Yobu 26 – CCL & BDS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yobu 26:1-14

Mawu a Yobu

1Pamenepo Yobu anayankha kuti,

2“Wamuthandizadi munthu wopanda mphamvu!

Walimbitsadi dzanja la munthu wofowoka!

3Wapereka malangizo kwa munthu amene alibe nzeru!

Ndipotu waonetsadi nzeru zochuluka!

4Kodi wakuthandiza ndani kuti uyankhule mawu awa?

Ndipo ndi mzimu wa yani umene unayankhula pakamwa pako?

5“Mizimu ya anthu akufa ikunjenjemera pansi pa madzi,

ndi zonse zokhala mʼmadzimo.

6Dziko la anthu akufa ndi lapululu pamaso pa Mulungu;

chiwonongeko ndi chosaphimbidwa.

7Mulungu anayala thambo la kumpoto pa phompho;

Iye anakoloweka dziko lapansi mʼmalo mwake pamene panali popanda nʼkanthu komwe.

8Amasunga madzi ambiri mʼmitambo yake,

koma mitamboyo siphulika chifukwa cha kulemera kwa madziwo.

9Iye amaphimba mwezi wowala,

amawuphimba ndi mitambo yake.

10Mulungu anawalembera madzi malire wonga uta,

kukhala malire pakati pa kuwunika ndi mdima.

11Mizati yochirikiza mitambo yakumwamba imanjenjemera,

ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.

12Ndi mphamvu zake anatontholetsa nyanja;

ndi nzeru zake anakantha chirombo cha mʼmadzi chija chotchedwa Rahabe.

13Ndi mpweya wake anayeretsa zamumlengalenga,

dzanja lake linapha chinjoka chothawa chija.

14Zimenezi ndi pangʼono chabe mwa ntchito yake;

tingomva pangʼono za Iye ngati kunongʼona!

Kodi ndani angathe kudziwa kukula kwa mphamvu zake?”

La Bible du Semeur

Job 26:1-14

Réponse de Job à Bildad

On ne connaît ni ne comprend l’œuvre de Dieu

1Alors Job prit la parole et dit :

2Ah, comme tu sais bien ╵aider l’homme sans force,

et secourir le bras ╵qui n’a plus de vigueur !

3Quel bon conseil tu donnes ╵à celui qui se trouve ╵dépourvu de sagesse,

et comme tu répands ╵la science à profusion !

4Mais à qui donc, dis-moi, ╵s’adressent tes discours ?

De quelle inspiration ╵émanent tes paroles ?

5Tous ceux qui sont morts tremblent

bien au-dessous des mers ╵et des êtres qui les habitent,

6car le séjour des morts ╵est à nu devant Dieu,

et le royaume des défunts26.6 En hébreu : Abaddôn, c’est-à-dire le lieu de destruction. Dans Ap 9.11, c’est le nom de l’ange de l’abîme. ╵n’a rien pour se couvrir.

7Il étend sur le vide ╵la région de l’Arctique

et il suspend la terre ╵au-dessus du néant.

8Il enserre les eaux ╵dans ses nuées épaisses,

mais jamais, sous leur poids, ╵les nuages n’éclatent.

9Il a couvert d’un voile ╵la face de son trône

en étendant sur lui ╵son épaisse nuée.

10Il a tracé un cercle ╵sur la face des eaux,

au lieu où la lumière ╵rencontre les ténèbres.

11Les colonnes du ciel ╵sont ébranlées,

épouvantées, ╵à sa menace.

12Par sa puissance, ╵il agite la mer ;

par son intelligence, ╵il en brise le monstre26.12 Voir v. 13 ; 3.8 et note. Autre traduction : il en brise l’orgueil (voir 9.13 et note)..

13Sous l’effet de son souffle, ╵le ciel devient serein.

Quant au serpent fuyard26.13 Voir Es 27.1 et note., ╵sa main l’a transpercé.

14Cependant, ce n’est là ╵qu’une infime partie ╵de ce qu’il accomplit,

dont nous ne percevons ╵qu’un murmure léger.

Qui pourra donc comprendre ╵les éclats de tonnerre ╵de sa puissance ?