Yobu 34 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 34:1-37

1Pamenepo Elihu anapitiriza kuyankhula kuti,

2“Imvani mawu anga, inu anthu anzeru;

tcherani khutu inu anthu ophunzira.

3Pakuti khutu limayesa mawu

monga momwe mʼkamwa mumalawira chakudya.

4Tsono tiyeni tizindikire chomwe chili choyenera;

tiphunzire pamodzi chomwe chili chabwino.

5“Yobu akunena kuti, ‘Ndine wosalakwa,

koma Mulungu akukana kundiweruza molungama.

6Ngakhale ndine wolungama mtima,

akundiyesa wabodza;

ngakhale ndine wosachimwa,

mivi yake ikundichititsa mabala osachiritsidwa.’

7Kodi munthu wofanana ndi Yobu ndani,

amene amayankhula zamwano ngati akumwa madzi?

8Iye amayenda ndi anthu ochita zoyipa;

amayanjana ndi anthu oyipa mtima.

9Paja iye amanena kuti, ‘Munthu sapindula kanthu

poyesetsa kukondweretsa Mulungu.’

10“Tsono mverani ine, inu anthu anzeru zomvetsa zinthu.

Mulungu sangachite choyipa ndi pangʼono pomwe,

Wamphamvuzonse sangathe kuchita cholakwa.

11Iye amamubwezera munthu molingana ndi ntchito zake;

Mulungu amabweretsa pa munthu molingana ndi zomwe amachita.

12Nʼchosayembekezeka kuti Mulungu achite cholakwa,

kuti Wamphamvuzonse apotoze chilungamo.

13Kodi anapatsa Mulungu udindo wolamulira dziko lapansi ndani?

Ndani anayika Mulungu kuti azilamulira dziko lonse?

14Mulungu akanakhala ndi maganizo

oti achotse mzimu wake ndi mpweya wake,

15zamoyo zonse zikanawonongekeratu

ndipo munthu akanabwerera ku fumbi.

16“Ngati ndinu omvetsa zinthu, imvani izi;

mvetserani zimene ndikunena.

17Kodi Mulungu wodana ndi chilungamo angathe kukhala wolamulira?

Kodi iwe ungathe kuweruza Wolungama ndi Wamphamvuyo?

18Kodi si Iye amene amanena kwa mafumu kuti, ‘Ndinu opanda pake,’

ndipo amawuza anthu otchuka, ‘Ndinu oyipa,’

19Iye sakondera akalonga

ndipo salemekeza anthu olemera kupambana osauka,

pakuti onsewa ndi ntchito ya manja ake?

20Iwo amafa mwadzidzidzi, pakati pa usiku;

anthu amachita mantha ndipo amamwalira;

munthu wamphamvu amachotsedwa popanda dzanja la munthu.

21“Maso a Mulungu amapenya njira za munthu;

amaona mayendedwe ake onse.

22Palibe malo obisika kapena a mdima wandiweyani

kumene anthu ochita zoyipa angabisaleko.

23Mulungu sasowa kuti apitirizebe kufufuza munthu,

kuti abwere pamaso pake kudzaweruzidwa.

24Popanda kufufuza, Iye amawononga anthu amphamvu

ndipo mʼmalo mwawo amayikamo ena.

25Pakuti Iyeyo amadziwa bwino ntchito zawo

amawagubuduza usiku ndipo amatswanyika.

26Iye amawalanga chifukwa cha kuyipa kwawo,

pamalo pamene aliyense akuwaona;

27Chifukwa anasiya kumutsata

ndipo sasamaliranso njira zake zonse.

28Anachititsa amphawi kuti kulira kwawo kufike pamaso pake,

kotero Iyeyo anamva kulira kwa amphawiwo.

29Koma ngati Mulungu akhala chete, ndani angamunene kuti walakwa?

Akabisa nkhope yake, ndani angathe kumupenyabe?

Komatu ndiye amene amayangʼana za munthu komanso mtundu wa anthu,

30kuti asalamuliridwe ndi anthu osapembedza,

kuti asatchere anthu misampha.

31“Mwina munthu atanena kwa Mulungu kuti,

‘Ndine wolakwa koma sindidzachimwanso,

32ndiphunzitseni zimene sindikuziona

ngati ndachita choyipa, sindidzachitanso.’

