Yobu 33 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 33:1-33

1“Koma tsopano, inu abambo Yobu chonde mverani mawu anga;

mutcherere khutu zonse zimene ndinene.

2Tsopano ndiyamba kuyankhula;

mawu anga ali pa msonga ya lilime langa.

3Mawu anga akuchokera mu mtima wolungama;

pakamwa panga pakuyankhula zoonadi zimene ndikuzidziwa.

4Mzimu wa Mulungu wandiwumba,

mpweya wa Wamphamvuzonse umandipatsa moyo.

5Mundiyankhe ngati mungathe;

konzekani tsopano kuti munditsutse.

6Ine ndili monga inu pamaso pa Mulungu;

nanenso ndinachokera ku dothi.

7Musachite mantha ndipo musandiope ayi,

Ine sindikupanikizani kwambiri ayi.

8“Koma inu mwayankhula ine ndikumva,

ndamva mawu anuwo onena kuti,

9‘Ndine wolungama mtima ndi wopanda tchimo;

ndine woyera mtima ndipo ndilibe cholakwa.

10Komatu Mulungu wapeza zifukwa zoti anditsutsire nazo;

Iye akundiyesa ngati mdani wake.

11Iyeyo wamanga mapazi anga mʼzigologolo,

akulonda mayendedwe anga onse.’

12“Koma ine ndi kuti kwa inu, inuyo simukukhoza pa zimenezi,

pakuti Mulungu ndi wamkulu kupambana munthu.

13Chifukwa chiyani mukudandaula kwa Iye

kuti sayankha mawu ena aliwonse a munthu?

14Pajatu Mulungu amayankhula mwa njira zosiyanasiyana,

ngakhale munthu sazindikira zimenezi.

15Mʼmaloto, mʼmasomphenya usiku,

pamene anthu ali mʼtulo tofa nato

pamene akungosinza chabe pa bedi,

16amawanongʼoneza mʼmakutu

ndi kuwaopseza ndi machenjezo ake,

17kumuchotsa munthu ku zoyipa,

ndi kuthetseratu kunyada kwake,

18kumulanditsa munthu ku manda,

kuti moyo wake usawonongeke ndi lupanga.

19“Mwina Mulungu amalanga munthu ndi matenda ndi ululu ali pa bedi pake,

nthawiyo thupi lake lonse limangophwanya,

20kuti asakhalenso ndi chilakolako cha chakudya,

ndipo amanyansidwa ndi chakudya chabwino chomwe.

21Thupi lake limawonda

ndipo mafupa ake, omwe anali obisika, tsopano amaonekera poyera.

22Munthuyo amayandikira ku manda,

moyo wake umayandikira kwa amene amabweretsa imfa.

23“Koma patakhala mngelo ngati mthandizi,

mmodzi mwa ambirimbiri oterewa,

adzafotokoza zimene zili zoyenera,

24kudzamukomera mtima ndi kunena kuti,

‘Mupulumutseni kuti asapite ku manda;

ine ndapeza cholowa mʼmalo mwa moyo wake,’

25pamenepo thupi lake lidzasanduka lasee ngati la mwana;

ndipo adzabwezeretsedwanso kukhala ngati mʼmasiku a unyamata wake.

26Akapemphera kwa Mulungu, iyeyo adzalandiridwa.

Mulungu adzamulandira mwa chimwemwe

ndipo adzamubwezeretsa pamalo ake oyamba.

27Ndipo adzabwera kwa anzake ndi kunena kuti,

‘Ndinachimwa ndipo sindinachite zolungama,

koma sindinalangidwe koyenerana ndi kuchimwa kwanga.

28Iye anapulumutsa moyo wanga kuti usapite ku manda,

ndipo ndidzakhala ndi moyo ndi kuonanso kuwala kwa dzuwa.’

29“Mulungu amachita zonsezi kwa munthu

kawirikawiri,

30kupulumutsa moyo wa munthuyo ku manda,

kuti athe kuonanso kuwala kwa moyo.

31“Abambo Yobu, tcherani khutu ndipo mundimvere;

khalani chete kuti ndiyankhule.

