Yobu 27 – CCL & NAV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 27:1-23

1Ndipo Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

2“Ndithu pali Mulungu wamoyo, amene wakana kundiweruza molungama,

Wamphamvuzonse, amene wawawitsa mtima wanga,

3nthawi zonse pamene ndili ndi moyo,

mpweya wa Mulungu uli mʼmphuno mwanga,

4pakamwa panga sipadzatuluka mawu oyipa,

lilime langa silidzayankhula zachinyengo.

5Sindidzavomereza kuti inu mukunena zoona;

mpaka imfa yanga, sindidzataya ungwiro wanga.

6Ndidzasunga chilungamo changa ndipo sindidzalola kuti chindichokere;

chikumbumtima changa sichidzanditsutsa nthawi yonse ya moyo wanga.

7“Mdani wanga akhale ngati woyipa,

wondiwukira akhale ngati munthu wosalungama!

8Nanga chiyembekezo cha munthu wosapembedza nʼchiyani pamene aphedwa,

pamene Mulungu achotsa moyo wake?

9Kodi Mulungu amamva kulira kwake

pamene zovuta zamugwera?

10Kodi adzapeza chikondwerero mwa Wamphamvuzonse?

Kodi adzapemphera kwa Mulungu nthawi zonse?

11“Ndidzakuphunzitsani za mphamvu ya Mulungu ndipo

sindidzabisa njira za Wamphamvuzonse.

12Inu mwadzionera nokha zonsezi.

Nanga bwanji mukuyankhula zopanda pake?

13“Pano pali chilango chimene Mulungu amasungira woyipa,

cholowa chimene munthu wankhanza amalandira kuchokera kwa Wamphamvuzonse.

14Angakhale ana ake achuluke chotani adzaphedwa ndi lupanga ndipo

zidzukulu zake zidzasowa zakudya.

15Amene adzatsalireko adzafa ndi mliri,

ndipo akazi awo amasiye sadzawalira.

16Ngakhale aunjike siliva ngati fumbi,

ndi kukundika zovala ngati mchenga,

17zimene wasungazo wolungama ndiye adzavale,

ndipo anthu osalakwa ndiwo adzagawane siliva wakeyo.

18Nyumba imene akuyimanga ili ngati mokhala kadziwotche,

ili ngati msasa umene mlonda amamanga.

19Amapita kokagona ali wolemera koma kutha kwake nʼkomweko;

akatsekula maso ake, chuma chake chonse chapita.

20Zoopsa zimamukokolola ngati madzi achigumula;

mphepo yamkuntho imamunyamula usiku.

21Mphepo ya kummawa imamuwulutsa ndipo iye saonekanso ndipo

imamuchotsa pamalo pake.

22Imakuntha pa iye osamuchitira chisoni,

pamene akuyesa kuthawa mphamvu zake mwaliwiro.

23Mphepoyo imamuwomba ndithu

ndipo kuchokera pamalo pake imamuopseza.”

Ketab El Hayat

أيوب 27:1-23

كلمات أيوب الأخيرة لأصدقائه

1وَاسْتَطْرَدَ أَيُّوبُ يَضْرِبُ مَثَلَهُ قَائِلاً: 2«حَيٌّ هُوَ اللهُ الَّذِي نَزَعَ حَقِّي، وَالْقَدِيرُ الَّذِي أَمَرَّ حَيَاتِي، 3وَلَكِنْ مَادَامَتْ نَسَمَتِي فِيَّ، وَنَفْخَةُ اللهِ فِي أَنْفِي، 4فَإِنَّ شَفَتَيَّ لَنْ تَنْطِقَا بِالسُّوءِ، وَلِسَانِي لَنْ يَتَلَفَّظَ بِالْغِشِّ. 5حَاشَا لِي أَنْ أُقِرَّ بِصَوَابِ أَقْوَالِكُمْ، وَلَنْ أَتَخَلَّى عَنْ كَمَالِي حَتَّى الْمَوْتِ. 6أَتَشَبَّثُ بِبِرِّي وَلَنْ أَرْخِيَهُ، لأَنَّ ضَمِيرِي لَا يُؤَنِّبُنِي عَلَى يَوْمٍ مِنْ أَيَّامِي.

7لِيَكُنْ عَدُوِّي نَظِيرَ الشِّرِّيرِ، وَمُقَاوِمِي كَالْفَاجِرِ، 8إِذْ مَا هُوَ رَجَاءُ الْفَاجِرِ عِنْدَمَا يَسْتَأْصِلُهُ اللهُ وَيُزْهِقُ أَنْفَاسَهُ؟ 9هَلْ يَسْتَمِعُ اللهُ إِلَى صَرْخَتِهِ إِذَا حَلَّ بِهِ ضِيقٌ؟ 10هَلْ يُسَرُّ بِالْقَدِيرِ وَيَسْتَغِيثُ بِهِ فِي كُلِّ الأَزْمِنَةِ؟

11إِنِّي أُعَلِّمُكُمْ عَنْ قُوَّةِ اللهِ، وَلا أَكْتُمُ عَنْكُمْ مَا لَدَى الْقَدِيرِ. 12فَأَنْتُمْ جَمِيعاً قَدْ عَايَنْتُمْ ذَلِكَ بِأَنْفُسِكُمْ، فَمَا بَالُكُمْ تَنْطِقُونَ بِالْبَاطِلِ قَائِلِينَ: 13هَذَا هُوَ نَصِيبُ الشِّرِّيرِ عِنْدَ اللهِ وَالْمِيرَاثُ الَّذِي يَنَالُهُ الظَّالِمُ مِنَ الْقَدِيرِ. 14إِنْ تَكَاثَرَ بَنُوهُ فَلِيَكُونُوا طَعَاماً لِلسَّيْفِ، وَنَسْلُهُ لَا يَشْبَعُ خُبْزاً. 15ذُرِّيَّتُهُ تَمُوتُ بِالْوَبَأِ، وَأَرَامِلُهُمْ لَا تَنُوحُ عَلَيْهِمْ. 16إِنْ جَمَعَ فِضَّتَهُ كَأَكْوَامِ التُّرَابِ، وَكَوَّمَ مَلابِسَ كَالطِّينِ، 17فَإِنَّ مَا يُعِدُّهُ مِنْ ثِيَابٍ يَرْتَدِيهِ الصِّدِّيقُ، وَالْبَرِيءُ يُوَزِّعُ الْفِضَّةَ. 18يَبْنِي بَيْتَهُ كَبَيْتِ الْعَنْكَبُوتِ، أَوْ كَمَظَلَّةٍ صَنَعَهَا حَارِسُ الْكُرُومِ. 19يَضْطَجِعُ غَنِيًّا وَيَسْتَيْقِظُ مُعْدَماً. يَفْتَحُ عَيْنَيْهِ وَإذَا بِثَرْوَتِهِ قَدْ تَلاشَتْ. 20يَطْغَى عَلَيْهِ رُعْبٌ كَفَيَضَانٍ، وَتَخْطِفُهُ فِي اللَّيْلِ زَوْبَعَةٌ. 21تُطَوِّحُ بِهِ الرِّيحُ الشَّرْقِيَّةُ فَيَخْتَفِي وَتَقْتَلِعُهُ مِنْ مَكَانِهِ. 22تُطْبِقُ عَلَيْهِ مِنْ غَيْرِ رَحْمَةٍ وَهُوَ هَارِبٌ مِنْ وَجْهِ عُنْفُوانِهَا. 23تُصَفِّرُ الرِّيحُ عَلَيْهِ، وَتُرْعِبُهُ بِقُوَّتِهَا الْمُدَمِّرَةِ.