Yobu 32 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 32:1-22

Mawu a Elihu

1Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama. 2Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga. 3Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa. 4Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo. 5Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

6Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

“Ine ndine wamngʼono,

inuyo ndinu akuluakulu,

nʼchifukwa chake ndimaopa,

ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.

7Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;

anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’

8Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,

mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.

9Si okalamba amene ali ndi nzeru,

si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.

10“Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;

inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’

11Ndadikira nthawi yonseyi,

ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula,

pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,

12ineyo ndinakumvetseranidi.

Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu;

palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.

13Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;

Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’

14Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,

ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.

15“Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;

mawu awathera.

16Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,

pakuti angoyima phee wopanda yankho?

17Inenso ndiyankhulapo tsopano;

nanenso ndinena zimene ndikudziwa.

18Pakuti ndili nawo mawu ambiri,

ndipo mtima wanga ukundikakamiza;

19mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,

ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.

20Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;

ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.

21Sindidzakondera munthu wina aliyense,

kapena kuyankhula zoshashalika,

22pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,

Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

New International Reader’s Version

Job 32:1-22

The Speech of Elihu

1So the three men stopped answering Job, because he thought he was right. 2But Elihu the Buzite was very angry with Job. That’s because Job said he himself was right instead of God. Elihu was the son of Barakel. He was from the family of Ram. 3Elihu was also very angry with Job’s three friends. They hadn’t found any way to prove that Job was wrong. But they still said he was guilty. 4Elihu had waited before he spoke to Job. That’s because the others were older than he was. 5But he saw that the three men didn’t have anything more to say. So he was very angry.

6Elihu the Buzite, the son of Barakel, said,

“I’m young, and you are old.

So I was afraid to tell you what I know.

7I thought, ‘Those who are older should speak first.

Those who have lived for many years

should teach people how to be wise.’

8But the spirit in people gives them understanding.

The breath of the Mighty One gives them wisdom.

9Older people aren’t the only ones who are wise.

They aren’t the only ones who understand what is right.

10“So I’m saying you should listen to me.

I’ll tell you what I know.

11I waited while you men spoke.

I listened to your reasoning.

While you were searching for words,

12I paid careful attention to you.

But not one of you has proved that Job is wrong.

None of you has answered his arguments.

13Don’t claim, ‘We have enough wisdom to answer Job.’

Let God, not a mere man, prove that he’s wrong.

14Job hasn’t directed his words against me.

I won’t answer him with your arguments.

15“Job, these men are afraid.

They don’t have anything else to say.

They’ve run out of words.

16Do I have to keep on waiting, now that they are silent?

They are just standing there with nothing to say.

17I too have something to say.

I too will tell what I know.

18I’m full of words.

My spirit inside me forces me to speak.

19Inside I’m like wine that is bottled up.

I’m like new wineskins ready to burst.

20I must speak so I can feel better.

I must open my mouth and reply.

21I’ll treat everyone the same.

I won’t praise anyone without meaning it.

22If I weren’t honest when I praised people,

my Maker would soon take me from this life.