32Ngati muli nʼchoti munene, ndiyankheni;

yankhulani, pakuti ine ndikufuna mupezeke wolungama.

33Koma ngati sichoncho, mundimvere;

khalani chete ndipo ine ndidzakuphunzitsani nzeru.”

Hoffnung für Alle

Hiob 33:1-33

Gott spricht auf mancherlei Weise

1»Hiob, hör mir jetzt zu,

gib acht auf das, was ich dir sage!

2Meine Rede will ich nun beginnen.

Die Worte liegen mir schon auf der Zunge.

3Ich spreche mit aufrichtigem Herzen,

klar und wahr, und sage nur das, was ich weiß.

4Gottes Geist hat mich geschaffen,

der Atem des Allmächtigen hat mir das Leben geschenkt.

5Antworte mir nur, wenn du kannst,

bereite dich vor und tritt mir entgegen!

6Schau: Vor Gott, da sind wir beide gleich,

auch ich bin nur von Lehm genommen so wie du.

7Du brauchst keine Angst vor mir zu haben,

ich setze dich nicht unter Druck!

8Ich hörte zu, wie du geredet hast –

und ich habe die Worte noch im Ohr:

9›Rein bin ich, ohne jede Sünde;

unschuldig bin ich, kein Vergehen lastet auf mir!

10Doch Gott erfindet immer neue Vorwürfe gegen mich,

er betrachtet mich als seinen Feind!

11Er legt meine Füße in Ketten,

überwacht mich auf Schritt und Tritt.‹

12Doch ich muss dir sagen, Hiob,

dass du im Unrecht bist,

denn Gott ist größer als ein Mensch!

13Warum beschwerst du dich bei ihm,

dass er auf Menschenworte keine Antwort gibt?

14Gott spricht immer wieder,

auf die eine oder andere Weise,

nur wir Menschen hören nicht darauf!

15Gott redet durch Träume,

durch Visionen in der Nacht,

wenn tiefer Schlaf auf die Menschen fällt.

Sie liegen da und schlummern,

16doch dann lässt er sie aufhorchen

und erschreckt sie mit seiner Warnung.

17Gott will sie abbringen von bösem Tun,

und ihren Hochmut will er ihnen austreiben.

18Er will sie vor dem Tod bewahren,

davor, dass sie in ihr eigenes Verderben rennen.

19Gott weist einen Menschen auch durch Schmerzen zurecht,

wenn er daliegt in seinen Qualen

20und sich vor jeder Speise ekelt,

selbst vor seinem Lieblingsgericht.

21Seine Gestalt verfällt zusehends,

man kann alle seine Knochen zählen.

22Er steht schon mit einem Fuß im Grab,

bald holen ihn die Todesboten.

23Doch wenn ein Engel sich für ihn einsetzt,

einer von den Tausenden,

die den Menschen sagen, was richtig für sie ist,

24wenn dieser Engel Mitleid mit ihm hat

und zu Gott sagt: ›Verschone ihn!

Lass ihn nicht sterben! Hier ist das Lösegeld!‹,

25dann blüht er wieder auf,

wird gesund und frisch,

er wird stark wie damals in seiner Jugend.

26Dann betet er zu Gott,

und sein Gebet wird gnädig angenommen.

Mit lautem Jubel tritt er vor ihn hin

und dankt dafür, dass Gott ihn wieder von seiner Schuld freispricht.

27Offen bekennt er den Menschen:

›Ich hatte gesündigt und das Recht missachtet,

doch Gott hat mir’s nicht angerechnet!

28Er hat mich vor dem sicheren Tod bewahrt,

nun darf ich weiterleben und sehe das Licht.‹

29Das alles tut Gott mehr als nur einmal im Leben eines Menschen,

30um ihn vor dem Tod zu bewahren

und ihm das Licht des Lebens zu erhalten.

31Hör mir zu, Hiob,

sei still und lass mich reden!

32Wenn du jetzt noch etwas zu sagen hast,

dann antworte mir!

Rede nur, denn ich würde dir gerne recht geben.

33Wenn du aber nichts mehr zu sagen weißt,

dann schweig und hör mir zu,

ich will dir zeigen, was Weisheit ist.«