Yobu, tamvani izi;

imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.

15Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo

ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?

16Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,

ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?

17Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta

pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,

18kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo

limene ndi lolimba ngati chitsulo?

19“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;

sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.

20Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?

Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?

21Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,

ndi kunyezimira mlengalenga,

kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.

22Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;

Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.

23Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;

pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.

24Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,

kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

Nouă Traducere În Limba Română

Iov 37:1-24

1În fața acestor lucruri, inima îmi tremură

și saltă din locul ei.

2Ascultați! Ascultați tunetul glasului Său

și bubuitul care iese din gura Sa!

3Își desfășoară fulgerul sub cerul întreg

și‑l trimite până la marginile pământului.

4Apoi se aude vuietul glasului Său;

El tună cu glasul Său măreț.

Când I se aude glasul,

El nu oprește fulgerele.

5Vocea lui Dumnezeu tună într‑un mod minunat

El face fapte mărețe, iar noi nu cunoaștem totul.

6El spune zăpezii: «Cazi pe pământ!»

și ploii: «Fii o ploaie puternică!»

7El pecetluiește mâna oricărui om,

pentru ca toți oamenii să cunoască lucrarea Lui.

8Atunci vietățile se duc la adăpostul lor

și rămân în vizuinile lor.

9Vijelia iese din odaia sa,

și frigul din vânturile cele năprasnice.

10Suflarea lui Dumnezeu face gheața

și îngheață apele mari.

11El încarcă norii grei cu umezeală;

împrăștie norii cu fulgerul Său.

12Ei se întorc de jur împrejur, după îndrumările Lui,

ca să facă tot ce le poruncește pe fața pământului locuit.

13El îi folosește ca pe o nuia,

sau pentru pământul Său, sau din dragoste13 Vezi nota de la 10:12..

14Iov, ia aminte la aceasta!

Stai și cugetă la minunile lui Dumnezeu!

15Știi tu cum conduce Dumnezeu norii

și cum face să strălucească fulgerul norului Său?

16Știi tu cum plutesc norii?

Înțelegi tu minunile Celui Desăvârșit în cunoaștere,

17tu, ale cărui haine sunt fierbinți,

când pământul tace din cauza vântului de sud?

18Poți tu să întinzi cerurile ca El,

tari ca o oglindă turnată?

19«Fă‑ne cunoscut ce să‑I spunem!

Din cauza întunericului nu ne putem aranja cuvintele.»

20I Se va spune că eu voi vorbi?

Ar vorbi un om doar ca să fie înghițit?

21Acum, ei nu pot privi

cum strălucește soarele în ceruri,

după ce vântul le‑a înseninat.

22Din nord vine aurora22 Lit.: aur;

împrejurul lui Dumnezeu este o splendoare de temut.

23Pe Cel Atotputernic nu‑l putem găsi.

El este măreț în putere,

dar judecata și abundența dreptății

El nu le asuprește.

24De aceea oamenii se tem de El;

El nu Se uită la cei înțelepți în inimă.“