Yobu 33 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 33:1-33

1“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga;

mutcherere khutu zonse zimene ndinene.

2Tsopano ndiyamba kuyankhula;

mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.

3Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama;

pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.

4Mzimu wa Mulungu wandiwumba,

mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.

5Mundiyankhe ngati mungathe;

konzekani tsopano kuti munditsutse.

6Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu;

nanenso ndinachokera ku dothi.

7Musachite mantha ndipo musandiope ayi,

Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.

8“Koma inu mwayankhula ine ndikumva,

ndamva mawu anuwo onena kuti,

9‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo;

ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.

10Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo;

Iye akundiyesa ngati mdani wake.

11Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo,

akulonda mayendedwe anga onse.’

12“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi,

pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.

13Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye

kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?

14Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana,

ngakhale munthu sazindikira zimenezi.

15Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku,

pamene anthu ali mʼtulo tofa nato

pamene akungosinza chabe pa bedi,

16amawanongʼoneza mʼmakutu

ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,

17kumuchotsa munthu ku zoyipa,

ndi kuthetseratu kunyada kwake,

18kumulanditsa munthu ku manda,

kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.

19“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake,

nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,

20kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya,

ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.

21Thupi lake limawonda

ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.

22Munthuyo amayandikira ku manda,

moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.

23“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi,

mmodzi mwa ambirimbiri oterewa,

adzafotokoza zimene zili zoyenera,

24kudzamukomera mtima ndi kunena kuti,

‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda;

ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’

25pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana;

ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.

26Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa.

Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe

ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.

27Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti,

‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama,

koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.

28Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda,

ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’

29“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu

kawirikawiri,

30kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda,

kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.

31“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere;

khalani chete kuti ndiyankhule.

32Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni;

yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.

33Koma ngati sichoncho, mundimvere;

khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

Ketab El Hayat

أيوب 33:1-33

1وَالآنَ يَا أَيُّوبُ أصْغِ إِلَى أَقْوَالِي، وَاسْمَعْ كَلامِي كُلَّهُ: 2هَا أَنَا قَدْ فَتَحْتُ فَمِي فَنَطَقَ لِسَانِي فِي حَنَكِي، 3كَلِمَاتِي تَصْدُرُ مِنْ قَلْبٍ مُسْتَقِيمٍ، وَشَفَتَايَ تَتَحَدَّثَانِ بِإِخْلاصٍ بِمَا أَعْلَمُ. 4رُوحُ اللهِ هُوَ الَّذِي كَوَّنَنِي، وَنَسَمَةُ الْقَدِيرِ أَحْيَتْنِي، 5فَأَجِبْنِي إِنْ كُنْتَ تَسْتَطِيعُ. أَحْسِنِ الدَّعْوَى، وَاتَّخِذْ لَكَ مَوْقِفاً. 6إِنَّمَا أَنَا نَظِيرُكَ أَمَامَ اللهِ، مِنَ الطِّينِ جُبِلْتُ، 7فَلا هَيْبَتِي تُخِيفُكَ، وَلا يَدِي ثَقِيلَةٌ عَلَيْكَ.

8حَقّاً قَدْ تَكَلَّمْتَ فِي أُذُنَيَّ فَاسْتَمَعْتُ إِلَى أَقْوَالِكَ. 9أَنْتَ قُلْتَ: أَنَا نَقِيٌّ بَرِيءٌ مِنْ كُلِّ ذَنْبٍ، أَنَا طَاهِرٌ لَا إِثْمَ فِيَّ، 10إِنَّمَا اللهُ يَتَرَبَّصُ بِي لِيَجِدَ عِلَّةً عَلَيَّ وَيَحْسِبَنِي عَدُوّاً لَهُ، 11يَضَعُ أَقْدَامِي فِي الْمِقْطَرَةِ، وَيَتَرَصَّدُ سُبُلِي.

