Yobu 31 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 31:1-40

1“Ndinachita pangano ndi maso anga

kuti sindidzapenya namwali momusirira.

2Kodi Mulungu kumwambako wandisungira zotani?

Kodi cholowa changa chochokera kwa Wamphamvuzonse kumwambako nʼchotani?

3Kodi si chiwonongeko kwa anthu oyipa,

tsoka kwa iwo amene amachita zolakwa?

4Kodi Mulungu saona zochita zanga,

ndi kudziwa mayendedwe anga?

5“Ngati ndachita zinthu mwachiphamaso,

kapena kufulumira kukachita zachinyengo,

6Mulungu andiyeze ndi muyeso wake wolungama

ndipo Iye adzadziwa kuti ine ndine wosalakwa,

7ngati mayendedwe anga asempha njira,

ngati mtima wanga wakhumbira zimene maso anga aona,

kapena ngati ndachita choyipa chilichonse.

8Pamenepo ena adye zimene ndinadzala,

ndipo zomera zanga zizulidwe.

9“Ngati mtima wanga unakopekapo ndi mkazi,

ndipo ngati ndinalakalaka mkazi wa mnansi wanga,

10pamenepo mkazi wanga aphikire mwamuna wina chakudya,

ndipo amuna ena azigona naye.

11Pakuti zimenezo zikanakhala zochititsa manyazi,

tchimo loyenera kulangidwa nalo.

12Ndi moto umene umayaka mpaka chiwonongeko;

ukanapsereza zokolola zanga.

13“Ngati ndinkapondereza mlandu wa akapolo anga aamuna kapena aakazi,

pamene ankabwera kwa ine ndi milandu yawo,

14ndidzatani pamene Mulungu adzanditsutsa?

Nanga ndidzayankha chiyani akadzandifunsa?

15Kodi amene anapanga ine mʼmimba mwa amayi anga si yemwe anapanganso iwo?

Kodi si mmodzi yemweyo amene anatipanga tonsefe mʼmimba mwa amayi athu?

16“Ngati ndinawamana aumphawi zinthu zimene ankazikhumba,

kapena kuwagwiritsa fuwa lamoto akazi amasiye amene amafuna thandizo kwa ine,

17ngati chakudya changa ndinadya ndekha,

wosagawirako mwana wamasiye,

18chonsechotu kuyambira unyamata wanga ndinamulera monga abambo ake,

ndipo moyo wanga wonse ndakhala ndikusamalira akazi amasiye,

19ngati ndinaona wina aliyense akuzunzika ndi usiwa,

kapena munthu wosauka alibe chofunda,

20ndipo ngati iyeyo sananditamandepo

chifukwa chomufunditsa ndi nsalu ya ubweya wankhosa,

21ngati ndinaopsezapo mwana wamasiye,

poganiza kuti ndinali ndi mphamvu mʼbwalo la milandu,

22pamenepo phewa langa lipokonyeke,

mkono wanga ukonyoke polumikizira pake.

23Popeza ine ndinaopa kwambiri chiwonongeko chochokera kwa Mulungu,

ndinachitanso mantha ndi ulemerero wake, sindikanatha kuchita zinthu zimenezi.

24“Ngati ndinayika mtima wanga pa chuma

kapena kunena kwa golide wabwino kwambiri kuti, ‘Iwe ndiye chitetezo changa,’

25ngati ndinakondwera chifukwa choti chuma changa chinali chambiri,

zinthu zimene manja anga anazipeza,

26ngati pamene ndinaona dzuwa likuwala,

kapena mwezi ukuyenda mwa ulemerero wake,

27ndipo kuti mtima wanga unakopeka nazo

nʼkuyika dzanja langa pakamwa mozilemekeza,

28pamenepo zimenezinso zikanakhala machimo oti ndilangidwe nawo,

chifukwa ndikanakhala wosakhulupirika kwa Mulungu wakumwamba.

29“Ngati ndinasangalala ndi kuwonongeka kwa mdani wanga,

kapena kusekera mavuto pamene mavuto anamugwera,

30ine sindinachimwe ndi pakamwa panga

potulutsa matemberero a mdani wanga kuti awonongeke,

31ngati anthu amene ndimakhala nawo mʼnyumba mwanga sananenepo kuti,

‘Kodi ndani amene sakhuta ndi chakudya cha Yobu?’

32Komatu mlendo sindinamusiye pa msewu usiku wonse,

pakuti khomo langa linali lotsekuka nthawi zonse kwa alendo,

33ngati ndinabisa tchimo langa monga amachitira anthu ena,

kubisa kulakwa mu mtima mwanga

34chifukwa choopa gulu la anthu,

ndi kuchita mantha ndi mnyozo wa mafuko

kotero ndinakhala chete ndipo sindinatuluke panja.

