Yobu 35 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 35:1-16

1Ndipo Elihu anawonjeza kunena kuti,

2“Kodi mukuganiza kuti mukukhoza?

Mukunena kuti, ‘Ndine wolungama pamaso pa Mulungu.’

3Komanso inu mukufunsa kuti, ‘Kodi phindu langa nʼchiyani,

ndipo ndimapeza chiyani ndikapanda kuchimwa?’

4“Ine ndikufuna ndikuyankheni inu

pamodzi ndi abwenzi anu omwe.

5Yangʼanani kumwamba ndipo muone

mitambo imene ili kutali ndi inuyo.

6Inuyo mukachimwa, Iye zimamukhudza motani?

Ngati machimo anu ndi ochuluka, zimenezo zimachita chiyani kwa Iye?

7Ngati inu ndinu wolungama, mumamupatsa Iyeyo chiyani?

Kapena Iye amalandira chiyani chochokera mʼdzanja lanu?

8Kuyipa kwanu kumangokhudza anthu ngati inuyo,

ndipo chilungamo chanu chimakhudza anthu anzanu.

9“Anthu akufuwula chifukwa cha kuzunzidwa;

akufuna chithandizo kuti achoke pansi pa ulamuliro wa anthu amphamvu.

10Koma palibe amene akunena kuti, ‘Kodi ali kuti Mulungu, Mlengi wanga,

amene amatisangalatsa nthawi ya usiku,

11amene amatiphunzitsa kupambana nyama za dziko lapansi

ndipo amatipatsa nzeru kupambana mbalame zowuluka?’

12Iye sayankha pamene anthu akufuwulira kwa Iye

chifukwa cha kudzikuza kwa anthu oyipa.

13Ndithu, Mulungu samva kupempha kwawo kopanda pake;

Wamphamvuzonse sasamalira zimenezi.

14Ndipo ndi bodza lalikulu kunena kuti

Iye saona zimene zikuchitika.

Iye adzaweruza molungama ngati

inu mutamudikira

15ndiye tsono popeza kuti ukali wake sukupereka chilango,

zoyipa zambiri zimene anthu amachita,

16abambo Yobu mumangoyankhula zopandapake,

mukungochulukitsa mawu opanda nzeru.”

New International Reader’s Version

Job 35:1-16

1Elihu continued,

2“Job, do you think it’s fair for you to say,

‘I am the one who is right, not God’?

3You ask him, ‘What good is it for me not to sin?

What do I get by not sinning?’

4“I’d like to reply to you

and to your friends who are with you.

5Look up at the heavens.

Observe the clouds that are high above you.

6If you sin, what does that mean to God?

If you sin many times, what does that do to him?

7If you do what is right, how does that help him?

What does he get from you?

8The evil things you do only hurt people like yourself.

The right things you do only help other human beings.

9“People cry out when they are treated badly.

They beg to be set free from the power of those who are over them.

10But no one says, ‘Where is the God who made me?

He gives us songs even during the night.

11He teaches us more than he teaches the wild animals.

He makes us wiser than the birds in the sky.’

12He doesn’t answer sinful people when they cry out to him.

That’s because they are so proud.

13In fact, God doesn’t listen to their empty cries.

The Mighty One doesn’t pay any attention to them.

14So he certainly won’t listen to you.

When you say you don’t see him, he won’t hear you.

He won’t listen when you state your case to him.

He won’t pay attention even if you wait for him.

15When you say his anger never punishes sin, he won’t hear you.

He won’t listen when you say he doesn’t pay any attention to evil.

16So you say things that don’t mean anything.

You use a lot of words,

but you don’t know what you are talking about.”