12وَلَكِنَّكَ مُخْطِئٌ فِي هَذَا، وَأَنَا الَّذِي أُجِيبُكَ. إِنَّ اللهَ أَعْظَمُ مِنَ الإِنْسَانِ، 13فَمَا بَالُكَ تُخَاصِمُهُ قَائِلاً: إِنَّهُ لَنْ يُجِيبَ عَنْ تَسَاؤُلاتِي؟ 14إِنَّ اللهَ يَتَكَلَّمُ بِطَرِيقَةٍ أَوْ بِأُخْرَى وَإِنْ كَانَ الإِنْسَانُ لَا يُدْرِكُهَا. 15يَتَكَلَّمُ فِي حُلْمٍ، فِي رُؤْيَا اللَّيْلِ عِنْدَمَا يَغْشَى النَّاسَ سُبَاتٌ عَمِيقٌ. 16عِنْدَئِذٍ يَفْتَحُ آذَانَ النَّاسِ وَيُرْعِبُهُمْ بِتَحْذِيرَاتِهِ، 17لِيَصْرِفَ الإِنْسَانَ عَنْ خَطِيئَتِهِ وَيَسْتَأْصِلَ مِنْهُ الْكِبْرِيَاءَ، 18لِيُنْقِذَ نَفْسَهُ مِنَ الْهَاوِيَةِ وَحَيَاتَهُ مِنَ الْهَلاكِ بِحَدِّ السَّيْفِ.

19قَدْ يُقَوَّمُ الإِنْسَانُ بِالأَلَمِ عَلَى مَضْجَعِهِ، وَبِالأَوْجَاعِ النَّاشِبَةِ فِي عِظَامِهِ، 20حَتَّى تَعَافَ حَيَاتُهُ الطَّعَامَ، وَشَهِيَّتُهُ لَذِيذَ الْمَأْكَلِ. 21يَبْلَى لَحْمُهُ فَيَخْتَفِي عَنِ الْعَيَانِ، وَتَنْبَرِي عِظَامُهُ الَّتِي كَانَتْ خَافِيَةً مِنْ قَبْلُ. 22تَدْنُو نَفْسُهُ مِنَ الْهَاوِيَةِ، وَحَيَاتُهُ مِنْ زَبَانِيَةِ الْمَوْتِ. 23إِنْ وُجِدَ لَهُ مَلاكٌ، شَفِيعٌ، وَاحِدٌ مِنْ بَيْنِ أَلْفٍ، لِيُعْلِنَ لِلإِنْسَانِ مَا هُوَ صَالِحٌ لَهُ، 24يتَرَأَّفُ عَلَيْهِ قَائِلاً: أَنْقِذْهُ يَا رَبُّ مِنَ الانْحِدَارِ إِلَى الْهَاوِيَةِ، فَقَدْ وَجَدْتُ لَهُ فِدْيَةً. 25فَيَصِيرَ لَحْمُهُ أَكْثَرَ غَضَاضَةً مِن أَيَّامِ صِبَاهُ وَيَعُودَ إِلَى عَهْدِ رَيعَانِ شَبَابِهِ 26عِنْدَئِذٍ يَدْعُو الْمَرْءُ اللهَ فَيَرْضَى عَنْهُ، وَيَمْثُلُ فِي حَضْرَتِهِ بِفَرَحٍ، وَيَرُدُّ لَهُ اللهُ بِرَّهُ، 27ثُمَّ يُرَنِّمُ أَمَامَ النَّاسِ قَائِلاً: لَقَدْ أَخْطَأْتُ وَحَرَّفْتُ مَا هُوَ حَقٌّ وَلَمْ أُجَازَ عَلَيْهِ، 28قَدِ افْتَدَى اللهُ حَيَاتِي مِنَ الانْحِدَارِ إِلَى الْهَاوِيَةِ، فَتَنْتَعِشُ حَيَاتِي لِتَرَى النُّورَ.

29هَذَا كُلُّهُ يُجْرِيهِ اللهُ عَلَى الإِنْسَانِ مَرَّتَيْنِ وَثَلاثَ مَرَّاتٍ، 30لِيَرُدَّ نَفْسَهُ عَنِ الْهَاوِيَةِ لِيَسْتَضِيءَ بِنُورِ الْحَيَاةِ. 31فَأَصْغِ يَا أَيُّوبُ وَأَنْصِتْ إِلَيَّ. اُصْمُتْ وَدَعْنِي أَتَكَلَّمُ. 32وَإِنْ كَانَ لَدَيْكَ مَا تَقُولُهُ فَأَجِبْنِي، تَكَلَّمْ، فَإِنِّي أَرْغَبُ فِي تَبْرِيرِكَ. 33وَإلَّا فَأَصْغِ إِلَيَّ، أَنْصِتْ فَأُعَلِّمَكَ الْحِكْمَةَ».