33Kodi Mulungu akuweruzeni potsata mmene inuyo mukuganizira,

pamene inu mukukana kulapa?

Chisankho nʼchanu, osati changa;

tsono ndiwuzeni zomwe mukudziwa.

34“Anthu omvetsa zinthu adzakambirana,

anthu anzeru amene akundimva adzandiwuza kuti,

35‘Yobu akuyankhula mopanda nzeru;

mawu ake ndi opanda fundo.’

36Aa, kunali bwino Yobu akanayesedwa mpaka kumapeto

chifukwa choyankha ngati munthu woyipa!

37Pa tchimo lake amawonjezerapo kuwukira;

amawomba mʼmanja mwake monyoza pakati pathu,

ndipo amachulukitsa mawu otsutsana ndi Mulungu.”

New Russian Translation

Иов 34:1-37

Вторая речь Элигу

1Затем Элигу продолжал говорить:

2– Послушайте, мудрые, мою речь.

Внимайте мне, умные люди.

3Ведь ухо разбирает слова,

как язык34:3 Букв.: «небо». – вкус пищи.

4Так давайте решим, где правда,

и рассудим, что есть добро.

Элигу обличает Иова в неправедности

5Иов сказал: «Я невинен,

но лишил меня Бог правосудия.

6И хоть я прав –

меня считают лжецом.

Хоть я без греха,

моя рана от Его стрелы неисцелима».

7Есть ли еще такой человек, как Иов,

кто кощунство, как воду, пьет?

8Он дружит с нечестивыми,

и общается со злодеями.

9Ведь он говорит: «Нет выгоды человеку,

который старается угодить Богу».

Элигу свидетельствует о справедливости Бога

10Потому, имеющие разум, послушайте меня!

Не может быть у Бога неправды,

чужд Всемогущий злу.

11Воздает он смертному по делам

и обходится с ним по его заслугам.

12Воистину, Бог не делает зла,

Всемогущий не извращает суд.

13Кто отдал землю Ему во власть?

Кто поставил Его над вселенной?

14Если бы Он решил забрать Свой дух

и отозвал бы Свое дыхание,

15то погибла бы разом любая плоть,

и возвратился бы смертный во прах.

16Имеешь ты разум, так слушай это;

внимай моей речи.

17Разве правил бы Бог, если бы ненавидел правосудие?

Обвинишь ли ты Справедливого и Могучего,

18Который говорит царю: «Негодяй!» –

и вельможам: «Вы беззаконники!»?

19Он вождям не выказывает пристрастий

и не ставит богатого выше бедного,

ведь все они – творение Его рук.

20Они умирают мгновенно в полночь;

мечутся люди и угасают;

не руки смертных сражают сильных.

21Глаза Его над путями людей;

Он видит каждый их шаг.

22Нет ни мрака, ни тьмы кромешной,

где могли бы спрятаться беззаконники.

23Ведь Богу нет нужды назначать время человеку34:23 Букв.: «Ведь Он еще не назначил человеку».,

чтобы предстать на суд перед Ним.

24Без допроса сокрушает Он сильных

и других на их место ставит.

25Истинно, ведая их дела,

низлагает их ночью – и им конец.

26На глазах у людей

Он карает их за грехи,

27ведь они от Него отступили,

не познали Его путей.

28И дошел до него крик бедных,

Он услышал крик страдальцев.

29Если Он промолчит, кто Его укорит?

Если скроет Он лицо Свое,

кто сможет Его увидеть?

Он над народом и над человеком,

30чтобы не царствовали безбожники,

став сетью для народа.

31Положим, кто-нибудь скажет Богу34:31 Или: «Лучше скажи Богу».:

«Я виновен34:31 Или: «пострадал» – больше не согрешу.

32Научи меня, если что-то не знаю34:32 Букв.: «не вижу».;

если я согрешил, то впредь зарекусь».

33Тогда должен ли Бог тебя удостоить награды,

когда ты отказываешься раскаяться?

Ты должен решать, а не я.

Говори же, что знаешь.

34Люди разумные скажут мне,

мудрецы, кто услышит меня:

35«От невежества говорит Иов,

нет в его речи разума».

36О, когда бы до конца был испытан Иов,

за ответы, достойные беззаконных!

37К греху своему приложил он бунт;

насмехаясь над нами, он бьет в ладоши

и слова против Бога множит.