35“Aa, pakanakhala wina wondimva!

Tsopano ndikutsiriza mawu anga odzitetezera. Wamphamvuzonse andiyankhe;

mdani wanga achite kulemba pa kalata mawu ake ondineneza.

36Ndithu ine ndikanakoleka kalatayo pa phewa langa,

ndikanayivala kumutu ngati chipewa chaufumu.

37Ndikanamufotokozera zonse zimene ndinachita;

ndikanafika pamaso pake ngati kalonga.

38“Ngati minda yanga ikulira monditsutsa ine

ndipo malo ake onse osalimidwa anyowa ndi misozi,

39ngati ndinadya za mʼminda mwake osapereka ndalama

kapena kukhumudwitsa anthu olima mʼmindamo,

40pamenepo mʼmindamo mumere namsongole mʼmalo mwa tirigu

ndi udzu mʼmalo mwa barele.”

Mawu a Yobu athera pano.

New International Reader’s Version

Job 31:1-40

1“I made an agreement with my eyes.

I promised not to look at a young woman with impure thoughts.

2What do we receive from God above?

What do we get from the Mighty One in heaven?

3Sinful people are destroyed.

Trouble comes to those who do what is wrong.

4Doesn’t God see how I live?

Doesn’t he count every step I take?

5“I haven’t told any lies.

My feet haven’t hurried to cheat others.

6So let God weigh me in honest scales.

Then he’ll know I haven’t done anything wrong.

7Suppose my steps have turned away from the right path.

Suppose my heart has wanted what my eyes have seen.

Or suppose my hands have become ‘unclean.’

8Then may others eat what I’ve planted.

May my crops be pulled up by the roots.

9“Suppose my heart has been tempted by a woman.

Or suppose I’ve prowled around my neighbor’s home.

10Then may my wife grind another man’s grain.

May other men sleep with her.

11Wanting another woman would have been an evil thing.

It would have been a sin that should be judged.

12It’s like a fire that burns down to the grave.

It would have caused my crops to be pulled up by the roots.

13“Suppose I haven’t treated any of my male and female servants fairly

when they’ve brought charges against me.

14Then what will I do when God opposes me?

What answer will I give him

when he asks me to explain myself?

15Didn’t he who made me make my servants also?

Didn’t the same God form us inside our mothers?

16“I haven’t said no to what poor people have wanted.

I haven’t let widows lose their hope.

17I haven’t kept my bread to myself.

I’ve shared it with children whose fathers had died.

18From the time I was young, I’ve helped those widows.

I’ve raised those children as a father would.

19Suppose I’ve seen people dying

because they didn’t have enough clothes.

I’ve seen needy people

who didn’t have enough to keep warm.

20And they didn’t give me their blessing

when I warmed them with wool from my sheep.

21Suppose I’ve raised my hand

against children whose fathers have died.

And I did it because I knew

I had power in the courts.

22Then let my arm fall from my shoulder.

Let it be broken off at the joint.

23I was afraid God would destroy me.

His glory terrifies me.

So I’d never do things like that.

24“Suppose I’ve put my trust in gold.

I’ve said to pure gold, ‘You make me feel secure.’

25And I’m happy because I’m so wealthy.

I’m glad because my hands have earned so much.

26Suppose I’ve worshiped the sun in all its glory.

I’ve bowed down to the moon in all its beauty.

27My heart has been secretly tempted.

My hand has thrown kisses to the sun and moon.

28Then these things would have been sins that should be judged.

And I wouldn’t have been faithful to God in heaven.

29“I wasn’t happy when hard times came to my enemies.

I didn’t enjoy seeing the trouble they had.

30I didn’t allow my mouth to sin

by asking for bad things to happen to them.

31The workers in my house always said,

‘Job always gives plenty of food to everyone.’

32No stranger ever had to spend the night in the street.

My door was always open to travelers.

33I didn’t hide my sin as other people do.

I didn’t hide my guilt in my heart.

34I was never afraid of the crowd.

I never worried that my relatives might hate me.

I didn’t have to keep quiet or stay inside.

35“I wish someone would listen to me!

I’m signing my name to everything I’ve said.

I hope the Mighty One will give me his answer.

I hope the one who brings charges against me will write them down.

36I’ll wear them on my shoulder.

I’ll put them on my head like a crown.

37I’ll give that person a report of every step I take.

I’ll present it to him like I would to a ruler.

38“Suppose my land cries out against me.

And all its soil is wet with tears.

39Suppose I’ve used up its crops without paying for them.

Or I’ve broken the spirit of its renters.

40Then let thorns grow instead of wheat.

Let stinkweed come up instead of barley.”

The words of Job end here.